< Ezara 7 >
1 Zitatha izi, Aritasasita ali mfumu ya ku Perisiya, panali wansembe wina dzina lake Ezara. Iyeyu abambo ake anali Seraya mwana wa Azariya, mwana wa Hilikiya,
Kalpasan dagitoy a banbanag, kabayatan ti panagturay ni Ari Artaxerxes, dagiti kapuonan ni Ezra ket da Seraias, Azarias, Hilkias,
2 mwana wa Salumu, mwana wa Zadoki, mwana wa Ahitubi,
Sallum, Zadok, Ahitub,
3 mwana wa Amariya, mwana wa Azariya, mwana wa Merayoti,
Amarias, Azarias, Merayot,
4 mwana wa Zerahiya, mwana wa Uzi, mwana wa Buki,
Zerahias, Uzzi, Bukki,
5 mwana wa Abisuwa, mwana wa Finehasi, mwana wa Eliezara, mwana wa Aaroni mkulu wa ansembe uja.
Abisua, Finees, Eleazar, kalpasanna ni Aaron a kangatoan a padi—
6 Ezara ameneyu anabwera kuchokera ku Babuloni. Iyeyu anali wophunzira kwambiri za malamulo a Mose, amene Yehova Mulungu wa Israeli anapereka. Mfumu inamupatsa chilichonse chimene anapempha pakuti dzanja la Yehova Mulungu wake linali pa iye.
Pimmanaw ni Ezra manipud Babilonia. Nalaing isuna nga eskriba iti linteg ni Moises nga inted ni Yahweh a Dios ti Israel. Inted ti ari kenkuana ti aniaman a dinawatna agsipud ta adda kenkuana ti ima ni Yahweh.
7 Tsono mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wa Aritasasita, Ezara pamodzi ndi Aisraeli ena, kuphatikizapo ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda, ndi anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ananyamuka kubwerera ku Yerusalemu.
Iti maikapito a tawen a panagturay ni Ari Artaxerxes, simmang-at met idiay Jerusalem dagiti sumagmamano a kaputotan ni Israel ken dagiti padi, dagiti Levita, dagiti kumakanta iti templo, dagiti mangbanbantay iti ruangan, ken dagiti nadutokan nga agserbi iti templo.
8 Ezara anafika ku Yerusalemu pa mwezi wachisanu wa chaka chachisanu ndi chiwiri cha mfumu.
Nakadanon isuna idiay Jerusalem iti maikalima a bulan iti isu met laeng a tawen.
9 Iye anayamba ulendo wochoka ku Babuloni pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, ndipo anafika ku Yerusalemu pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu chifukwa dzanja labwino la Mulungu wake linali pa iye.
Pimmanaw isuna idiay Babilonia iti umuna nga aldaw iti umuna a bulan. Simmangpet isuna idiay Jerusalem idi umuna nga aldaw iti maikalima a bulan, agsipud ta adda kenkuana ti naimbag nga ima ti Dios.
10 Popeza Ezara anadzipereka kuwerenga ndi kusunga malamulo a Yehova, iye anafunitsitsa kuphunzitsa Aisraeli malamulo ndi malangizo a Mulungu.
Impapuso ni Ezra a nang-adal, nangaramid, ken nangisuro dagiti annuroten ken dagiti naipaulog a linteg ni Yahweh.
11 Iyi ndi kalata imene mfumu Aritasasita anapereka kwa wansembe Ezara, mlembi wa malamulo, munthu wophunzira kwambiri zokhudza malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Daytoy ti naipaulog a linteg nga inted ni Ari Artaxerxes kenni Ezra a padi ken eskriba dagiti bilin ken alagaden ni Yahweh para iti Israel:
12 Ndine Aritasasita, mfumu ya mafumu. Ndikulembera iwe Ezara wansembe ndi mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba. Malonje.
