< Agalatiya 1 >
1 Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
本信函来自保罗,我的使徒身份并非由人类组织或人类权力所指认,恰恰相反,我是由耶稣基督和让耶稣复活的天父上帝所指认。
2 pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
这封写给加拉太众教会的信函,由与我同在的所有兄弟姐妹共同写就。
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
愿上帝天父以及主耶稣基督的恩惠和平安与你们同在。
4 Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn )
基督遵循我们天父上帝的旨意,因我们的罪而献出自己的生命,让我们脱离现在这个邪恶的时代。 (aiōn )
5 Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
愿荣耀归给他,直到永远。阿门。 (aiōn )
6 Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
让我震惊的是,你们借由耶稣恩惠的召唤信了上帝,却又如此快速将其放弃,转向其他福音,
7 umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
而那根本不是福音,只是其他人用于迷惑你们,想要曲解基督的福音。
8 Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
但无论是谁,即使是我们自己或天堂的天使,如果所传“福音”并非我们之前传给你们的福音,就该受到谴责。
9 Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
我们想再重复这一点:如果有人所传并非我们之前传给你们的福音,就该受到谴责。
10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
你们认为我需要谁的认可?来自人或是来自上帝?你认为我试图取悦人?如果我想要取悦人,就不是基督的仆人。
11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
朋友们,让我明确地告诉你们,我所传的福音并非来自任何人类。
12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
因为我并非从人那里获得这福音,也并非由人教导,而是通过耶稣基督的启示获取。
13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
你们都听过,我过去曾是犹太宗教的追随者,听说过我如何疯狂迫害上帝的教会,残忍地想要破坏它。
14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
我在犹太宗教中的经历超过了许多同代人,因为我对祖先的传统格外热情。
15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
但当上帝在我出生时就让我与他人有所区别,他通过其恩典呼唤我,并很高兴地
16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
将他的儿子向我显化,让我向所有国家宣扬福音,我便没有与任何人商量。
17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
我没有到耶路撒冷与先于我成为使徒的人谈话,而是去了阿拉伯,然后再回到大马士革。
18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
三年后我才上耶路撒冷去见彼得,和他住了两个星期。
19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
我也没有见其他的使徒,除了主的兄弟雅各。
20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
(在上帝面前,我向你们保证所写之事绝非谎言!)
21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
后来我去了叙利亚和基利家。
22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
尽管如此,犹太教会中的众人并未见过我的面。
23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
他们只听人说“那个从前迫害我们的人,现在开始传播他曾经想要破坏的信仰!”
24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.
他们因我而颂赞上帝。