< Agalatiya 5 >
1 Khristu anatimasula kuti tikhale mfulu. Tsono chirimikani, ndipo musakodwenso mʼgoli la ukapolo.
the/this/who freedom (which *k*) me Christ to set free to stand therefore/then and not again yoke/scales slavery to oppose
2 Chonde mvetsetsani! Ine Paulo, ndikukuwuzani kuti mukalola kuchita mdulidwe, Khristu simupindula nayenso konse.
look! I/we Paul to say you that/since: that if to circumcise Christ you none to help
3 Ndikubwerezanso kuwuza munthu aliyense wovomereza kuchita mdulidwe kuti ayeneranso kutsata Malamulo onse.
to testify then again all a human to circumcise that/since: that debtor to be all the/this/who law to do/make: do
4 Inu amene mukufuna kulungamitsidwa ndi lamulo mwachotsedwa mwa Khristu; munagwa kusiyana nacho chisomo.
to abate away from (the/this/who *k*) Christ who/which in/on/among law to justify the/this/who grace to fall out
5 Koma mwachikhulupiriro, ife tikudikira mwachidwi kudzera mwa Mzimu, chilungamo chimene tikuyembekeza.
me for spirit/breath: spirit out from faith hope righteousness to expect
6 Pakuti mwa Khristu Yesu mdulidwe kapena kusachita mdulidwe zilibe phindu. Chinthu chokhacho chimene chimafunika ndi chikhulupiriro chogwira ntchito mwachikondi.
in/on/among for Christ Jesus neither circumcision one be strong neither uncircumcision but faith through/because of love be active
7 Inu munkathamanga mpikisano wanu wabwino. Anakuletsani ndani kuti musamverenso choonadi?
to run well which? you (to impede *N(k)O*) the/this/who truth not to persuade
8 Kukopeka kwanu kumeneku sikuchokera kwa Iye amene anakuyitanani.
the/this/who persuasion no out from the/this/who to call: call you
9 “Yisiti wapangʼono amagwira ntchito mu buledi yense.”
small leaven all the/this/who lump to leaven
10 Ine ndikutsimikiza mwa Ambuye kuti inu simudzasiyana nane maganizo. Iye amene akukusokonezani adzalangidwa, kaya iyeyo ndiye ndani.
I/we to persuade toward you in/on/among lord: God that/since: that none another to reason the/this/who then to trouble you to carry the/this/who judgment who/which (if *N(k)O*) to be
11 Abale, ngati ine ndikulalikirabe za mdulidwe, nʼchifukwa chiyani ndikusautsidwabe? Ngati ndikanakhala kuti sindikulalikira chipulumutso cha mtanda, palibe amene akanakhumudwa.
I/we then brother if circumcision still to preach which? still to pursue therefore to abate the/this/who stumbling block the/this/who cross
12 Kunena za amene akukuvutani, ndikanakonda akanangodzithena okha!
I wish! and to cut off the/this/who to cause trouble you
13 Inu abale, Mulungu anakuyitanani kuti mukhale mfulu. Koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo kuchita zoyipa zachikhalidwe cha uchimo cha thupi lanu, koma mutumikirane wina ndi mnzake mwachikondi.
you for upon/to/against freedom to call: call brother alone not the/this/who freedom toward opportunity the/this/who flesh but through/because of the/this/who love be a slave one another
14 Pakuti malamulo onse akuphatikizidwa mu lamulo ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.”
the/this/who for all law in/on/among one word (to fulfill *N(k)O*) in/on/among the/this/who to love the/this/who near/neighbor you as/when (you *NK(O)*)
15 Ngati mupitiriza kulumana ndi kukhadzulana, samalani kuti mungawonongane.
if then one another to bite and to devour to see not by/under: by one another to consume
16 Choncho ine ndikuti, mulole kuti Mzimu akutsogolereni ndipo simudzachita zofuna za thupi lanu la uchimo.
to say then spirit/breath: spirit to walk and desire flesh no not to finish
17 Pakuti thupi lanu la uchimo limalakalaka zimene ndi zotsutsana ndi Mzimu, ndi Mzimu zimene ndi zotsutsana ndi thupi lanu la uchimo. Ziwirizi zimadana, kotero kuti simungachite zimene mukufuna.
the/this/who for flesh to long for according to the/this/who spirit/breath: spirit the/this/who then spirit/breath: spirit according to the/this/who flesh this/he/she/it (for *N(k)O*) one another be an opponent in order that/to not which (if *N(k)O*) to will/desire this/he/she/it to do/make: do
18 Koma ngati Mzimu akutsogolerani, ndiye kuti simuli pansi pa lamulo.
if then spirit/breath: spirit to bring no to be by/under: under law
19 Ntchito za thupi lanu la uchimo zimaonekera poyera ndi izi: dama, zodetsa ndi kuchita zonyansa;
clear then to be the/this/who work the/this/who flesh who/which to be (adultery *K*) sexual sin impurity debauchery
20 kupembedza mafano ndi ufiti; kudana, kukangana, kupsa mtima, kudzikonda, kugawikana, mipatuko
idolatry (sorcery *NK(o)*) hostility quarrel (zeal *N(k)O*) wrath rivalry dissension sect
21 ndi nsanje, kuledzera, mchezo ndi zina zotere. Ine ndikukuchenjezani monga ndinachita poyamba paja kuti amene amachita zimenezi sadzalandira ufumu wa Mulungu.
envy (murder *KO*) drunkenness orgy and the/this/who like this/he/she/it which to foretell you as/just as (and *k*) to predict that/since: that the/this/who the/this/who such as this to do/require kingdom God no to inherit
22 Koma chipatso cha Mzimu Woyera ndi chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,
the/this/who then fruit the/this/who spirit/breath: spirit to be love joy peace patience kindness goodness faith: faithfulness
23 kufatsa ndi kudziretsa. Palibe lamulo loletsa zimenezi.
gentleness self-control according to the/this/who such as this no to be law
24 Amene ali ake a Khristu Yesu anapachika pa mtanda thupi lawo la uchimo pamodzi ndi zokhumba zawo ndi zolakalaka zawo.
the/this/who then the/this/who Christ (Jesus *NO*) the/this/who flesh to crucify with the/this/who suffering and the/this/who desire
25 Popeza timakhala ndi moyo mwa Mzimu Woyera, tiyeni tiyende pamodzi ndi Mzimu Woyera.
if to live spirit/breath: spirit spirit/breath: spirit and to follow
26 Tisakhale odzitukumula, oputana ndi ochitirana nsanje.
not to be conceited one another to provoke one another to envy