< Ezara 5 >

1 Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
Abaprofethi, oHagayi umprofethi loZekhariya indodana kaIdo, basebeprofetha kumaJuda ayekoJuda laseJerusalema, ebizweni likaNkulunkulu kaIsrayeli phezu kwawo.
2 Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
Khonokho kwasuka oZerubhabheli indodana kaSalatiyeli loJeshuwa indodana kaJozadaki, baqala ukwakha indlu kaNkulunkulu eseJerusalema, njalo kanye labo abaprofethi bakaNkulunkulu bebasekela.
3 Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
Ngalesosikhathi kwafika kibo oTathenayi umbusi nganeno komfula loShethari-Bozenayi, labangane babo, bakhuluma kanje kibo: Ngubani obeke umthetho kini wokwakha lindlu lokuqedisa lumduli?
4 Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
Sasesibatshela ngokunjalo: Ngobani amabizo abantu abakha lesisakhiwo?
5 Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
Kodwa ilihlo likaNkulunkulu wabo laliphezu kwabadala bamaJuda, ukuthi kababenzanga beme, ize ifike leyondaba kuDariyusi, baze babuyisele-ke incwadi ngayo.
6 Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
Ikhophi yencwadi oTathenayi umbusi nganeno komfula loShethari-Bozenayi labangane bakhe amaAfarisathiki ayenganeno komfula abayithumela kuDariyusi inkosi;
7 Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
bathumeza incwadi kuye, njalo kwabhalwa kanje kuyo: KuDariyusi inkosi, ukuthula konke.
8 Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
Kakwaziwe enkosini ukuthi saya esabelweni sakoJuda, endlini kaNkulunkulu omkhulu, eyakhiwe ngamatshe amakhulu, izigodo sezifakiwe emidulwini; njalo lumsebenzi uyenziwa ngokuphangisa, uphumelela esandleni sabo.
9 Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
Sasesibabuza labobadala sakhuluma kanje kubo: Ngubani obeke umthetho kini wokwakha lindlu lokuqedisa lumduli?
10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
Njalo sababuza amabizo abo ukuze sikwazise, ukuze sibhale amabizo abantu abazinhloko zabo.
11 Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
Langokunjalo babuyisela ilizwi kithi besithi: Thina siyizinceku zikaNkulunkulu wamazulu lomhlaba, sakha indlu eyayakhiwe iminyaka eminengi phambi kwalokhu, inkosi enkulu yakoIsrayeli eyayakha yayiqeda.
12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Kodwa emva kwalokho obaba bamthukuthelisa uNkulunkulu wamazulu, wabanikela esandleni sikaNebhukadinezari inkosi yeBhabhiloni, umKhaladiya, owachitha lindlu, wathumbela abantu eBhabhiloni.
13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
Kodwa ngomnyaka wokuqala kaKoresi inkosi yeBhabhiloni, uKoresi inkosi wamisa umthetho wokwakha lindlu kaNkulunkulu.
14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
Njalo lezitsha zendlu kaNkulunkulu ezingezegolide lesiliva uNebhukadinezari ayezithethe wazisusa ethempelini eliseJerusalema waziletha ethempelini leBhabhiloni, lezo uKoresi inkosi wazikhupha ethempelini leBhabhiloni, zanikwa olebizo elinguSheshibazari ayembeke ukuthi abe ngumbusi.
15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
Wasesithi kuye: Thatha lezizitsha, uyezibeka ethempelini eliseJerusalema, lendlu kaNkulunkulu kayakhiwe endaweni yayo.
16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
Ngakho uSheshibazari lo wafika wabeka izisekelo zendlu kaNkulunkulu eseJerusalema; njalo kusukela kulesosikhathi kuze kube khathesi ilokhu isakhiwa, kayikapheli.
17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.
Ngakho-ke uba kulungile enkosini kakuhlolisiswe endlini yokuligugu kwenkosi ekhona eBhabhiloni ukuthi kungaba yikuthi umthetho wenziwa yini nguKoresi inkosi wokwakha lindlu kaNkulunkulu eJerusalema. Kayithumele-ke intando yenkosi kithi mayelana lalinto.

< Ezara 5 >