< Ezara 7 >

1 Zitatha izi, Aritasasita ali mfumu ya ku Perisiya, panali wansembe wina dzina lake Ezara. Iyeyu abambo ake anali Seraya mwana wa Azariya, mwana wa Hilikiya,
Njalo emva kwalezizinto, ekubuseni kukaAthakisekisi inkosi yePerisiya, uEzra indodana kaSeraya, indodana kaAzariya, indodana kaHilikhiya,
2 mwana wa Salumu, mwana wa Zadoki, mwana wa Ahitubi,
indodana kaShaluma, indodana kaZadoki, indodana kaAhitubi,
3 mwana wa Amariya, mwana wa Azariya, mwana wa Merayoti,
indodana kaAmariya, indodana kaAzariya, indodana kaMerayothi,
4 mwana wa Zerahiya, mwana wa Uzi, mwana wa Buki,
indodana kaZerahiya, indodana kaUzi, indodana kaBuki,
5 mwana wa Abisuwa, mwana wa Finehasi, mwana wa Eliezara, mwana wa Aaroni mkulu wa ansembe uja.
indodana kaAbishuwa, indodana kaPhinehasi, indodana kaEleyazare, indodana kaAroni umpristi oyinhloko.
6 Ezara ameneyu anabwera kuchokera ku Babuloni. Iyeyu anali wophunzira kwambiri za malamulo a Mose, amene Yehova Mulungu wa Israeli anapereka. Mfumu inamupatsa chilichonse chimene anapempha pakuti dzanja la Yehova Mulungu wake linali pa iye.
UEzra lo wenyuka esuka eBhabhiloni; njalo wayengumbhali oyingcitshi emlayweni kaMozisi, uJehova uNkulunkulu kaIsrayeli ayewunikile. Inkosi yasimnika sonke isicelo sakhe, njengokwesandla sikaJehova uNkulunkulu wakhe esiphezu kwakhe.
7 Tsono mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wa Aritasasita, Ezara pamodzi ndi Aisraeli ena, kuphatikizapo ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda, ndi anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ananyamuka kubwerera ku Yerusalemu.
Kwasekusenyuka abanye babantwana bakoIsrayeli lababapristi lamaLevi labahlabeleli labalindimasango lamaNethini baya eJerusalema ngomnyaka wesikhombisa kaAthakisekisi inkosi.
8 Ezara anafika ku Yerusalemu pa mwezi wachisanu wa chaka chachisanu ndi chiwiri cha mfumu.
Wasefika eJerusalema ngenyanga yesihlanu okwakungumnyaka wesikhombisa wenkosi.
9 Iye anayamba ulendo wochoka ku Babuloni pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, ndipo anafika ku Yerusalemu pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu chifukwa dzanja labwino la Mulungu wake linali pa iye.
Ngoba ngolokuqala lwenyanga yokuqala waqala ukwenyuka esuka eBhabhiloni, langolokuqala lwenyanga yesihlanu wafika eJerusalema, ngokwesandla esihle sikaNkulunkulu wakhe phezu kwakhe.
10 Popeza Ezara anadzipereka kuwerenga ndi kusunga malamulo a Yehova, iye anafunitsitsa kuphunzitsa Aisraeli malamulo ndi malangizo a Mulungu.
Ngoba uEzra wayelungise inhliziyo yakhe ukudinga umlayo weNkosi lokuwenza, lokufundisa umthetho lesimiso koIsrayeli.
11 Iyi ndi kalata imene mfumu Aritasasita anapereka kwa wansembe Ezara, mlembi wa malamulo, munthu wophunzira kwambiri zokhudza malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Le-ke yikhophi yencwadi inkosi uAthakisekisi ayinika uEzra umpristi, umbhali, umbhali wamazwi emilayo yeNkosi lowezimiso zayo kuIsrayeli.
12 Ndine Aritasasita, mfumu ya mafumu. Ndikulembera iwe Ezara wansembe ndi mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba. Malonje.
