< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Ovo je povijest Noinih sinova: Šema, Hama i Jafeta, kojima su se rodili sinovi poslije Potopa.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
Sinovi su Jafetovi: Gomer, Magog, Madaj, Javan, Tubal, Mešak, Tiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
A sinovi su Gomerovi: Aškenaz, Rifat i Togarma.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
Javanovi su opet sinovi: Eliša, Taršiš, Kitijci i Dodanci.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
Od njih su se razgranali narodi po otocima. To su Jafetovi sinovi prema svojim zemljama - svaki s vlastitim jezikom - prema svojim plemenima i narodima.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
Sinovi su Hamovi: Kuš i Misrajim, Put i Kanaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
Kuševi su: Seba, Havila, Sabta, Rama i Sabteka. Ramini su: Šeba i Dedan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
Od Kuša se rodio Nimrod, koji je postao prvi velmoža na zemlji.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
Voljom Jahve bio je silan lovac. Zato se veli: “Kao Nimrod, silan lovac voljom Jahve.”
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
Glavno uporište njegova kraljevstva bili su: Babilon, Erek, Akad i Kalne, svi u zemlji Šinearu.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
Iz ove je zemlje došao Ašur. On je podigao Ninivu, Rehobot Ir, Kalah
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
i Resen između Ninive i Kalaha (to je glavni grad).
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
Od Misrajima potekli su Ludijci, Anamijci, Lehabijci, Naftuhijci,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
pa Patrušani, Kasluhijci i Kaftorci, od kojih su potekli Filistejci.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
Od Kanaana potječe Sidon, njegov prvenac, i Het.
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
Dalje: Jebusejci, Amorejci, Girgašani,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
Hivijci, Arkijci, Sinijci,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
Arvađani, Semarjani i Hamaćani. Poslije se kanaanska plemena razgranaše,
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
tako da se granica Kanaanaca protezala od Sidona prema Geraru sve do Gaze pa prema Sodomi, Gomori, Admi i Sebojimu sve do Leše.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
To su sinovi Hamovi prema svojim plemenima i jezicima, po svojim zemljama i narodima.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
A i Šemu - praocu svih sinova Eberovih i starijem bratu Jafetovu - rodili se sinovi.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
Šemovi su sinovi: Elam, Ašur, Arpakšad, Lud i Aram.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
A Aramovi su sinovi: Us, Hul, Geter i Maš.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
Arpakšad rodi Šelaha, Šelah rodi Ebera.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
Eberu su se rodila dva sina: jednomu bješe ime Peleg, jer se za njegova vijeka zemlja razdijelila. Njegovu je bratu bilo ime Joktan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
Od Joktana se rodiše: Almodad, Šelef, Hasarmavet, Jerah,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
Hadoram, Uzal, Dikla,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
Obal, Abimael, Šeba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
Ofir, Havila i Jobab. Sve su to sinovi Joktanovi.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
Njihova se naselja protezahu od Meše sve do Sefara, brdovitih krajeva na istoku.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
To su sinovi Šemovi prema svojim plemenima, jezicima i zemljama, po svojim narodima.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
To su rodovi Noinih sinova prema svojim lozama i narodima. Od njih su se razgranali narodi po zemlji poslije Potopa.

< Genesis 10 >