< Ezara 5 >

1 Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
Toho času prorokoval Aggeus prorok a Zachariáš syn Iddo, proroci, Židům, kteříž byli v Judstvu a v Jeruzalémě, ve jménu Boha Izraelského mluvíce k nim.
2 Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
Tedy povstavše Zorobábel syn Salatielův, a Jesua syn Jozadakův, počali zase stavěti domu Božího, kterýž jest v Jeruzalémě, a byli s nimi proroci Boží, pomáhajíce jim.
3 Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
Téhož času přišel k nim Tattenai, vývoda za řekou, a Setarbozenai, i tovaryši jejich, kteříž takto k nim řekli: Kdo vám poručil dům tento stavěti a zdi tyto dělati?
4 Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
Tedy jsme jim řekli takto, ano i ty muže, kteří to stavení dělali, jmenovali.
5 Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
Nad staršími pak Židovskými byla ochrana Boha jejich, tak že nepřekazili jim, dokudž ta věc nepřišla před Daria, jehož tehdáž odpověd přinesli o té věci.
6 Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
Přípis listu, kterýž poslal Tattenai vývoda za řekou, a Setarbozenai s tovaryši svými, i Afarsechaiští, kteříž byli za řekou, k Dariovi králi.
7 Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
List poslali jemu, a takto bylo psáno v něm: Dariovi králi pokoj všeliký.
8 Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
Známo buď králi, že jsme přišli do Judské krajiny k domu Boha velikého. Kterýžto stavějí kamením velikým, a dříví kladou do stěn, a dílo to spěšně se staví, a daří se v rukou jejich.
9 Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
Tedy otázali jsme se těch starších, a takto jsme jim řekli: Kdo vám poručil stavěti dům tento, a zdi tyto dělati?
10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
Ano i na jména jejich ptali jsme se jich, abychom oznámili tobě, a napsali jména mužů těch, kteříž jsou přední mezi nimi.
11 Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
Těmito pak slovy nám odpověděli, řkouce: My jsme služebníci Boha nebe a země, a stavíme dům, kterýž byl ustaven prvé před mnohými lety, jejž byl veliký král Izraelský stavěl i dokonal.
12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Ale potom, když popudili otcové naši Boha nebeského, vydal je v ruku Nabuchodonozora krále v Babyloně, Kaldejského, kterýž dům tento zbořil, a lid převedl do Babylona.
13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
A však léta prvního Cýra krále Babylonského, Cýrus král rozkázal, aby tento Boží dům byl staven.
14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
Nadto i nádoby domu Božího zlaté a stříbrné, kteréž byl Nabuchodonozor vynesl z chrámu, jenž byl v Jeruzalémě, a vnesl je do chrámu Babylonského, i ty vynesl Cýrus král z chrámu Babylonského, a dány jsou Sesbazarovi, jehož byl vývodou ustanovil.
15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
A poručil mu, řka: Nádoby tyto vezma, odejdi a slož je v chrámě, kterýž jest v Jeruzalémě, a dům Boží ať stavějí na místě jeho.
16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
Tedy Sesbazar ten přišed, založil grunty domu Božího, kterýž jest v Jeruzalémě, a od toho času až po dnes staví se, a ještě není dokonán.
17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.
Nyní tedy jestli se za dobré králi vidí, nechť se pohledá mezi poklady královskými, kteříž jsou tam v Babyloně, jest-li tak, že by Cýrus král poručil, aby staven byl dům Boží tento, kterýž jest v Jeruzalémě. Potom vůli královskou nechť nám pošle o té věci.

< Ezara 5 >