UAthakisekisi inkosi yamakhosi kuEzra umpristi, umbhali womlayo kaNkulunkulu wamazulu, ukuthula okupheleleyo, langesikhathi esinje:
13 Tsopano ndikulamula kuti Mwisraeli aliyense, wansembe kapena Mlevi wokhala mʼdziko langa, amene akufuna kupita ku Yerusalemu ndi iwe, apite.
Umthetho umiswa yimi wokuthi wonke ozithandelayo embusweni wami esizweni sakoIsrayeli labapristi baso lamaLevi ukuya eJerusalema angahamba lawe.
14 Ine mfumu pamodzi ndi alangizi anga asanu ndi awiri tikukutumani kuti mukafufuze za dziko la Yuda ndi mzinda wa Yerusalemu kuti mukaone mmene anthu akutsatira malamulo a Mulungu wanu, amene anawapereka kwa inu.
Ngoba uthunyiwe yinkosi labacebisi bayo abayisikhombisa ukuyahlolisisa ngoJuda langeJerusalema ngokomlayo kaNkulunkulu wakho osesandleni sakho,
15 Utenge siliva ndi golide zimene ine mfumu ndi alangizi anga tapereka mwa ufulu kwa Mulungu wa Israeli, amene amakhala ku Yerusalemu.
lokuthwala isiliva legolide inkosi labacebisi bayo abakunikele ngesihle kuNkulunkulu kaIsrayeli ondawo yakhe yokuhlala iseJerusalema,
16 Mutengenso siliva yense ndi golide amene mungamupeze mʼdziko lonse la Babuloni, ngakhalenso zinthu zimene anthu pamodzi ndi ansembe adzapereka mwaufulu kuperekera ku Nyumba ya Mulungu wawo ya ku Yerusalemu.
lalo lonke isiliva legolide ongakuthola esigabeni sonke seBhabhiloni lomnikelo wesihle wabantu labapristi abanikelela indlu kaNkulunkulu wabo eseJerusalema ngesihle,
17 Ndi ndalama zimenezi mudzaonetsetse kuti mwagula ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa aamuna pamodzi ndi zopereka zake za chakudya ndi za chakumwa. Mudzapereke zimenezi pa guwa lansembe la Nyumba ya Mulungu wanu ya ku Yerusalemu.
ukuthi uthenge masinyane ngalimali izinkunzi, izinqama, amawundlu, leminikelo yakho yokudla, leminikelo yakho yokunathwayo, ukunikele phezu kwelathi lendlu kaNkulunkulu wenu eseJerusalema.
18 Ndalama zotsala mudzagwiritse ntchito zimene inuyo ndi abale anu zikakukomerani malingana nʼkufuna kwa Mulungu wanu.
Lokukulungeleyo wena labafowenu ukukwenza ngesiliva legolide eliseleyo, kwenzeni lokhu ngokwentando kaNkulunkulu wenu.
19 Ziwiya zonse zimene akupatsani kuti mukatumikire nazo mʼNyumba ya Mulungu wanu, kaziperekeni kwa Mulungu ku Yerusalemu.
Lezitsha ezinikelwe kuwe zomsebenzi wendlu kaNkulunkulu wakho, zinikele ngokupheleleyo phambi kukaNkulunkulu weJerusalema.
20 Ndipo chilichonse chimene chingafunike mʼNyumba ya Mulungu wanu, chimene mudzapeze mpata wopereka, ndalama zake zogulira zidzachokere mʼthumba la chuma cha mfumu.
Lokunye okuswelekayo endlini kaNkulunkulu wakho okufanele ukuphe, uzakunika kuvela endlini yenotho yenkosi.
21 Tsopano Ine, mfumu Aritasasita, ndikulamula asungichuma onse a dera la Patsidya pa Yufurate kuti, chilichonse chimene wansembe Ezara, mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba adzapempha kwa inu, mupatseni mwa msanga.
