< Ezara 5 >
1 Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
and to prophesy Haggai (prophet [the] *Q(K)*) and Zechariah son Iddo (prophet [the] *Q(k)*) since Jew [the] that in/on/with Judah and in/on/with Jerusalem in/on/with name god Israel since them
2 Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
in/on/with then to stand: rise Zerubbabel son Shealtiel and Jeshua son Jozadak and to loose to/for to build house god [the] that in/on/with Jerusalem and with them (prophet [the] *Q(k)*) that god [the] to support to/for them
3 Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
in/on/with her time [the] to come since them Tattenai governor beyond River [the] and Shethar-bozenai Shethar-bozenai and associate their and thus to say to/for them who? to set: make to/for you command house [the] this to/for to build and wall [the] this to/for to complete
4 Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
then thus to say to/for them who? they name man [the] that this building [the] to build
5 Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
and eye god their to be since be gray Jew [the] and not to cease they till account [the] to/for Darius to go and then to return: reply document [the] since this
6 Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
copy letter [the] that to send Tattenai governor beyond River [the] and Shethar-bozenai Shethar-bozenai and associate her governors [the] that in/on/with beyond River [the] since Darius king [the]
7 Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
edict [the] to send since him and like/as this to write in/on/with midst her to/for Darius king [the] peace [the] all [the]
8 Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
to know to be to/for king [the] that to go to/for Judah province [the] to/for house god [the] great [the] and he/she/it to build stone great and wood to set: put/give in/on/with wall [the] and service [the] this diligently to make and to prosper in/on/with hand their
9 Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
then to ask to/for be gray [the] these thus to say to/for them who? to set: make to/for you command house [the] this to/for to build and wall [the] this to/for to complete
10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
and also name their to ask (to/for them *LA(bh)*) to/for to know you that to write name man [the] that in/on/with head their
11 Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
and thus edict [the] to return: reply us to/for to say we they servant/slave his that god heaven [the] and earth: planet [the] and to build house [the] that to be to build from previously this year greatly and king to/for Israel great to build him and to complete her
12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
except from that to enrage father our to/for god heaven [the] to give they in/on/with hand Nebuchadnezzar king Babylon (Chaldean [the] *Q(k)*) and house [the] this to destroy her and people [the] to reveal to/for Babylon
13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
nevertheless in/on/with year one to/for Cyrus king [the] that Babylon Cyrus king [the] to set: make command house god [the] this to/for to build
14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
and also utensil [the] that house god [the] that gold [the] and silver [the] that Nebuchadnezzar to go out from temple [the] that in/on/with Jerusalem and to bring they to/for temple [the] that Babylon to go out they Cyrus king [the] from temple [the] that Babylon and to give to/for Sheshbazzar name her that governor to set: appoint her
15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
and to say to/for her (these *Q(K)*) utensil [the] to lift to go to descend they in/on/with temple [the] that in/on/with Jerusalem and house god [the] to build since place her
16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
then Sheshbazzar this to come to give foundation [the] that house god [the] that in/on/with Jerusalem and from then and till now to build and not be complete
17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.
and now if since king [the] fine to enquire in/on/with house treasure [the] that king [the] there that in/on/with Babylon if there is that from Cyrus king [the] to set: make command to/for to build house god [the] this in/on/with Jerusalem and pleasure king [the] since this to send since us