“Manipud iti Ari dagiti ari a ni Artaxerxes, nga agpaay kenni Ezra a padi, nga eskriba ti linteg ti Dios ti langit:
13 Tsopano ndikulamula kuti Mwisraeli aliyense, wansembe kapena Mlevi wokhala mʼdziko langa, amene akufuna kupita ku Yerusalemu ndi iwe, apite.
Ibilbilinko a siasinoman iti pagariak ti naggapu idiay Israel, agraman dagiti papadida ken dagiti Levita nga agtartarigagay a mapan idiay Jerusalem, ket mabalin a sumurot kenka.
14 Ine mfumu pamodzi ndi alangizi anga asanu ndi awiri tikukutumani kuti mukafufuze za dziko la Yuda ndi mzinda wa Yerusalemu kuti mukaone mmene anthu akutsatira malamulo a Mulungu wanu, amene anawapereka kwa inu.
Siak, nga ari, ken dagiti pito a mammagbagak, ibaonkayo amin a mangsukimat ti maipapan iti Juda ken Jerusalem, a maiyannurot iti linteg ti Dios a naawatanyo,
15 Utenge siliva ndi golide zimene ine mfumu ndi alangizi anga tapereka mwa ufulu kwa Mulungu wa Israeli, amene amakhala ku Yerusalemu.
ket tapno maiyegyo ti pirak ken balitok nga indatonda iti Dios ti Israel idiay Jerusalem, ti pagtaenganna.
16 Mutengenso siliva yense ndi golide amene mungamupeze mʼdziko lonse la Babuloni, ngakhalenso zinthu zimene anthu pamodzi ndi ansembe adzapereka mwaufulu kuperekera ku Nyumba ya Mulungu wawo ya ku Yerusalemu.
Itedyo amin a pirak ken balitok nga inted dagiti amin a taga-Babilonia agraman ti inted dagiti tattao ken dagiti padi para iti balay ti Dios idiay Jerusalem.
17 Ndi ndalama zimenezi mudzaonetsetse kuti mwagula ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa aamuna pamodzi ndi zopereka zake za chakudya ndi za chakumwa. Mudzapereke zimenezi pa guwa lansembe la Nyumba ya Mulungu wanu ya ku Yerusalemu.
Isu a gumatangka kadagiti baka, kalakian ken urbon a karnero, trigo ken daton a mainom. Idatonyo dagitoy iti rabaw ti altar iti balay ti Diosyo idiay Jerusalem.
18 Ndalama zotsala mudzagwiritse ntchito zimene inuyo ndi abale anu zikakukomerani malingana nʼkufuna kwa Mulungu wanu.
Aramidem ken dagiti kakabsatmo a lallaki ti ammom a nasayaat para iti natidda a pirak ken balitok, tapno maay-ayo ti Diosyo.
19 Ziwiya zonse zimene akupatsani kuti mukatumikire nazo mʼNyumba ya Mulungu wanu, kaziperekeni kwa Mulungu ku Yerusalemu.
Idatagmo dagiti alikamen a siwawaya a naited kenka iti sangoananna para iti panagserbi iti balay ti Diosyo idiay Jerusalem.
20 Ndipo chilichonse chimene chingafunike mʼNyumba ya Mulungu wanu, chimene mudzapeze mpata wopereka, ndalama zake zogulira zidzachokere mʼthumba la chuma cha mfumu.
Aniaman a masapul para iti balay ti Diosyo a kasapulam, alaem ti bayadna manipud iti pagiduldulinan ti gamengko.
21 Tsopano Ine, mfumu Aritasasita, ndikulamula asungichuma onse a dera la Patsidya pa Yufurate kuti, chilichonse chimene wansembe Ezara, mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba adzapempha kwa inu, mupatseni mwa msanga.