Mina-ke Athakisekisi inkosi, umlayo umiswe yimi kubo bonke abaphathi bezikhwama abangaphetsheya komfula ukuthi konke uEzra umpristi, umbhali womlayo kaNkulunkulu wamazulu, azakucela kini, kwenziwe masinyane,
22 Ngakhale atafunika makilogalamu 3,400 asiliva, makilogalamu 10,000 a tirigu, malita 2,000 a vinyo, malita 2,000 a mafuta ndi mchere wochuluka motani, zonsezi mupereke monga zingafunikire.
kuze kufike kumathalenta esiliva alikhulu, njalo kuze kufike kumakhori engqoloyi alikhulu, njalo kuze kufike kumabhathi alikhulu ewayini, njalo kuze kufike kumabhathi alikhulu amafutha, letshwayi elingelasimiso.
23 Chimene Mulungu Wakumwamba walamula, chichitike mosamalitsa ku Nyumba ya Mulungu Wakumwamba kuopa kuti mkwiyo wa Mulungu ungayakire mfumu, dziko lake ndi ana ake.
Konke okungokomlayo kaNkulunkulu wamazulu kakwenzelwe indlu kaNkulunkulu wamazulu ngokukhuthala, ngoba kungani kuzakuba lolaka phezu kombuso wenkosi lamadodana ayo?
24 Tikukudziwitsaninso kuti kudzakhala kosaloledwa kukhometsa msonkho uliwonse anthu awa: ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda kapena aliyense wogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu.
Futhi siyalazisa mayelana labo bonke abapristi, lamaLevi, abahlabeleli, abalindimasango, amaNethini, lenceku zalindlu kaNkulunkulu, kakulagunya ukubeka phezu kwabo umthelo, imali eyimfanelo, lemali yendlela.
25 Ndipo iwe, Ezara, monga mwa nzeru za Mulungu wako zimene uli nazo, usankhe oyendetsa zinthu ndi oweruza kuti azilamulira anthu onse okhala ku dera la Patsidya pa Yufurate, onse amene amadziwa malamulo a Mulungu wako. Ndipo uphunzitse aliyense amene sawadziwa.
Wena-ke Ezra, ngokwenhlakanipho kaNkulunkulu wakho esesandleni sakho, beka omantshi labahluleli abazakwahlulela bonke abantu abangaphetsheya komfula, bonke abayaziyo imilayo kaNkulunkulu wakho; longayaziyo limfundise.
26 Ndipo amene sadzamvera lamulo la Mulungu wako ndi lamulo la mfumu alangidwe kolimba kapena aphedwe kapena achotsedwe mʼdzikolo, kapena katundu wake alandidwe, kapena aponyedwe mʼndende.
Wonke-ke ongawenziyo umlayo kaNkulunkulu wakho lomlayo wenkosi, isigwebo kasenziwe ngokukhuthala phezu kwakhe, kungaba ngokufa, loba ngokuxotshwa, loba ngokuthathelwa impahla, loba ngezibopho.
27 Ezara anati atamandike Yehova, Mulungu wa makolo athu, amene wayika ichi mu mtima wa mfumu kuti alemekeze Nyumba ya Yehova ya ku Yerusalemu mʼnjira imeneyi.
Kayibusiswe iNkosi uNkulunkulu wabobaba eyakufaka kanje enhliziyweni yenkosi ukucecisa indlu yeNkosi eseJerusalema,
28 Ameneyonso waonetsa chikondi chake chosasinthika kwa ine pamaso pa mfumu, alangizi ake ndi nduna zake zamphamvu kuti andikomere mtima. Choncho ndinalimba mtima popeza Yehova, Mulungu wanga anali nane, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri ambiri a Israeli kuti apite nane pamodzi.
eyelule umusa kimi phambi kwenkosi labacebisi bayo laphambi kwazo zonke izinduna ezilamandla zenkosi. Mina-ke ngaqiniswa ngokwesandla seNkosi uNkulunkulu wami phezu kwami, ngabutha koIsrayeli inhloko ukwenyuka lami.

< Ezara 7 >