< Ezara 7 >

1 Zitatha izi, Aritasasita ali mfumu ya ku Perisiya, panali wansembe wina dzina lake Ezara. Iyeyu abambo ake anali Seraya mwana wa Azariya, mwana wa Hilikiya,
Ngemva kwalezizinto, ngesikhathi sokubusa kuka-Athazekisisi inkosi yasePhezhiya, u-Ezra indodana kaSeraya, indodana ka-Azariya, indodana kaHilikhiya,
2 mwana wa Salumu, mwana wa Zadoki, mwana wa Ahitubi,
indodana kaShalumi, indodana kaZadokhi indodana ka-Ahithubi,
3 mwana wa Amariya, mwana wa Azariya, mwana wa Merayoti,
indodana ka-Amariya, indodana ka-Azariya, indodana kaMerayothi,
4 mwana wa Zerahiya, mwana wa Uzi, mwana wa Buki,
indodana kaZerahiya, indodana ka-Uzi, indodana kaBhukhi,
5 mwana wa Abisuwa, mwana wa Finehasi, mwana wa Eliezara, mwana wa Aaroni mkulu wa ansembe uja.
indodana ka-Abhishuwa, indodana kaFinehasi, indodana ka-Eliyazari, indodana ka-Aroni umphristi omkhulu,
6 Ezara ameneyu anabwera kuchokera ku Babuloni. Iyeyu anali wophunzira kwambiri za malamulo a Mose, amene Yehova Mulungu wa Israeli anapereka. Mfumu inamupatsa chilichonse chimene anapempha pakuti dzanja la Yehova Mulungu wake linali pa iye.
u-Ezra lo weza evela eBhabhiloni. Wayeyisifundiswa esazi kakhulu ngoMthetho kaMosi, owawuphiwe nguThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli. Inkosi yayimuphe konke ayekucelile, ngoba isandla sikaThixo uNkulunkulu wakhe sasiphezu kwakhe.
7 Tsono mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wa Aritasasita, Ezara pamodzi ndi Aisraeli ena, kuphatikizapo ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda, ndi anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ananyamuka kubwerera ku Yerusalemu.
Abanye abako-Israyeli, labaphristi, lamaLevi, labahlabeleli, labalindi bamasango lezinceku zethempelini labo babuya eJerusalema ngomnyaka wesikhombisa wokubusa kwenkosi u-Athazekisisi.
8 Ezara anafika ku Yerusalemu pa mwezi wachisanu wa chaka chachisanu ndi chiwiri cha mfumu.
U-Ezra wafika eJerusalema ngenyanga yesihlanu ngomnyaka wesikhombisa wenkosi.
9 Iye anayamba ulendo wochoka ku Babuloni pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, ndipo anafika ku Yerusalemu pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu chifukwa dzanja labwino la Mulungu wake linali pa iye.
Wayeqalise uhambo lwakhe esuka eBhabhiloni ngelanga lakuqala lenyanga yokuqala, wafika eJerusalema ngelanga lakuqala lenyanga yesihlanu, ngoba isandla somusa sikaNkulunkulu sasiphezu kwakhe.
10 Popeza Ezara anadzipereka kuwerenga ndi kusunga malamulo a Yehova, iye anafunitsitsa kuphunzitsa Aisraeli malamulo ndi malangizo a Mulungu.
Ngoba u-Ezra wayezinikele ekufundeni lokugcina uMthetho kaThixo lokufundisa izimiso zawo ko-Israyeli.
11 Iyi ndi kalata imene mfumu Aritasasita anapereka kwa wansembe Ezara, mlembi wa malamulo, munthu wophunzira kwambiri zokhudza malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Nansi incwadi iNkosi u-Athazekisisi ayeyiphe u-Ezra umphristi lomabhalane, indoda eyayifundile ezindabeni zemithetho lezimiso zikaThixo ku-Israyeli:
12 Ndine Aritasasita, mfumu ya mafumu. Ndikulembera iwe Ezara wansembe ndi mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba. Malonje.
