< Ezara 7 >

1 Zitatha izi, Aritasasita ali mfumu ya ku Perisiya, panali wansembe wina dzina lake Ezara. Iyeyu abambo ake anali Seraya mwana wa Azariya, mwana wa Hilikiya,
He kah olka hnukah Persia manghai Artaxerxes kah ram ah Hilkiah koca Azariah kah a ca, Seraiah capa Ezra.
2 mwana wa Salumu, mwana wa Zadoki, mwana wa Ahitubi,
Shallum capa Hilkiah, Zadok capa Shallum, Ahitub capa Zadok.
3 mwana wa Amariya, mwana wa Azariya, mwana wa Merayoti,
Amariah capa Ahitub, Azariah capa, Meraioth capa Azariah.
4 mwana wa Zerahiya, mwana wa Uzi, mwana wa Buki,
Zerahiah capa Meraioth, Uzzi capa Zerahiah, Bukki capa Uzzi.
5 mwana wa Abisuwa, mwana wa Finehasi, mwana wa Eliezara, mwana wa Aaroni mkulu wa ansembe uja.
Abishua capa Bukki, Phinekha capa Abishua, Eleazar capa Phinekha, khosoih boeilu Aaron capa Eleazar.
6 Ezara ameneyu anabwera kuchokera ku Babuloni. Iyeyu anali wophunzira kwambiri za malamulo a Mose, amene Yehova Mulungu wa Israeli anapereka. Mfumu inamupatsa chilichonse chimene anapempha pakuti dzanja la Yehova Mulungu wake linali pa iye.
Ezra he Babylon lamloh a mael vaengah Moses olkhueng dongkah a cadaek te amah loh a ming. Te te Israel Pathen BOEIPA loh a paek. A Pathen BOEIPA kut loh anih soah a om dongah a kueknah boeih te manghai loh a taengah a paek.
7 Tsono mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wa Aritasasita, Ezara pamodzi ndi Aisraeli ena, kuphatikizapo ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda, ndi anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ananyamuka kubwerera ku Yerusalemu.
Te vaengah Israel ca rhoek lamkah khaw, khosoih neh Levi lamkah khaw, laa sa neh thoh tawt khaw, tamtaeng rhoek khaw manghai Artaxerxes kah a kum rhih vaengah tah Jerusalem la cet uh.
8 Ezara anafika ku Yerusalemu pa mwezi wachisanu wa chaka chachisanu ndi chiwiri cha mfumu.
Manghai kah kum rhih nah hla nga vaengah tah Jerusalem pawk.
9 Iye anayamba ulendo wochoka ku Babuloni pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, ndipo anafika ku Yerusalemu pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu chifukwa dzanja labwino la Mulungu wake linali pa iye.
Hla khat dongkah lamhmacuek hnin vaengah Babylon lamkah tangtlaeng a tongnah lamloh hla nga dongkah lamhmacuek hnin ah tah Jerusalem ah pawk. A Pathen kah kut tah anih soah then tangloeng.
10 Popeza Ezara anadzipereka kuwerenga ndi kusunga malamulo a Yehova, iye anafunitsitsa kuphunzitsa Aisraeli malamulo ndi malangizo a Mulungu.
Ezra he BOEIPA olkhueng thuep ham neh vai ham khaw, Israel khuiah oltlueh neh laitloeknah tukkil ham khaw a thinko cikngae.
11 Iyi ndi kalata imene mfumu Aritasasita anapereka kwa wansembe Ezara, mlembi wa malamulo, munthu wophunzira kwambiri zokhudza malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
He kah capat catlaep he manghai Artaxerxes loh BOEIPA kah olpaek ol neh Israel ham a oltlueh dongkah cadaek saya, khosoih Ezra taengah a paek.
12 Ndine Aritasasita, mfumu ya mafumu. Ndikulembera iwe Ezara wansembe ndi mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba. Malonje.
