< Ezara 6 >

1 Atalandira mawuwo mfumu Dariyo anapereka lamulo ndipo kafukufuku anachitikadi ku Babuloni mʼnyumba yosungira chuma ndi mabuku ambiri yakale.
UDariyusi inkosi wasemisa umthetho, basebephenya endlini yezingwalo lapho okwakubekwe khona okuligugu eBhabhiloni.
2 Ndipo ku Ekibatana, likulu la dera la Mediya, kunapezeka mpukutu mmene munalembedwa kuti, Chikumbutso:
Kwasekutholakala eAkimetha, esigodlweni esisesigabeni samaMede, incwadi egoqwayo, okwakubhalwe phakathi kwayo isikhumbuzo ngalindlela:
3 Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi, mfumuyo inapereka lamulo lokhudza Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Analamula kuti Nyumba ya Mulungu imangidwenso kukhala malo woperekerako nsembe. Maziko ake amangidwe kolimba pa malo pomwe paja pali maziko ake akale ndipo mulitali mwake mukhale mamita 27, mulifupi mwake mukhale mamita 27.
Ngomnyaka wokuqala kaKoresi inkosi, uKoresi inkosi wamisa umthetho: Indlu kaNkulunkulu eseJerusalema, kayakhiwe lindlu endaweni lapho abanikela khona iminikelo, lezisekelo zayo zizabekwa ngokuqinileyo; ukuphakama kwayo kube zingalo ezingamatshumi ayisithupha, ububanzi bayo bube zingalo ezingamatshumi ayisithupha;
4 Mumange mizere itatu ya miyala yayikulu ndi mzere umodzi wa matabwa, ndalama zake zolipirira ntchitoyo zichokere mʼthumba la ufumu.
ibe lemizila emithathu yamatshe amakhulu lomzila wezigodo ezintsha. Izindleko zizaphiwa-ke zivela endlini yenkosi.
5 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu kupita nazo ku Babuloni, zonsezi zibwezedwe ndipo zipite ku Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Chilichonse chikabwezedwe pamalo pake mʼNyumbayo.
Futhi lezitsha zegolide lezesiliva zendlu kaNkulunkulu uNebhukadinezari azikhupha ethempelini eliseJerusalema waziletha eBhabhiloni, kazibuyiselwe zisiwe ethempelini eliseJerusalema, endaweni yayo, uzibeke endlini kaNkulunkulu.
6 Tsopano Tatenai, bwanamkubwa wa dera la Patsidya pa Yufurate ndiponso Setari-Bozenai pamodzi ndi anzanu muchokeko kumeneko.
Khathesi, Tathenayi, mbusi waphetsheya komfula, Shethari-Bozenayi, labangane benu amaAfarisathiki, abaphetsheya komfula, banini khatshana lalapho.
7 Ntchito yomanga Nyumba ya Mulunguyi muyileke. Mulekeni bwanamkubwa wa Ayuda ndiponso akuluakulu a Ayuda kuti amangenso Nyumba ya Mulunguyo pamalo pake.
Uyekeleni umsebenzi walindlu kaNkulunkulu; umbusi wamaJuda labadala bamaJuda kabakhe lindlu kaNkulunkulu endaweni yayo.
8 Kuwonjezera pamenepo, ndikukhazikitsa lamulo lonena za mmene mudzachitire ndi akuluakulu a Ayuda powathandiza kumanganso Nyumba ya Mulunguyo: Anthuwa muwalipire msanga kuchokera mʼthumba la ufumu, kuchotsa pa msonkho wa dera la Patsidya pa Yufurate.
Futhi umthetho umiswa yimi ngelizakwenzela abadala balamaJuda ekwakhiweni kwalindlu kaNkulunkulu, ukuthi empahleni zenkosi ezivela emthelweni wangaphetsheya komfula, izindleko ziphiwe lamadoda masinyane ukuze angami.
9 Ndipo zonse zofunikira monga, ana angʼombe, nkhosa zazimuna, ana ankhosa aamuna zoperekera nsembe yopsereza kwa Mulungu wakumwamba, ndi tirigu, mchere, vinyo ndi mafuta monga mmene ansembe a ku Yerusalemu angafunire, muziwapatsa zimenezo tsiku ndi tsiku ndipo musamalephere kutero.
Lokuswelakalayo, kokubili amajongosi lezinqama lamawundlu komnikelo wokutshiselwa uNkulunkulu wamazulu, ingqoloyi, itshwayi, iwayini, lamafutha, njengokutsho kwabapristi abaseJerusalema, kabakunikwe insuku ngensuku kungaphuthi,
10 Zikatero ndiye kuti azipereka nsembe za fungo lokomera Mulungu wakumwamba ndi kupempherera moyo wa mfumu ndi ana ake.
ukuze banikele iminikelo yephunga elimnandi kuNkulunkulu wamazulu, bakhulekele impilo yenkosi leyamadodana ayo.
11 Ndikulamulanso kuti ngati wina asintha zimene ndalamulazi, mtanda umodzi wa nyumba yake udzasololedwa ndi kumunkhomera pamenepo ndipo nyumba yake adzayisandutse dzala.
Futhi umthetho umiswe yimi wokuthi loba ngubani oguqula lelilizwi, kakuhwatshwe ugodo endlini yakhe, aphakanyiswe abethelwe phezu kwalo; lendlu yakhe yenziwe inqumbi yomquba ngenxa yalokhu.