Athazekisisi, nkosi yamakhosi, Ku-Ezra umphristi, umfundisi womthetho kaNkulunkulu wasezulwini: Ngiyabingelela.
13 Tsopano ndikulamula kuti Mwisraeli aliyense, wansembe kapena Mlevi wokhala mʼdziko langa, amene akufuna kupita ku Yerusalemu ndi iwe, apite.
Manje-ke ngimisa umthetho wokuthi ingqe ngubani wako-Israyeli osembusweni wami, kugoqela abaphristi labaLevi, ofisa ukuhamba lawe eJerusalema, kahambe.
14 Ine mfumu pamodzi ndi alangizi anga asanu ndi awiri tikukutumani kuti mukafufuze za dziko la Yuda ndi mzinda wa Yerusalemu kuti mukaone mmene anthu akutsatira malamulo a Mulungu wanu, amene anawapereka kwa inu.
Uthunywa yinkosi labacebisi bayo abayisikhombisa ukuba uyofunisisa ngoJuda langeJerusalema mayelana loMthetho kaNkulunkulu wakho, owuphetheyo.
15 Utenge siliva ndi golide zimene ine mfumu ndi alangizi anga tapereka mwa ufulu kwa Mulungu wa Israeli, amene amakhala ku Yerusalemu.
Njalo ubothatha isiliva legolide elinikwe ngesihle yinkosi labacebisi bayo kuNkulunkulu ka-Israyeli, ohlala eJerusalema,
16 Mutengenso siliva yense ndi golide amene mungamupeze mʼdziko lonse la Babuloni, ngakhalenso zinthu zimene anthu pamodzi ndi ansembe adzapereka mwaufulu kuperekera ku Nyumba ya Mulungu wawo ya ku Yerusalemu.
kanye lesiliva legolide lonke ongalizuza elizweni laseBhabhiloni kanye leminikelo yokuzizwela eyabantu labaphristi benikelela ithempeli likaNkulunkulu wabo eJerusalema.
17 Ndi ndalama zimenezi mudzaonetsetse kuti mwagula ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa aamuna pamodzi ndi zopereka zake za chakudya ndi za chakumwa. Mudzapereke zimenezi pa guwa lansembe la Nyumba ya Mulungu wanu ya ku Yerusalemu.
Ngaleyomali umele uthenge inkunzi, lenqama, lamazinyane ezimvu amaduna, ndawonye leminikelo yabo yamabele leyokunathwayo, konke kunikelwe e-alithareni lethempeli likaNkulunkulu wenu eJerusalema.
18 Ndalama zotsala mudzagwiritse ntchito zimene inuyo ndi abale anu zikakukomerani malingana nʼkufuna kwa Mulungu wanu.
Wena labazalwane bakho abangamaJuda selingenza lokho okuyabe kufanele ngesiliva legolide eliseleyo, mayelana lentando kaNkulunkulu wenu.
19 Ziwiya zonse zimene akupatsani kuti mukatumikire nazo mʼNyumba ya Mulungu wanu, kaziperekeni kwa Mulungu ku Yerusalemu.
Hambisani kuNkulunkulu weJerusalema zonke impahla eliziphathisiweyo ezokukhonza ethempelini likaNkulunkulu wenu.
20 Ndipo chilichonse chimene chingafunike mʼNyumba ya Mulungu wanu, chimene mudzapeze mpata wopereka, ndalama zake zogulira zidzachokere mʼthumba la chuma cha mfumu.
Akuthi loba yini efunekayo ethempelini likaNkulunkulu wenu elifuna ukuthi izuzakale, kayidingwe ngendleko ephuma esikhwameni senkosi.
21 Tsopano Ine, mfumu Aritasasita, ndikulamula asungichuma onse a dera la Patsidya pa Yufurate kuti, chilichonse chimene wansembe Ezara, mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba adzapempha kwa inu, mupatseni mwa msanga.
