< Ezara 4 >

1 Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
Now the enemies of Judah and of Benjamin heard that the sons of the captivity were building a temple to the Lord, the God of Israel.
2 Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”
And so, drawing near to Zerubbabel and to the leaders of the fathers, they said to them: “Let us build with you, for we seek your God just as you do. Behold, we have immolated victims to him from the days of Esarhaddon, king of Assyria, who brought us here.”
3 Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
And Zerubbabel, and Jeshua, and the rest of the leaders of the fathers of Israel said to them: “It is not for you to build the house of our God with us. Instead, we alone shall build to the Lord our God, just as Cyrus, the king of the Persians, has commanded us.”
4 Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo.
Therefore, it happened that the people of the land impeded the hands of the people of Judah, and they troubled them in building.
5 Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.
Then they hired counselors against them, so that they might argue against their plan during all the days of Cyrus, king of Persia, even until the reign of Darius, king of the Persians.
6 Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.
And so, during the reign of Ahasuerus, at the beginning of his reign, they wrote an accusation against the inhabitants of Judah and of Jerusalem.
7 Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.
And so, in the days of Artaxerxes, Bishlam, Mithredath, and Tabeel, and the others who were in their council wrote to Artaxerxes, king of the Persians. Now the letter of accusation was written in Syriac, and was being read in the Syrian language.
8 Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:
Rehum, the commander, and Shimshai, the scribe, wrote one letter from Jerusalem to king Artaxerxes, in this manner:
9 Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu,
“Rehum, the commander, and Shimshai, the scribe, and the rest of their counselors, the judges, and rulers, the officials, those from Persia, from Erech, from Babylonia, from Susa, the Dehavites, and the Elamites,
10 ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.
and the rest of the nations, whom the great and glorious Osnappar transferred and caused to live in the cities of Samaria and in the rest of the regions across the river in peace:
11 Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa: Kwa mfumu Aritasasita: Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:
to king Artaxerxes. (This is a copy of the letter, which they sent to him.) Your servants, the men who are across the river, send a greeting.
12 Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.
Let it be known to the king, that the Jews, who ascended from you to us, have arrived in Jerusalem, a rebellious and most wicked city, which they are building, constructing its ramparts and repairing the walls.
13 Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa.
And now let be it known to the king, that if this city will have been built up, and its walls repaired, they will not pay tribute, nor tax, nor yearly revenues, and this loss will affect even the kings.
14 Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse.
But, remembering the salt that we have eaten in the palace, and because we are led to believe that it is a crime to see the king harmed, we have therefore sent and reported to the king,
15 Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga.
so that you may search in the books of the histories of your fathers, and you may find written in the records, and you may know that this city is a rebellious city, and that it is harmful to the kings and the provinces, and that wars were incited within it from the days of antiquity. For which reason also, the city itself was destroyed.
16 Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.
We report to the king that if this city will have been built, and its walls repaired, you will have no possession across the river.”
17 Mfumu inatumiza yankho ili: Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate. Landirani moni.
The king sent word to Rehum, the commander, and to Shimshai, the scribe, and to the rest who were in their council, to the inhabitants of Samaria, and to the others across the river, offering a greeting and peace.
18 Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga.
“The accusation, which you have sent to us, has been read aloud before me.
19 Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo.
And it was commanded by me, and they searched and found that this city, from the days of antiquity, has rebelled against the kings, and that seditions and battles have been incited within it.
20 Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse.
Then too, there have been very strong kings in Jerusalem, who also ruled over the entire region which is across the river. They have also taken tribute, and tax, and revenues.
21 Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula
Now therefore, hear the sentence: Prohibit those men, so that this city may be not built, until perhaps there may be further orders from me.
22 Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?
See to it that you are not negligent in fulfilling this, otherwise, little by little, the evil may increase against the kings.”
23 Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.
And so a copy of the edict of king Artaxerxes was read before Rehum, the commander, and Shimshai, the scribe, and their counselors. And they went away hurriedly to Jerusalem, to the Jews. And they prohibited them by force and by strength.
24 Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.
Then the work of the house of the Lord in Jerusalem was interrupted, and it did not resume until the second year of the reign of Darius, the king of the Persians.

< Ezara 4 >