< Agalatiya 5 >
1 Khristu anatimasula kuti tikhale mfulu. Tsono chirimikani, ndipo musakodwenso mʼgoli la ukapolo.
Stand fast therefore in the freedom for which Christ has set us free, and do not submit again to a yoke of slavery.
2 Chonde mvetsetsani! Ine Paulo, ndikukuwuzani kuti mukalola kuchita mdulidwe, Khristu simupindula nayenso konse.
Behold, I, Paul, say to you that if you let yourselves be circumcised, Christ will be of no benefit to you.
3 Ndikubwerezanso kuwuza munthu aliyense wovomereza kuchita mdulidwe kuti ayeneranso kutsata Malamulo onse.
I testify again to every man who lets himself be circumcised that he is obligated to keep the entire law.
4 Inu amene mukufuna kulungamitsidwa ndi lamulo mwachotsedwa mwa Khristu; munagwa kusiyana nacho chisomo.
You who are seeking to be justified by the law are alienated from Christ; you have fallen away from grace.
5 Koma mwachikhulupiriro, ife tikudikira mwachidwi kudzera mwa Mzimu, chilungamo chimene tikuyembekeza.
For through the Spirit, by faith, we eagerly await the hope of righteousness.
6 Pakuti mwa Khristu Yesu mdulidwe kapena kusachita mdulidwe zilibe phindu. Chinthu chokhacho chimene chimafunika ndi chikhulupiriro chogwira ntchito mwachikondi.
For in Christ Jesus neither does circumcision have any significance, nor uncircumcision, but what matters is faith working through love.
7 Inu munkathamanga mpikisano wanu wabwino. Anakuletsani ndani kuti musamverenso choonadi?
You were running well. Who hindered you from obeying the truth?
8 Kukopeka kwanu kumeneku sikuchokera kwa Iye amene anakuyitanani.
This persuasion does not come from him who calls you.
9 “Yisiti wapangʼono amagwira ntchito mu buledi yense.”
A little leaven leavens the whole lump.
10 Ine ndikutsimikiza mwa Ambuye kuti inu simudzasiyana nane maganizo. Iye amene akukusokonezani adzalangidwa, kaya iyeyo ndiye ndani.
I have confidence in you in the Lord that you will adopt no other mindset. But the one who is troubling you will bear his judgment, whoever he may be.
11 Abale, ngati ine ndikulalikirabe za mdulidwe, nʼchifukwa chiyani ndikusautsidwabe? Ngati ndikanakhala kuti sindikulalikira chipulumutso cha mtanda, palibe amene akanakhumudwa.
Now, brothers, if I am still preaching circumcision, why am I still being persecuted? In that case the offense of the cross has been done away with.
12 Kunena za amene akukuvutani, ndikanakonda akanangodzithena okha!
Oh that those who are unsettling you would cut themselves off!
13 Inu abale, Mulungu anakuyitanani kuti mukhale mfulu. Koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo kuchita zoyipa zachikhalidwe cha uchimo cha thupi lanu, koma mutumikirane wina ndi mnzake mwachikondi.
You were called to freedom, brothers. Only do not use your freedom as an opportunity for the flesh, but serve one another in love.
14 Pakuti malamulo onse akuphatikizidwa mu lamulo ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.”
For the entire law is fulfilled in this one commandment: “Yoʋ shall love yoʋr neighbor as yoʋrself.”
15 Ngati mupitiriza kulumana ndi kukhadzulana, samalani kuti mungawonongane.
But if you bite and devour one another, watch out, or you will be consumed by one another.
16 Choncho ine ndikuti, mulole kuti Mzimu akutsogolereni ndipo simudzachita zofuna za thupi lanu la uchimo.
I say then, walk by the Spirit and you will certainly not gratify the desires of the flesh.
17 Pakuti thupi lanu la uchimo limalakalaka zimene ndi zotsutsana ndi Mzimu, ndi Mzimu zimene ndi zotsutsana ndi thupi lanu la uchimo. Ziwirizi zimadana, kotero kuti simungachite zimene mukufuna.
For the flesh desires what is contrary to the Spirit, and the Spirit desires what is contrary to the flesh. These are opposed to each other, to keep you from doing the very things you want to do.
18 Koma ngati Mzimu akutsogolerani, ndiye kuti simuli pansi pa lamulo.
But if you are led by the Spirit, you are not under the law.
19 Ntchito za thupi lanu la uchimo zimaonekera poyera ndi izi: dama, zodetsa ndi kuchita zonyansa;
Now the works of the flesh are obvious: adultery, fornication, impurity, sensuality,
20 kupembedza mafano ndi ufiti; kudana, kukangana, kupsa mtima, kudzikonda, kugawikana, mipatuko
idolatry, sorcery, hostilities, quarrels, jealousies, fits of rage, selfish ambitions, dissensions, factions,
21 ndi nsanje, kuledzera, mchezo ndi zina zotere. Ine ndikukuchenjezani monga ndinachita poyamba paja kuti amene amachita zimenezi sadzalandira ufumu wa Mulungu.
envy, murder, drunkenness, revelries, and the like. I warn you, just as I warned you before, that those who practice such things will not inherit the kingdom of God.
22 Koma chipatso cha Mzimu Woyera ndi chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,
But the fruit of the Spirit is love, joy, peace, patience, kindness, goodness, faithfulness,
23 kufatsa ndi kudziretsa. Palibe lamulo loletsa zimenezi.
gentleness, and self-control; against such things there is no law.
24 Amene ali ake a Khristu Yesu anapachika pa mtanda thupi lawo la uchimo pamodzi ndi zokhumba zawo ndi zolakalaka zawo.
Now those who belong to Christ have crucified the flesh with its passions and desires.
25 Popeza timakhala ndi moyo mwa Mzimu Woyera, tiyeni tiyende pamodzi ndi Mzimu Woyera.
Since we live by the Spirit, let us also keep in step with the Spirit.
26 Tisakhale odzitukumula, oputana ndi ochitirana nsanje.
Let us not become conceited, provoking one another and envying one another.