Mina, iNkosi Athazekisisi ngimisa umthetho wokuthi bonke abaphathi bezikhwama abangaphetsheya kweYufrathe baphe u-Ezra umphristi, umfundisi woMthetho kaNkulunkulu wasezulwini ngokuphangisa loba yini ayicelayo kini,
22 Ngakhale atafunika makilogalamu 3,400 asiliva, makilogalamu 10,000 a tirigu, malita 2,000 a vinyo, malita 2,000 a mafuta ndi mchere wochuluka motani, zonsezi mupereke monga zingafunikire.
kuze kube ngamathalenta esiliva alikhulu, lamasaka alikhulu engqoloyi, imigqomo elikhulu yewayini, imigqomo elikhulu yamafutha e-oliva, letswayi elingelakulinganiswa.
23 Chimene Mulungu Wakumwamba walamula, chichitike mosamalitsa ku Nyumba ya Mulungu Wakumwamba kuopa kuti mkwiyo wa Mulungu ungayakire mfumu, dziko lake ndi ana ake.
Ingqe yini emiswe nguNkulunkulu wasezulwini, kakwenziwe ngokukhuthala kusenzelwa ithempeli likaNkulunkulu wasezulwini. Kakudingeki ukuthi ulaka luze lwehliselwe phezu kwenkosi lamadodana ayo.
24 Tikukudziwitsaninso kuti kudzakhala kosaloledwa kukhometsa msonkho uliwonse anthu awa: ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda kapena aliyense wogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu.
Yazini njalo ukuthi kalilamvumo yokubiza imithelo loba inkongozelo yenkosi kumbe imbadalo yokungenisa impahla elizweni kubaphristi, labaLevi, labahlabeleli, labalindimasango, lezinceku zethempelini loba kwezinye izisebenzi zale indlu kaNkulunkulu.
25 Ndipo iwe, Ezara, monga mwa nzeru za Mulungu wako zimene uli nazo, usankhe oyendetsa zinthu ndi oweruza kuti azilamulira anthu onse okhala ku dera la Patsidya pa Yufurate, onse amene amadziwa malamulo a Mulungu wako. Ndipo uphunzitse aliyense amene sawadziwa.
Yikho wena Ezra, ngokuhlakanipha olakho okukaNkulunkulu wakho, beka abathonisi labehluleli ukwahlulela kuhle bonke abantu abangaphetsheya kweYufrathe, bonke abayaziyo imithetho kaNkulunkulu wenu. Kumele ufundise labo abangayaziyo.
26 Ndipo amene sadzamvera lamulo la Mulungu wako ndi lamulo la mfumu alangidwe kolimba kapena aphedwe kapena achotsedwe mʼdzikolo, kapena katundu wake alandidwe, kapena aponyedwe mʼndende.
Lowo ongawulaleliyo umthetho kaNkulunkulu wenu lomthetho wenkosi ngeqiniso umele ajeziswe ngokufa, loba ngokuxotshwa, loba ngokuhluthunelwa impahla loba ngokufakwa entolongweni.
27 Ezara anati atamandike Yehova, Mulungu wa makolo athu, amene wayika ichi mu mtima wa mfumu kuti alemekeze Nyumba ya Yehova ya ku Yerusalemu mʼnjira imeneyi.
Udumo kalube kuThixo, uNkulunkulu wabokhokho bethu, okufakileyo enhliziyweni yenkosi ukuletha inhlonipho endlini kaThixo eJerusalema ngale indlela
28 Ameneyonso waonetsa chikondi chake chosasinthika kwa ine pamaso pa mfumu, alangizi ake ndi nduna zake zamphamvu kuti andikomere mtima. Choncho ndinalimba mtima popeza Yehova, Mulungu wanga anali nane, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri ambiri a Israeli kuti apite nane pamodzi.
njalo otshengise umusa wakhe kini phambi kwenkosi labeluleki bakhe lazozonke izinduna zakhe ezilamandla. Ngenxa yokuthi isandla sikaThixo uNkulunkulu wami besiphezu kwami, ngaba lesibindi ngaqoqa amadoda angabakhokheli ko-Israyeli ukuthi bahambe lami.

< Ezara 7 >