Manghai boeih kah manghai Artaxerxes loh vaan Pathen kah oltlueh cadaek khosoih Ezra tah a yoethen pai.
13 Tsopano ndikulamula kuti Mwisraeli aliyense, wansembe kapena Mlevi wokhala mʼdziko langa, amene akufuna kupita ku Yerusalemu ndi iwe, apite.
Ka ram khui kah a puhlu boeih ham kai lamloh saithainah ka paek coeng. Israel pilnam neh a khosoih rhoek khaw, Levi khaw Jerusalem la caeh ham nang m'puei saeh.
14 Ine mfumu pamodzi ndi alangizi anga asanu ndi awiri tikukutumani kuti mukafufuze za dziko la Yuda ndi mzinda wa Yerusalemu kuti mukaone mmene anthu akutsatira malamulo a Mulungu wanu, amene anawapereka kwa inu.
He kong dongah Manghai neh anih kah olrhoep parhih taeng lamloh Judah taeng neh Jerusalem taengah na kut dongkah na Pathen oltlueh te thoelh hamla a pat coeng.
15 Utenge siliva ndi golide zimene ine mfumu ndi alangizi anga tapereka mwa ufulu kwa Mulungu wa Israeli, amene amakhala ku Yerusalemu.
Amah kolhmuen Jerusalem kah Israel Pathen taengah manghai neh a olrhoep rhoek loh a puhlu cak neh sui khaw khuen ham om.
16 Mutengenso siliva yense ndi golide amene mungamupeze mʼdziko lonse la Babuloni, ngakhalenso zinthu zimene anthu pamodzi ndi ansembe adzapereka mwaufulu kuperekera ku Nyumba ya Mulungu wawo ya ku Yerusalemu.
Cak neh sui boeih te Babylon paeng pum ah na hmuh bitni. Jerusalem kah a Pathen im ham tah pilnam khaw a puhlu tih khosoih rhoek long khaw a puhlu.
17 Ndi ndalama zimenezi mudzaonetsetse kuti mwagula ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa aamuna pamodzi ndi zopereka zake za chakudya ndi za chakumwa. Mudzapereke zimenezi pa guwa lansembe la Nyumba ya Mulungu wanu ya ku Yerusalemu.
He kong ah tangka nen he vaito, tutal, tuca khaw, a khosaa neh a tuisi khaw tluem tluem lai. Te te Jerusalem ah na Pathen im kah hmueihtuk dongah nawn.
18 Ndalama zotsala mudzagwiritse ntchito zimene inuyo ndi abale anu zikakukomerani malingana nʼkufuna kwa Mulungu wanu.
Namah taengkah neh na manuca taengkah boeih te tah cak khaw, sui khaw a coih nen te a then la saii lamtah na Pathen kah ngaihnah bangla saii uh.
19 Ziwiya zonse zimene akupatsani kuti mukatumikire nazo mʼNyumba ya Mulungu wanu, kaziperekeni kwa Mulungu ku Yerusalemu.
Te hnopai te na Pathen im kah thothuengnah ham nang taengah kam paek. Te te Jerusalem kah Pathen taengah cum coeng.
20 Ndipo chilichonse chimene chingafunike mʼNyumba ya Mulungu wanu, chimene mudzapeze mpata wopereka, ndalama zake zogulira zidzachokere mʼthumba la chuma cha mfumu.
Na Pathen im kah a tloe a ngoe dongah thoh hamla nang soah aka tla te tah manghai cabu im lamkah te thoo mai.
21 Tsopano Ine, mfumu Aritasasita, ndikulamula asungichuma onse a dera la Patsidya pa Yufurate kuti, chilichonse chimene wansembe Ezara, mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba adzapempha kwa inu, mupatseni mwa msanga.
Manghai Artaxerxes kai kamah lamloh sok paem kah hnokhoem boeih taengah saithainah ka paek. A cungkuem dongah vaan Pathen kah oltlueh cadaek khosoih Ezra nang n'dawt saeh lamtah tluem tluem saii.
