< Agalatiya 3 >
1 Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani? Tinamuonetsa poyera pamaso panu Yesu Khristu monga wopachikidwa pa mtanda.
Inteno yushi qoponta Gelatiya asatoy! intes baletontamala iza kaqetetha ta inte sinthan milale mala gigisa besdisko shin intena oone biitiday?
2 Ine ndikufuna ndiphunzire kuchokera kwa inu chinthu chimodzi ichi: Kodi munalandira Mzimu pochita ntchito za lamulo, kapena pokhulupirira zimene munamva?
Inte Xillo ayana ekiday Muse wogga nagone ye sabaketida qaala amanone? Ta hano isiniyo ta intefe erana koyays.
3 Kani ndinu opusa chotere? Inu mutayamba ndi Mzimu, kodi mukufuna kutsiriza ndi ntchito zathupi?
Inte hessamala qopi eronta asse? Ayanan oykidaysa zaridi ashon geyanas wayeteti?
4 Kodi munavutika kwambiri pachabe, ngati kunali kwachabedi?
Tumu inte hano gakanas daburida daburisay co mella?
5 Kodi Mulungu amene anakupatsani Mzimu wake ndi kuchita zodabwitsa pakati panu, amachita zimenezi chifukwa mumachita ntchito za lamulo kapena chifukwa mumakhulupirira zimene munamva?
Xoossi intes ayana imidayne inte achan malata oothiday inte Muse wogga nagida gisheye Woyko inte siiyda qalan amanida giishe?
6 Nʼchimodzimodzinso Abrahamu, “Iye anakhulupirira Mulungu, ndipo Mulungu anamutenga kukhala wolungama.”
Ane inte Abirame gish qoppiite “Izi Xoosu amanin amamoy izas xiillotethan qodetides.”
7 Tsono zindikirani kuti amene akhulupirira, ndi ana a Abrahamu.
Hesa gish amanizayti Abirame nayta gididaysa yushi qopiite (Wozinan wothiite)
8 Malemba anaonetseratu kuti Mulungu adzalungamitsa anthu a mitundu ina mwachikhulupiriro, ndipo ananeneratu Uthenga Wabwino kwa Abrahamu kuti, “Mitundu yonse ya anthu idzadalitsika kudzera mwa iwe.”
Dere asay amanon atanaysa eridi Xoosu kasse maxxafan “Derey wuri ne bagara anjjistana” Giidi mishiracho qaala Abiirames erisides.
9 Choncho iwo amene ali ndi chikhulupiriro ndi odalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu, munthu wachikhulupiriro.
Hesa gish amanizayti wurii amaniza Abiramera isipw anjjetidayta.
10 Onse amene amadalira ntchito za lamulo ndi otembereredwa, pakuti zalembedwa mʼBuku la Malamulo kuti, “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita zonse zimene zalembedwa mʼBuku la Malamulo.”
Muse wogga nagon amanetizayti wurikka qantha garisan detes. Muse wogga maxxafatan xafetidaysa wursi Othontadey zi qangetidade” geteti xafetides.
11 Chodziwikiratu nʼchakuti palibe amene amalungamitsidwa pamaso pa Mulungu ndi lamulo, chifukwa, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
“Xiillo uray amanon deyos” giiza gish onikka Xoossa sinthan Muse woggan atontaysi gesha.
12 Koma chikhulupiriro si Malamulo, chifukwa Malemba akuti, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
Muse woggan amanon xaphiibeyna. Gido attin “Muse wogata Musesi nagizadey he izi nagidaysan deyon dana getetides.
13 Khristu anatiwombola ku temberero la lamulo pokhala temberero mʼmalo mwathu, pakuti analemba kuti, “Aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa.”
“Miitha bolla kaqetizadey he uray qangetidade” geteti xafetida gish Kiristossay nu gish qangetidade gididi nuna Muse wogga qangethafe wozinas.
14 Iye anatiwombola ife ndi cholinga chakuti madalitso woperekedwa kwa Abrahamu abwere kwa anthu a mitundu ina kudzera mwa Khristu Yesu, kuti ndi chikhulupiriro tilandire lonjezo la Mzimu.
Abirime imetida anjjoy Yesuss Kiristosa bagara deres gakanamala nuna wozides. Hesikka nuni amanon Xoossi immana gida iza ayana ufaysa ekanamala hanides.
15 Abale, ndiloleni ndipereke chitsanzo cha zochitika mʼmoyo wa tsiku ndi tsiku. Pangano likakhazikitsidwa palibe amene angachotsepo kapena kuwonjezerapo, choncho ndi chimodzimodzi pa nkhani iyi.
Ta ishato ane ta intes asi ba dusan hanizamisha Museso imays. Haray atoshin asi isito bazida qaala isito bazidappe guye oonikka sharanas woykko hara iza bolla gujjana danda7ontaysamala haysikka hessa malakko.
