< Ezara 5 >

1 Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
Then Haggai the prophet and Zechariah son of Iddo the prophet prophesied in the name of the God of Israel to the Jews in Judah and Jerusalem.
2 Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
Zerubbabel son of Shealtiel and Jeshua son of Jozadak rose up and began to build the house of God in Jerusalem with the prophets who supported them.
3 Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
Then Tattenai the governor of the Province Beyond the River, Shethar-Bozenai, and his associates came and said to them, “Who gave you a decree to build this house and complete these walls?”
4 Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
They also said, “What are the names of the men building this building?”
5 Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
But God's eye was on the Jewish elders and their enemies did not stop them. They were waiting for a letter to be sent to the king and for a decree to be returned to them concerning this.
6 Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
This is a copy of the letter of Tattenai, governor of the Province Beyond the River, and Shethar-Bozenai and his accociates in the Province Beyond the River, which they sent to Darius the king.
7 Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
They sent a report, writing this to King Darius, “May all peace be yours.
8 Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
Let the king know that we went to Judah to the house of the great God. It is being built with large stones and timbers set in the walls. This work is being done thoroughly and is going forward well in their hands.
9 Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
We asked the elders, 'Who gave you a decree to build this house and these walls?'
10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
We also asked them their names so you might know the name of each man who led them.
11 Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
They replied and said, 'We are servants of the one who is the God of heaven and earth, and we are rebuilding this house that had been built many years ago when the great king of Israel built it and completed it.
12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
However, when our ancestors enraged the God of heaven, he gave them into the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon, the Chaldean, who destroyed this house and took the people into exile in Babylon.
13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
Nevertheless, in the first year when Cyrus was king of Babylon, Cyrus issued a decree to rebuild the house of God.
14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
King Cyrus also returned the gold and silver objects belonging to the house of God that Nebuchadnezzar had brought from the temple in Jerusalem to the temple in Babylon. He restored them to Sheshbazzar, whom he had made governor.
15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
He said to him, “Take these objects. Go and put them in the temple in Jerusalem. Let the house of God be rebuilt there.”
16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
Then this Sheshbazzar came and laid the foundation for the house of God in Jerusalem; and it is being constructed, but is not yet complete.'
17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.
Now if it pleases the king, may it be investigated in the house of archives in Babylon if a judgment from King Cyrus exists there to build this house of God in Jerusalem. Then let the king send his decision to us.

< Ezara 5 >