< Ezara 8 >
1 Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
Voici donc les princes des familles, et la généalogie de ceux qui sont montés avec moi sous le règne d’Artaxerxès, roi de Babylone:
2 Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
D’entre les fils de Phinéès, Gersom; des fils d’Ithamar, Daniel; des fils de David, Hattus;
3 mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
D’entre les fils de Séchénias, qui étaient fils de Pharos, Zacharias: et avec lui furent dénombrés cent cinquante hommes;
4 Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
D’entre les fils de Phahath-Moab, Elioénaï, fils de Zaréhé, et avec lui deux cents hommes;
5 Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
D’entre les fils de Séchénias, le fils d’Ézéchiel, et avec lui trois cents hommes;
6 Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
D’entre les fils d’Adan, Abed, fils de Jonathan, et avec lui cinquante hommes;
7 Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
D’entre les fils d’Alam, Isaïe, fils d’Athalias, et avec lui soixante-dix hommes;
8 Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
D’entre les fils de Saphatias, Zébédia, fils de Michaël, et avec lui quatre-vingts hommes;
9 Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
D’entre les fils de Joab, Obédia, fils de Jahiel, et avec lui deux cent dix-huit hommes;
10 Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
D’entre les fils de Sélomith, le fils de Josphia, et avec lui cent soixante hommes;
11 Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
D’entre les fils de Bébaï, Zacharie, fils de Bébaï, et avec lui vingt-huit hommes;
12 Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
D’entre le fils d’Azgad, Johanan, fils d’Eccétan, et avec lui cent dix hommes;
13 Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
D’entre les fils d’Adonicam. qui étaient les derniers, et voici leurs noms: Eliphéleth, Jéhiel, Samaïas, et avec eux soixante hommes;
14 Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
D’entre les fils de Béguï, Uthaï et Zachur, et avec eux soixante-dix hommes.
15 Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
Or je les assemblai près du fleuve qui coule vers Ahava, et nous demeurâmes là trois jours; et je cherchai parmi le peuple et les prêtres des fils de Lévi, et je n’en trouvai point là.
16 Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
C’est pourquoi j’envoyai Eliézer, Ariel, et Séméias, Elnathan, Jarib, et un autre Elnathan, Nathan, Zacharias, et Mosollam, les princes; Joïarib et Elnathan, les sages.
17 ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
Et je les envoyai vers Eddo, qui est le premier du lieu de Chasphia, et je mis en leur bouche les paroles qu’ils devaient dire à Eddo, et à ses frères Nathinéens, dans le lieu de Chasphia, afin qu’ils nous amenassent les ministres de la maison de notre Dieu.
18 Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
Et ils nous amenèrent, par la main favorable de notre Dieu, laquelle était sur nous, un homme très savant d’entre les fils de Maholi, fils de Lévi, fils d’Israël, et Sarabia, et ses fils, et ses frères, au nombre de dix-huit;
19 Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
Et Hasabia, et avec lui Isaïe d’entre les fils de Mérari, et ses frères, et ses fils, au nombre de vingt;
20 Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
Et d’entre les Nathinéens que David et les princes avaient établis pour le service des Lévites, deux cent vingt Nathinéens: tous ceux-ci étaient appelés par leurs noms.
21 Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
Or je publiai là le jeûne près du fleuve Ahava, afin de nous affliger devant le Seigneur notre Dieu, et afin de lui demander la voie droite pour nous, pour nos fils, et pour tout ce qui était à nous;
22 Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
Car j’eus honte de demander au roi du secours et des cavaliers pour nous défendre de l’ennemi dans le chemin, parce que nous avions dit au roi: La main de notre Dieu est favorable à tous ceux qui le cherchent sincèrement; et son empire, et sa fureur, sur tous ceux qui l’abandonnent.
23 Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
Or nous jeûnâmes et nous priâmes notre Dieu pour cela: et tout nous advint heureusement.
24 Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
Et je séparai douze des princes des prêtres, Sarabia et Hasabia, et avec eux dix de leurs frères;
25 ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
Et je leur pesai l’argent, l’or et les vases consacrés de la maison de notre Dieu, qu’avaient offerts le roi, ses conseillers, ses princes et tous ceux d’Israël qui avaient été trouvés;
26 Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
Je pesai aussi en leurs mains six cent cinquante talents d’argent, cent vases d’argent, et cent talents d’or,
27 mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
Et vingt coupes d’or qui pesaient mille drachmes, et deux vases d’un airain brillant excellent, beaux comme l’or.
28 Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
Et je leur dis: Vous êtes les saints du Seigneur, et les vases sont saints, ainsi que l’argent et l’or qui ont été spontanément offerts au Seigneur Dieu de nos pères.
29 Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
Veillez, et gardez-les jusqu’à ce que vous les pesiez devant les princes des prêtres, des Lévites, et devant les chefs des familles d’Israël à Jérusalem, pour le trésor de la maison du Seigneur.
30 Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
Or les prêtres et les Lévites reçurent le poids de l’argent, de l’or et des vases, pour les porter à Jérusalem dans la maison de notre Dieu.
31 Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
Nous partîmes donc du fleuve d’Ahava le douzième jour du premier mois pour aller à Jérusalem; et la main de notre Dieu fut sur nous, et nous délivra de la main de l’ennemi, et de celui qui tendait des pièges dans le chemin.
32 Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
Et nous vînmes à Jérusalem, et demeurâmes là trois jours.
33 Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
Mais au quatrième jour, l’argent fut pesé, et l’or et les vases, dans la maison de notre Dieu par la main de Mérémoth, fils d’Urie, le prêtre; et avec lui était Eléazar, fils de Phinéès, et avec eux Jozabed, fils de Josué, et Noadaïa, fils de Bennoïa, fils de Bennoï, le Lévite,
34 Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
Selon le nombre et le poids du tout; ainsi tout poids fut écrit en ce temps-là.
35 Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
Mais les fils de la transmigration qui étaient venus de la captivité, offrirent des holocaustes au Dieu d’Israël, douze veaux pour tout le peuple d’Israël, quatre-vingt-seize béliers, soixante dix-sept agneaux, douze boucs pour le péché: le tout eu holocauste au Seigneur.
36 Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.
Or ils donnèrent les édits du roi aux satrapes qui étaient auprès du roi, et aux chefs au-delà du fleuve, et ils exaltèrent le peuple et la maison de Dieu.