22 Ngakhale atafunika makilogalamu 3,400 asiliva, makilogalamu 10,000 a tirigu, malita 2,000 a vinyo, malita 2,000 a mafuta ndi mchere wochuluka motani, zonsezi mupereke monga zingafunikire.
Cak talent yakhat hil, cangyen kore yakhat hil, misurtui bath yakhat hil, situi bath yakhat neh lungkaehtael toeklek toekna pawt hil tawn saeh.
23 Chimene Mulungu Wakumwamba walamula, chichitike mosamalitsa ku Nyumba ya Mulungu Wakumwamba kuopa kuti mkwiyo wa Mulungu ungayakire mfumu, dziko lake ndi ana ake.
Vaan Pathen kah saithainah lamkah boeih he vaan Pathen im dongah tluem tluem saii saeh. Balae tih kosi manghai kah ram neh a ca a bo thil eh.
24 Tikukudziwitsaninso kuti kudzakhala kosaloledwa kukhometsa msonkho uliwonse anthu awa: ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda kapena aliyense wogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu.
Te phoeiah khosoih boeih neh Levi khaw, laasa rhoek khaw, thoh tawt rhoek khaw, tamtaeng rhoek khaw, Pathen im kah tho aka thueng he khaw, mangmu neh hlang mangmu khaw, cawn khaw, amih soah coi ham saithainah om pawh tila namah taengah mingpha saeh.
25 Ndipo iwe, Ezara, monga mwa nzeru za Mulungu wako zimene uli nazo, usankhe oyendetsa zinthu ndi oweruza kuti azilamulira anthu onse okhala ku dera la Patsidya pa Yufurate, onse amene amadziwa malamulo a Mulungu wako. Ndipo uphunzitse aliyense amene sawadziwa.
Ezra nang khaw na Pathen kah cueihnah rhangneh na kut dongkah aka taemrhai ham neh laitloekung la m'hmoel coeng. Te tlam te a om uh daengah ni sok paem kah pilnam cungkuem taengah neh na Pathen oltlueh aka ming boeih taengah khaw, na ming bangla aka ming pawt taengah khaw lai aka tloek rhoek loh lai a tloek thai eh.
26 Ndipo amene sadzamvera lamulo la Mulungu wako ndi lamulo la mfumu alangidwe kolimba kapena aphedwe kapena achotsedwe mʼdzikolo, kapena katundu wake alandidwe, kapena aponyedwe mʼndende.
Na Pathen kah oltlueh neh manghai kah oltlueh aka vai pawt boeih te tah laitloeknah tluem tluem om saeh. Anih te dueknah nen khaw, haeknah nen khaw, a koe tuuknah nen khaw, pinnah nen khaw saii saeh.
27 Ezara anati atamandike Yehova, Mulungu wa makolo athu, amene wayika ichi mu mtima wa mfumu kuti alemekeze Nyumba ya Yehova ya ku Yerusalemu mʼnjira imeneyi.
Mamih napa rhoek kah Pathen Yahweh tah a yoethen pai saeh. Tahae kah bangla Jerusalem kah BOEIPA im te cam hamla manghai kah lungbuei ah a cuen sak.
28 Ameneyonso waonetsa chikondi chake chosasinthika kwa ine pamaso pa mfumu, alangizi ake ndi nduna zake zamphamvu kuti andikomere mtima. Choncho ndinalimba mtima popeza Yehova, Mulungu wanga anali nane, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri ambiri a Israeli kuti apite nane pamodzi.
Kai ham khaw manghai neh a olrhoep mikhmuh ah, hlangrhalh manghai kah mangpa boeih taengah khaw sitlohnah a tueng sak. Ka sokah kah ka Pathen BOEIPA kut rhangneh kamah khaw ka moem uh. Te dongah kamah neh aka puei la Israel boeilu te ka coi.

< Ezara 7 >