< Agalatiya 6 >

1 Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe.
Braćo, ako se tko i zatekne u kakvu prijestupu, vi, duhovni, takva ispravljajte u duhu blagosti. A pazi na samoga sebe da i ti ne podlegneš napasti.
2 Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu.
Nosite jedni bremena drugih i tako ćete ispuniti zakon Kristov!
3 Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha.
Jer misli li tko da jest štogod, a nije ništa, sam sebe vara.
4 Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake,
Svatko neka ispita sam svoje djelo pa će onda u samom sebi imati čime se dičiti, a ne u usporedbi s drugim.
5 pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
Ta svatko će nositi svoj teret.
6 Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
Koji se uči Riječi, neka sva dobra dijeli sa svojim učiteljem.
7 Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa.
Ne varajte se: Bog se ne da izrugivati! Što tko sije, to će i žeti!
8 Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios g166)
Doista, tko sije u tijelo svoje, iz tijela će žeti raspadljivost, a tko sije u duh, iz duha će žeti život vječni. (aiōnios g166)
9 Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa.
Neka nam ne dozlogrdi činiti dobro: ako ne sustanemo, u svoje ćemo vrijeme žeti!
10 Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
Dakle, dok imamo vremena, činimo dobro svima, ponajpače domaćima u vjeri.
11 Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
Gledajte kolikim vam slovima pišem svojom rukom.
12 Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu.
Svi koji se hoće praviti važni tijelom, sile vas na obrezanje, samo da zbog križa Kristova ne bi trpjeli progonstvo.
13 Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo.
Ta ni sami obrezani ne opslužuju Zakona, ali hoće da se vi obrežete da bi se mogli ponositi vašim tijelom.
14 Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi.
A ja, Bože sačuvaj da bih se ičim ponosio osim križem Gospodina našega Isusa Krista po kojem je meni svijet raspet i ja svijetu.
15 Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano.
Uistinu, niti je što obrezanje niti neobrezanje, nego - novo stvorenje.
16 Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
A na sve koji se ovoga pravila budu držali, i na sveg Izraela Božjega - mir i milosrđe!
17 Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
Ubuduće neka mi nitko ne dodijava jer ja na svom tijelu nosim biljege Isusove!
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.
Milost Gospodina našega Isusa Krista s duhom vašim, braćo! Amen

< Agalatiya 6 >