< Ezara 8 >

1 Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
EIA ka poe koikoi o na makua, a me ke kuauhau o lakou, ka poe i pii pu me au, mai Babulona aku, i ke au ia Aretasaseta ke alii.
2 Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
No na mamo a Pinehasa; o Geresoma; no na mamo a Itamara; o Daniela; no na mamo a Davida; o Hatusa;
3 mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
No na mamo a Sekania, no na mamo a Parosa; o Zekaria: a me ia ua heluia ma ke kuauhau o na kane, hookahi haneri a me kanalima.
4 Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
No na mamo a Panatamoaba; o Elihoenai ke keiki a Zerahia, a me ia no elua haneri kane.
5 Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
No na mamo a Sekania; o ke keiki a Iahaziela, a me ia no ekolu haneri kane.
6 Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
No na mamo a Adina; o Ebeda, ke keiki a Ionatana, a me ia no he kanalima kane.
7 Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
No na mamo a Elama; o Iesaia, ke keiki a Atalia, a me ia no he kanahiku kane.
8 Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
No na mamo a Sepatia; o Zebadia ke keiki a Mikaela, a me ia no he kanawalu kane.
9 Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
No na mamo a Ioaba; o Obadia ke keiki a Iehiela, a me ia no elua haneri a me ka umikumamawalu kane.
10 Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
O na mamo a Selomita; o ke keiki a Iosipia, a me ia no hookahi haneri a me kanaono kane.
11 Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
No na mamo a Bebai; o Zekaria ke keiki a Bebai, a'me ia no he iwakalua a me kumamawalu kane.
12 Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
No na mamo a Azegada; o Iohanana ke keiki a Hakatana, a me ia no hookahi haneri a me ka umi na kane.
13 Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
No na mamo hope a Adonikama, a eia ka inoa o lakou, o Elipeleta, o Ieiela, a me Semaia, a me lakou no he kanaono kane.
14 Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
A no na mamo hoi a Bigevai; o Utai, a o Zabuda, a me laua no he kanahiku na kane.
15 Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
A hoakoakoa ae la au ia lakou ma ka muliwai e kahe ana i Ahava, a malaila makou i hoomoana'i i na ia ekolu: a nana aku la au i na kanaka, a me na kahuna, aole i lona malaila kekahi o na mamo a Levi.
16 Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
Alaila kii aku la au ia Eliezera, a ia Ariela, a ia Simaia, a ia Elenatana, a ia Iariba, a ia Elenatana, a ia Nataua, a ia Zekaria, a me Mesulama, he mau mea koikoi; a ia Ioiariba, a ia Elenatana, he mau mea naauao.
17 ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
A hoouna aku au ia lakou e kauoha ia Ido, i ka luna ma ke kauwahi i Kasipia, a hai aku au ia lakou i na mea a lakou e olelo aku ai ia Ido, a me kona mau houhanau, ka poe Netini ma ke kauwahi i Kaeipia, e lawe mai lakou na makou i mea lawelawe no ka hale o ko kakou Akua.
18 Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
A ma ka lima o ke Akua maluna o makou e pono ai, lawe mai lakou no makou i kekahi kanaka naauao no na keiki a Maheli, ka mamo a Levi, ke keiki a Iseraela; a ia Serebia, me kana mau keiki, a me kona mau hoahanau he umikumamawalu;
19 Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
A me Hasabia, a me ia no o Iesaia, no na mamo a Merari, kona mau hoahanau, a me ka lakou mau keiki, he iwakalua;
20 Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
A no ka poe Netini, na mea a Davida, a me na luna i hoonoho ai no ka oihana Levi, elua haneri a me ka iwakalua Netini: ua kaheaia lakou a pau ma ka inoa.
21 Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
Alaila kukala aku au i hookeai malaila ma ka muliwai o Ahava, i hoohaahaa iho ai makou ia makou iho imua o ko kakou Akua, e imi aku ia ia i aoao pono no makou, a no ka makou kamalii, a no ka makou waiwai a pau.
22 Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
No ka mea ua hilahila no wau e noi aku i ke alii i poe koa, a me na holohololio, e kokua ia makou no na enemi ma ke ala: no ka mea, ua olelo makou i ke alii, i ka i ana'ku, O ka lima o ko kakou Akua maluna o lakou a pau e pono ai, o ka poe e imi ana ia ia; aka, ua ku e mai kona mana a me kona huhu i ka poe a pau e haalele ia ia.
23 Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
A hookeai iho la makou, n nonoi aku i ko kakou Akua no keia mea; a hoolohe mai no ia ia makou.
24 Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
Alaila hookaawale au i na luna kahuna he umikumamalua. o Serebia, o Hasabia, a ho umi o ko laua mau hoahanau me laua;
25 ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
A kaupaona iho la au no lakou i ke kala, a i ke gula, a me na kiaha, ka manawalea no ka hale o ko kakou Akua, a ke alii, a me kona poe kakaolelo, a me kona poe luna, a me ka Iseraela a pau e noho ana, i haawi mai ai:
26 Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
Kaupaona aku la nu no ko lakou lima i eono haneri a mo kanalima talena kala, a me na kiaha kala hookahi haneri talena, a me ke gula hookahi haneri talena;
27 mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
A he iwakalua bola gula, hookahi tausani derama; a elua kiaha keleawe melemele maikai, he nui ke kumukuai, e like me ke gula.
28 Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
A i aku la au ia lakou, Ua hoolaaia oukou no Iehova: ua hoolaaia no hoi na kiaha; a o ke kala a me ke gula, he makana wale no Iehova ke Akua o ko oukou poe kupuna.
29 Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
E makaala oukou, a e malama hoi, a kaupaona oukou ia mea imua o na luna kahuna a me na Levi, a me na mea koikoi o na makua o ka Iseraela ma Ierusalema, iloko o na keena ma ka hale o Iehova.
30 Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
A lawe ae la na kahuna a me na Levi i ke kala, a me ke gula, a me na kiaha i kaupaonaia, e hali aku i Ierusalema ma ka hale o ko kakou Akua.
31 Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
A haalele makou i ka muliwai o Ahava, i ka la umikumamalua o ka malama mua, e hele i Ierusalema; a maluna o makou ka lima o ko makou Akua, a hoopakele no oia ia makou i ka lima o ka enemi, a me ka poe hoohalua ma ke ala.
32 Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
A hele mai makou i Ierusalema, a noho malaila i na la ekolu.
33 Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
A i ka ha o ka la, kaupaonaia ke kala, a me ke gula, a me na kiaha, iloko o ka hale o ko kakou Akua, ma ka lima o Meremota, ke keiki a Uria ke kahana; a me ia no o Eleazara, ke keiki a Pioehasa; a me lakou no o Iozabada, ke keiki a Iesua, a o Noadia, ke keiki a Binui, no na Levi;
34 Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
Ma ka helu ana, a me ke kaupaona ana, o na mea a pau: a o na paona a pau, ua kakauia i kela manawa.
35 Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
A o na keiki a ka poe pio i hoi hou mai, kaumaha aku lakou i na mohaikuni i ke Akua o ka Iseraela, he umikumamalua na bipikane no ka Iseraela a pau, a he kanaiwakumamaono na hipakane, a he kauahikukumamahiku na keikihipa, he umikumamalua na kaokane, i mohai hala: oia mea a pau i mohaikuni ia Iehova.
36 Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.
A haawi aku lakou i na kauoha a ke alii, i na kiaaina, a me na'lii aimoku o ke alii ma keia aoao o ka muliwai; a kokua lakou i na kauaka, a me ka hale o ke Akua.

< Ezara 8 >