< Agalatiya 1 >

1 Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
Pál, apostol (nem emberektől, sem nem ember által, hanem Jézus Krisztus által és az Atya Isten által, aki feltámasztotta őt a halálból);
2 pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
és a velem levő összes atyafiak, Galácia gyülekezeteinek:
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
Kegyelem néktek és békesség az Atya Istentől és a mi Urunk Jézus Krisztustól,
4 Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
aki adta önmagát a mi bűneinkért, hogy kiszabadítson minket e jelenvaló gonosz világból, az Istennek és a mi Atyánknak akarata szerint, (aiōn g165)
5 Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
akinek dicsőség örökkön-örökké! Ámen. (aiōn g165)
6 Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
Csodálkozom, hogy attól, aki titeket Krisztus kegyelme által elhívott, ily hamar más evangéliumra hajlotok.
7 umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
Holott nincs más; de némelyek zavarnak titeket, és el akarják ferdíteni a Krisztus evangéliumát.
8 Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
De ha akár mi avagy mennyből való angyal hirdetne is néktek valamit azon kívül, amit néktek hirdettünk, legyen átok.
9 Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
Amint előbb mondottuk, most is ismét mondom: Ha valaki néktek hirdet valamit azon kívül, amit elfogadtatok, átok legyen.
10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
Mert most embereknek engedek-e avagy az Istennek? Vagy embereknek igyekezem-e tetszeni? Bizonyára, ha még embereknek igyekeznék tetszeni, nem volnék Krisztus szolgája.
11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
Tudtotokra adom pedig, atyámfiai, hogy az az evangélium, melyet én hirdettem, nem ember szerint való,
12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
mert én sem embertől vettem azt, sem nem tanítottak arra, hanem a Jézus Krisztus kijelentése által.
13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
Mert hallottátok, mint forgolódtam én egykor a zsidóságban, hogy én igen nagyon háborgattam az Isten anyaszentegyházát, és pusztítottam azt.
14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
És felülmúltam a zsidóságban nemzetembeli sok kortársamat, szerfelett rajongva atyai hagyományaimért.
15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
De mikor az Istennek tetszett, ki elválasztott engem az én anyám méhétől fogva, és elhívott az ő kegyelme által,
16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
hogy kijelentse az ő Fiát énbennem, hogy hirdessem őt a pogányok között: azonnal nem tanácskoztam testtel és vérrel,
17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
sem nem mentem Jeruzsálembe az előttem való apostolokhoz, hanem elmentem Arábiába, és ismét visszatértem Damaszkuszba.
18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
Azután három esztendő múlva fölmentem Jeruzsálembe, hogy Pétert meglátogassam, és nála maradtam tizenöt napig.
19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
Az apostolok közül pedig mást nem láttam, hanem csak Jakabot, az Úr testvérét.
20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
Amiket pedig néktek írok, ím Isten előtt mondom, hogy nem hazudom.
21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
Azután mentem Szíriának és Ciliciának tartományaiba.
22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
Személyesen pedig ismeretlen voltam a Júdeában levő keresztyén gyülekezetek előtt,
23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
hanem csak hallották, hogy aki minket üldözött egykor, most hirdeti azt a hitet, amelyet egykor pusztított.
24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.
És dicsőítették bennem az Istent.

< Agalatiya 1 >