+ Genesis 1 >
1 Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Iesākumā Dievs radīja debesis un zemi.
2 Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
Un zeme bija tumša un tukša, un tumsa bija pār dziļumiem, un Dieva Gars lidinājās pa ūdeņu virsu.
3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
Un Dievs sacīja: Lai top gaisma. Tad tapa gaisma.
4 Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
Un Dievs redzēja gaismu labu esam. Un Dievs šķīra gaismu no tumsas.
5 Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
Un Dievs nosauca gaismu par dienu, un tumsu Viņš nosauca par nakti. Un tapa vakars un tapa rīts, pirmā diena.
6 Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
Tad Dievs sacīja: Lai top izplatījums ūdeņu starpā un lai tas šķir ūdeni no ūdens.
7 Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
Un Dievs darīja izplatījumu, un darīja starpu to ūdeni, kas izplatījuma apakšā, un to ūdeni, kas izplatījuma virsū; un tā notika.
8 Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
Un Dievs nosauca izplatījumu par debesi. Un tapa vakars un tapa rīts, otra diena.
9 Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
Tad Dievs sacīja: Lai ūdens debess apakšā krājās vienā vietā, ka sausums top redzams; un tā notika.
10 Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Un Dievs nosauca sausumu par zemi, un to ūdeņu krājumu Viņš nosauca par jūru. Un Dievs redzēja to labu esam.
11 Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
Un Dievs sacīja: Lai zeme izdod zaļumu un zāli, kas savu sēklu nes, auglīgus kokus, kas augļus nes pēc savas kārtas, kam sava sēkla iekš sevis ir virs zemes; un tā notika.
12 Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Un zeme izdeva zaļumu un zāli, kas savu sēklu nes pēc savas kārtas, un kokus, kas augļus nes, kam sava sēkla iekš sevis pēc savas kārtas. Un Dievs redzēja to labu esam.
13 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
Un tapa vakars un tapa rīts, trešā diena.
14 Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
Tad Dievs sacīja: Lai top spīdekļi debess izplatījumā, kas šķir dienu no nakts un kas dod zīmes un laikus un dienas un gadus;
15 zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
Un lai tie ir par spīdekļiem debess izplatījumā un spīd virs zemes; un tā notika.
16 Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
Un Dievs darīja divus lielus spīdekļus, lielāko spīdekli, dienu valdīt un mazāko spīdekli, naktī valdīt, - un zvaigznes.
17 Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
Un Dievs tos lika debess izplatījumā, lai tie spīd uz zemi.
18 kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Un valda dienu un nakti un šķir gaismu no tumsas. Un Dievs redzēja to labu esam.
19 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
Un tapa vakars un tapa rīts, ceturtā diena.
20 Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
Tad Dievs sacīja: Lai pa pulkiem rodas ūdenī kustošas dzīvas dvašas un putni, kas virs zemes skrien apakš debess izplatījuma.
21 Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Un Dievs radīja lielus jūras zvērus un visādas dzīvas dvašas, kas lien, ko ūdens pa pulkiem izdod pēc viņu kārtām, un visādus spārnainus putnus pēc viņu kārtas. Un Dievs redzēja to labu esam.
22 Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
Un Dievs tos svētīja sacīdams: Vaislojaties un vairojaties un piepildiet ūdeni jūrā, un putni lai vairojās virs zemes.
23 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
Un tapa vakars un tapa rīts, piektā diena.
24 Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
Tad Dievs sacīja: Lai zeme izdod dzīvas dvašas pēc viņu kārtas, lopus, tārpus un zemes zvērus pēc viņu kārtas; un tā notika.
25 Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Un Dievs darīja zemes zvērus pēc viņu kārtas un lopus pēc viņu kārtas un visādus zemes tārpus pēc viņu kārtas. Un Dievs redzēja to labu esam.
26 Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
Un Dievs sacīja: Darīsim cilvēkus pēc mūsu ģīmja, pēc mūsu līdzības, lai tie valda pār zivīm jūrā un pār putniem apakš debess un pār lopiem un pār visu zemi un pār visiem tārpiem, kas lien virs zemes.
27 Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
Un Dievs radīja cilvēku pēc Sava ģīmja, pēc Dieva ģīmja Viņš to radīja, un radīja tos, vīrieti un sievieti.
28 Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
Un Dievs tos svētīja, un Dievs uz tiem sacīja: Augļojaties un vairojaties un piepildiet zemi un pārvaldiet to un valdat pār zivīm jūrā un pār putniem apakš debess un pār visām dvašām, kas lien virs zemes.
29 Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
Un Dievs sacīja: Redzi, Es jums esmu devis visādu zāli, kas nes sēklu, kas ir pa visu zemes virsu, un visus kokus, kam savi augļi iekš sevis un kas nes sēklu, jums par ēdamo.
30 Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
Un visiem zvēriem virs zemes un visiem putniem apakš debess un visiem tārpiem virs zemes, kam dzīva dvaša, esmu devis visādu zaļu zāli par barību. Un tā notika.
31 Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.
Un Dievs uzlūkoja visu, ko Viņš bija darījis, un redzi, tas bija ļoti labs. Un tapa vakars un tapa rīts, sestā diena.