16 Malonjezo awa anaperekedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbewu yake. Malemba sakunena kuti, “kwa mbewu zake,” kutanthauza anthu ambiri, koma, “kwa mbewu yako,” kutanthauza munthu mmodzi, amene ndi Khristu.
Xoossi Abirames yotida qaala Abiramesne iza zerethas. Maxxafay daro asas yotizamala “Iza zerethatas” Gena gido attiin isi asas yotetizamala “Ne zerethas” ges. Hesikka Kiristossa.
17 Chimene ndikutanthauza ine ndi ichi: Malamulo amene anabwera patatha zaka 430, sangathetse pangano limene linakhazikitsidwa kale ndi Mulungu ndi kuliwononga lonjezolo.
Ta gizaykka hayssako ooydu xistane heezdzdutamu laythafe guye imetida Muse wogay kasetidi Xoosi minthida caqqoza lalidi buro hanana ufaysa qaala sharena.
18 Ngati madalitso athu akudalira ntchito za lamulo ndiye kuti madalitsowo sakupatsidwa chifukwa cha lonjezo. Koma Mulungu mwachisomo chake anadalitsa Abrahamu kudzera mu lonjezo.
Biita latoy Muse wogan hanizako ufayasa qaala gelanas koshena gish Xoossi ba kiiyatethan qalan Abirames imetides.
19 Nanga tsono cholinga cha lamulo chinali chiyani? Linaperekedwa chifukwa cha zolakwa mpaka itafika mbewu imene lonjezo limanena. Malamulowo anaperekedwa ndi angelo kudzera mwa mʼkhalapakati.
Hiistin Muse woggan azzas imetide? Muse wogay gudetiday asay woga yedhi athiza gish he ufaysay besiza zerethay yana gakanas Muse wogay ydayka kiitanchata bagara naga giiza isade bagara ydes.
20 Ngakhale zili chomwecho, mʼkhalapakati sayimira mbali imodzi yokha, koma Mulungu ndi mmodzi.
Gidikkoka ganazi isa baga xala xelizade gidena. Xoossi gidiko izi isa xala.
21 Kodi ndiye kuti lamulo limatsutsana ndi malonjezo a Mulungu? Ayi. Nʼkosatheka! Pakuti ngati tikanapatsidwa malamulo opatsa moyo ndiye kuti mwa lamulo tikanakhala olungama.
Histin Muse wogay inthafe Xoosi wothina qaala digizaze? Cirasheka digena. Muse woga imetiday asi izan deyo demanas gididako tumuka xiilotethi bistanakoshin.
22 Koma Malemba akunenetsa kuti dziko lonse lili mu ulamuliro wauchimo, kuti mwachikhulupiriro mwa Yesu Khristu, chimene chinalonjezedwa chiperekedwe kwa amene akhulupirira.
Qasse maxxafay haysi 7alamey wurikka nagaran qachetidaysa awajjes. Hesikka asi wurikka Yesuss Kiristossa amanon betiza ufaysay amanizaytas wurisos imistanasa.
23 Chikhulupiriro ichi chisanabwere, ife tinali mʼndende ya lamulo, otsekeredwa mpaka pamene chikhulupiriro chikanavumbulutsidwa.
Haysi amanoy yanape kasse nuni Muse wogan qachetidi gordana dosu.
24 Choncho lamulo linayikidwa kukhala lotiyangʼanira kuti lititsogolere kwa Khristu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro.
Hessa gish nu amanon xiilana mala Muse wogay nuna Kiristosakko gathanas nagizade mala gidi nagides.
25 Tsopano pakuti chikhulupiriro chabwera, ife sitilinso mu ulamuliro wa lamulo.
Ha7i qasse he amanoy yida gihs hayssafe guye nuni Muse wogga garisan dokko.
26 Nonse ndinu ana a Mulungu kudzera mʼchikhulupiriro mwa Khristu Yesu,
Inte wurikka Yesuss Kiristossa amanon Xoossa nayta.
27 pakuti nonse amene munalumikizana ndi Khristu mu ubatizo munavala Khristu.
Inte Kirstossara gidana xamaqetidayti wurikka Kiristossa maydista.
28 Palibe Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu, mwamuna kapena mkazi, pakuti nonse ndinu amodzi mwa Khristu Yesu.
Inte wurikka Yesusi Kiristossan isino attiin Ayhudene Girike aylene Goqqane maccane ade giza dumatethi dena. Inte wurikka Yesusi Kiristosan isi asho.
29 Ngati inu muli ake a Khristu, ndiye kuti ndinu mbewu ya Abrahamu, ndi olowamʼmalo molingana ndi lonjezo.
Inte Kirstossayta gidiko inte Abirame zerethata kasse imetida ufaysa qaala mala inte latanayta.