< Agalatiya 6 >

1 Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe.
اما‌ای برادران، اگر کسی به خطایی گرفتارشود، شما که روحانی هستید چنین شخص را به روح تواضع اصلاح کنید. و خود راملاحظه کن که مبادا تو نیز در تجربه افتی.۱
2 Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu.
بارهای سنگین یکدیگر را متحمل شوید و بدین نوع شریعت مسیح را به‌جا آرید.۲
3 Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha.
زیرا اگر کسی خود را شخص گمان برد و حال آنکه چیزی نباشد، خود را می‌فریبد.۳
4 Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake,
اما هرکس عمل خودرا امتحان بکند، آنگاه فخر در خود به تنهایی خواهد داشت نه در دیگری،۴
5 pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
زیرا هرکس حامل بار خود خواهد شد.۵
6 Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
اما هرکه در کلام تعلیم یافته باشد، معلم خود را در همه‌چیزهای خوب مشارک بسازد.۶
7 Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa.
خود را فریب مدهید، خدا رااستهزاء نمی توان کرد. زیرا که آنچه آدمی بکارد، همان را درو خواهد کرد.۷
8 Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios g166)
زیرا هر‌که برای جسم خود کارد، از جسم فساد را درو کند و هرکه برای روح کارد از روح حیات جاودانی خواهد دروید. (aiōnios g166)۸
9 Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa.
لیکن از نیکوکاری خسته نشویم زیرا که درموسم آن درو خواهیم کرد اگر ملول نشویم.۹
10 Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
خلاصه بقدری که فرصت داریم با جمیع مردم احسان بنماییم، علی الخصوص با اهل بیت ایمان.۱۰
11 Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
ملاحظه کنید چه حروف جلی بدست خود به شما نوشتم.۱۱
12 Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu.
آنانی که می‌خواهند صورتی نیکو در جسم نمایان سازند، ایشان شمارا مجبور می‌سازند که مختون شوید، محض اینکه برای صلیب مسیح جفا نبینند.۱۲
13 Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo.
زیراایشان نیز که مختون می‌شوند، خود شریعت رانگاه نمی دارند بلکه می‌خواهند شما مختون شوید تا در جسم شما فخر کنند.۱۳
14 Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi.
لیکن حاشا ازمن که فخر کنم جز از صلیب خداوند ما عیسی مسیح که بوسیله او دنیا برای من مصلوب شد و من برای دنیا.۱۴
15 Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano.
زیرا که در مسیح عیسی نه ختنه چیزی است و نه نامختونی بلکه خلقت تازه.۱۵
16 Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
وآنانی که بدین قانون رفتار می‌کنند، سلامتی ورحمت بر ایشان باد و بر اسرائیل خدا.۱۶
17 Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
بعد ازاین هیچ‌کس مرا زحمت نرساند زیرا که من در بدن خود داغهای خداوند عیسی را دارم.۱۷
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.
فیض خداوند ما عیسی مسیح با روح شما باد‌ای برادران. آمین.۱۸

< Agalatiya 6 >