Siak ni Artaxerxes nga Ari, nangaramidak iti bilin kadagiti amin a tesorero iti ballasiw ti Karayan, nga aniaman a dawaten ni Ezra kadakayo ket nasken nga itedyo a naan-anay
22 Ngakhale atafunika makilogalamu 3,400 asiliva, makilogalamu 10,000 a tirigu, malita 2,000 a vinyo, malita 2,000 a mafuta ndi mchere wochuluka motani, zonsezi mupereke monga zingafunikire.
agingga iti sangagasut a talento a pirak, sangagasut a kasukat a trigo, sangagasut a bat nga arak, ken sangagasut a bat ti lana kasta met ti aglaplapusanan nga asin.
23 Chimene Mulungu Wakumwamba walamula, chichitike mosamalitsa ku Nyumba ya Mulungu Wakumwamba kuopa kuti mkwiyo wa Mulungu ungayakire mfumu, dziko lake ndi ana ake.
Aniaman a bilin manipud ti Dios iti Langit, aramidenyo daytoy a naan-anay para iti balayna. Ta apay koma nga umay ti pungtotna iti pagariak ken kadagiti annakko a lallaki?
24 Tikukudziwitsaninso kuti kudzakhala kosaloledwa kukhometsa msonkho uliwonse anthu awa: ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda kapena aliyense wogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu.
Ipakpakaammomi kadakuada a saankayo a mangsingsingir iti aniaman a buwis iti siasinoman kadagiti padi, kadagiti Levita, kadagiti kumakanta, kadagiti mangbanbantay iti ruangan, wenno kadagiti tattao a nadutokan nga agserbi iti templo ken kadagiti adipen iti daytoy balay ti Dios.
25 Ndipo iwe, Ezara, monga mwa nzeru za Mulungu wako zimene uli nazo, usankhe oyendetsa zinthu ndi oweruza kuti azilamulira anthu onse okhala ku dera la Patsidya pa Yufurate, onse amene amadziwa malamulo a Mulungu wako. Ndipo uphunzitse aliyense amene sawadziwa.
Sika Ezra, babaen iti sirib nga inted kenka ti Dios, masapul a mangdutokka kadagiti ukom ken nasirib a tattao nga agserbi kadagiti amin a tattao iti ballasiw ti Karayan, ken agserbi iti siasinoman a makaammo ti linteg ti Diosmo. Masapul met a suroam dagiti saan a makaamo iti linteg.
26 Ndipo amene sadzamvera lamulo la Mulungu wako ndi lamulo la mfumu alangidwe kolimba kapena aphedwe kapena achotsedwe mʼdzikolo, kapena katundu wake alandidwe, kapena aponyedwe mʼndende.
Dusaem ti siasinoman a saan a naan-anay nga agtultulnog iti linteg ti Dios wenno iti linteg ti ari, uray babaen iti pannakapapatay, iti pannakaibelleng, iti pannakasamsam dagiti sanikuada, wenno pannakaibalud.”
27 Ezara anati atamandike Yehova, Mulungu wa makolo athu, amene wayika ichi mu mtima wa mfumu kuti alemekeze Nyumba ya Yehova ya ku Yerusalemu mʼnjira imeneyi.
Kinuna ni Ezra “Madaydayaw ni Yahweh a Dios dagiti kapuonantayo, a nangtignay iti puso ti ari tapno mangdayaw iti balay ni Yahweh idiay Jerusalem
28 Ameneyonso waonetsa chikondi chake chosasinthika kwa ine pamaso pa mfumu, alangizi ake ndi nduna zake zamphamvu kuti andikomere mtima. Choncho ndinalimba mtima popeza Yehova, Mulungu wanga anali nane, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri ambiri a Israeli kuti apite nane pamodzi.
ken ti nangipaay ti kinapudnona iti tulagna kaniak iti sangoanan ti ari, dagiti mammagbagana, ken dagiti amin a mannakabalin nga opisialna. Napabilegak babaen iti ima ni Yahweh a Diosko, ket inummongko dagiti mangidadaulo manipud iti Israel tapno kumuyog kaniak.”