12 Mulungu amene anasankha kuti anthu azimupembedza pa malo amenewa, achotse mfumu iliyonse kapena munthu aliyense amene adzasinthe zimenezi kapena kuwononga Nyumba ya Mulungu ya ku Yerusalemuko. Ine Dariyo ndikuyika lamuloli, aliyense alitsate mosamala kwambiri.
LoNkulunkulu owenze ibizo lakhe lihlale lapho kachithe loba yiyiphi inkosi loba abantu abazakwelula isandla sabo ukuguqula lokuchitha lindlu kaNkulunkulu eseJerusalema. Mina Dariyusi ngimise umthetho, kakwenziwe masinyane.
13 Tsono potsata zomwe analamula mfumu Dariyo, Tatenai bwanamkubwa wa dera la Patsidya pa Yufurate, Setari-Bozenai ndi anzawo anatsatira mosamala kwambiri zimene mfumu Dariyo analamula.
Khonokho uTathenayi umbusi nganeno komfula, uShethari-Bozenayi, labangane babo benza njalo masinyane njengalokho uDariyusi inkosi ayekuthumele.
14 Ndipo akuluakulu a Ayuda anapitiriza ntchito yomanga ija molimbikitsidwa ndi aneneri Hagai ndi Zekariya mwana wa Ido. Anamaliza ntchito yomanga Nyumbayo, monga momwe Mulungu wa Israeli analamulira ndiponso potsata lamulo la Koresi, Dariyo ndi Aritasasita, mafumu a ku Perisiya.
Abadala bamaJuda basebesakha njalo baphumelela ngesiprofetho sikaHagayi umprofethi loZekhariya indodana kaIdo. Bakha baqeda njengokomlayo kaNkulunkulu kaIsrayeli langokomlayo kaKoresi, loDariyusi, loAthakisekisi inkosi yePerisiya.
15 Anatsiriza kumanga Nyumbayo pa tsiku lachitatu la mwezi wa Adara mʼchaka chachisanu ndi chimodzi cha ulamuliro wa mfumu Dariyo.
Lindlu yasiphela ngosuku lwesithathu enyangeni kaAdari, okwakungumnyaka wesithupha wokubusa kukaDariyusi inkosi.
16 Choncho Aisraeli, ansembe, Alevi ndi anthu ena onse amene anali atabwerako ku ukapolo, anachita chikondwerero chopereka Nyumba ya Mulungu mwachimwemwe.
Abantwana bakoIsrayeli, abapristi lamaLevi labanye abantwana bokuthunjwa, basebesenza ukwehlukaniselwa kwalindlu kaNkulunkulu ngentokozo.
17 Poporeka Nyumba ya Mulunguyi, anthu anapereka nsembe za ngʼombe zazimuna 100, nkhosa zazimuna 200, ana ankhosa aamuna 400. Anaperekanso mbuzi zazimuna 12 ngati nsembe yopepesera machimo a anthu onse, potsata chiwerengero cha mafuko a Israeli.
Banikelela ukwehlukaniselwa kwalindlu kaNkulunkulu inkunzi ezilikhulu, inqama ezingamakhulu amabili, amawundlu angamakhulu amane; lezimpongo zezimbuzi ezilitshumi lambili zingumnikelo wesono kaIsrayeli wonke, ngokwenani lezizwe zakoIsrayeli.
18 Ndipo anakhazikitsa ansembe ndi Alevi pa ntchito zawo zotumikira Mulungu mu Yerusalemu monga zinalembedwera mʼbuku la Mose.
Basebemisa abapristi ngezigaba zabo, lamaLevi ngamaqembu awo, enkonzweni kaNkulunkulu eseJerusalema, njengokubhaliweyo egwalweni lukaMozisi.
19 Pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba, obwera ku ukapolo aja anachita chikondwerero cha Paska.
Abantwana bokuthunjwa benza lephasika ngolwetshumi lane lwenyanga yokuqala.
20 Ansembe ndi Alevi anali atadziyeretsa ndipo onsewo anali oyeretsedwa. Alevi anapha mwana wankhosa wa Paska kuphera onse amene anatuluka ku ukapolo, ansembe anzawo ndi iwo eni.
Ngoba abapristi lamaLevi babezihlambulule ndawonye, bonke babehlambulukile. Bahlabela bonke abantwana bokuthunjwa iphasika, labafowabo abapristi, labo ngokwabo.
21 Nkhosa ya Paskayo anayidya ndi Aisraeli onse amene anatuluka ku ukapolo, wina aliyense amene anaphatikana nawo atadziyeretsa ku zonyansa za mitundu ina ya anthu akunja a mʼdzikomo kuti apembedze Yehova Mulungu wa Israeli.
Ngokunjalo badla abantwana bakoIsrayeli ababebuyile ekuthunjweni, labo bonke ababezehlukanisele kubo lokungcolileyo kwezizwe zelizwe, ukudinga iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli.
22 Choncho pa masiku asanu ndi awiri anasangalala pa chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa Yehova anawadzaza ndi chimwemwe. Iye anatembenuza mtima wa mfumu ya ku Asiriya motero kuti iyo inakomera mtima Aisraeli ndi kuwathandiza ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu, Mulungu wa Israeli.
Benza umkhosi wesinkwa esingelamvubelo insuku eziyisikhombisa ngentokozo; ngoba iNkosi yayibenze bathokoza, yaphendulela kibo inhliziyo yenkosi yeAsiriya, ukuqinisa izandla zabo emsebenzini wendlu kaNkulunkulu, uNkulunkulu kaIsrayeli.

< Ezara 6 >