< Agalatiya 1 >
1 Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
Paul, an apostle—not from men, nor through man, but through Jesus Christ, and God the Father, who raised him from the dead—
2 pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
and all the brothers who are with me, to the assemblies of Galatia:
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
Grace to you and peace from God the Father and our Lord Jesus Christ,
4 Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn )
who gave himself for our sins, that he might deliver us out of this present evil age, according to the will of our God and Father— (aiōn )
5 Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
to whom be the glory forever and ever. Amen. (aiōn )
6 Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
I marvel that you are so quickly deserting him who called you in the grace of Christ to a different “good news”,
7 umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
but there isn’t another “good news.” Only there are some who trouble you and want to pervert the Good News of Christ.
8 Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
But even though we, or an angel from heaven, should preach to you any “good news” other than that which we preached to you, let him be cursed.
9 Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
As we have said before, so I now say again: if any man preaches to you any “good news” other than that which you received, let him be cursed.
10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
For am I now seeking the favor of men, or of God? Or am I striving to please men? For if I were still pleasing men, I wouldn’t be a servant of Christ.
11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
But I make known to you, brothers, concerning the Good News which was preached by me, that it is not according to man.
12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
For I didn’t receive it from man, nor was I taught it, but it came to me through revelation of Jesus Christ.
13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
For you have heard of my way of living in time past in the Jews’ religion, how that beyond measure I persecuted the assembly of God and ravaged it.
14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
I advanced in the Jews’ religion beyond many of my own age among my countrymen, being more exceedingly zealous for the traditions of my fathers.
15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
But when it was the good pleasure of God, who separated me from my mother’s womb and called me through his grace,
16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
to reveal his Son in me, that I might preach him among the Gentiles, I didn’t immediately confer with flesh and blood,
17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
nor did I go up to Jerusalem to those who were apostles before me, but I went away into Arabia. Then I returned to Damascus.
18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
Then after three years I went up to Jerusalem to visit Peter, and stayed with him fifteen days.
19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
But of the other apostles I saw no one except James, the Lord’s brother.
20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
Now about the things which I write to you, behold, before God, I’m not lying.
21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
Then I came to the regions of Syria and Cilicia.
22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
I was still unknown by face to the assemblies of Judea which were in Christ,
23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
but they only heard, “He who once persecuted us now preaches the faith that he once tried to destroy.”
24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.
So they glorified God in me.