< Ezara 5 >
1 Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
Then were moved to prophesy, Haggai the prophet, and Zechariah son of Iddo, the prophets, unto the Jews who were in Judaea and in Jerusalem, —in the name of the God of Israel, unto them.
2 Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
Then arose—Zerubbabel son of Shealtiel, and Jeshua son of Jozadak, and began to build the house of God, which was in Jerusalem, —and, with them, were the prophets of God, strengthening them.
3 Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
At that time, came unto them Tattenai pasha Beyond the River, and Shethar-bozenai, and their associates, —and, thus, spake they unto them, Who hath issued unto you an edict, this house, to build, and, this wall, to complete?
4 Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
Then, after this manner, spake we unto them, —What are the names of these men, who, this building, do rear?
5 Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
Nevertheless, the eye of their God, was upon the elders of Judah, and they did not forbid them, until the matter, unto Darius, should come, —and, then, answer be returned by letter, concerning this.
6 Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
A copy of the letter which Tattenai pasha Beyond the River, and Shethar-bozenai, and his associates, the Apharsachites, who were Beyond the Rivet, sent unto Darius the king:
7 Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
a message, sent they unto him, —and, thus, was it written therein, Unto Darius the king, all prosperity!
8 Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
Be it known unto the king, that we journeyed into the province of Judah, unto the house of the Great God, and, the same, is being built with large stones, and, timber, is being laid in the walls, —and, this work, with speed, is being done, and is prospering in their hands.
9 Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
Then asked we of these elders, thus, we said to them, —Who hath issued to you an edict, this house, to build, and, this wall, to complete?
10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
Yea, their names also, asked we of them, to certify thee, —that we might write the name, of the men who are at their head.
11 Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
And, thus, returned they, answer, to us saying, —We, are servants of the God of the heavens and the earth, and are building the house which was built these many years ago, which, a great king of Israel, built and completed.
12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
But, after that our fathers had provoked the God of the heavens to wrath, he delivered them into the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon, the Chaldean, —and, this house, he destroyed, and, the people, he exiled to Babylon.
13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
Howbeit, in the first year of Cyrus king of Babylon, Cyrus the king, issued an edict, this house of God, to build.
14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
Moreover also, the utensils of the house of God, of gold and silver, which, Nebuchadnezzar, had brought forth out of the temple which was in Jerusalem, and had brought into the temple of Babylon, Cyrus the king, brought them forth, out of the temple of Babylon, —and they were delivered to one Sheshbazzar by name, whom he made, pasha;
15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
and said to him—These utensils, take, go carry them into the temple that is in Jerusalem, —and let, the house of God, be built in its place.
16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
Then, this Sheshbazzar, came, he laid the foundations of the house of God, which was in Jerusalem, —and, since then, even until now, it hath been in building, and is not finished.
17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.
Now, therefore, if, unto the king, it seem good, let search be made in the treasure-house of the king which is there, in Babylon, whether it be so, that, from Cyrus the king, issued an edict, to build this house of God, in Jerusalem, —and, the pleasure of the king concerning this, let him send unto us.