< Ezara 3 >

1 Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
Isifikile inyanga yesikhombisa, labantwana bakoIsrayeli sebesemizini, abantu babuthana njengamuntu munye eJerusalema.
2 Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
Kwasekusukuma uJeshuwa indodana kaJozadaki labafowabo abapristi, loZerubhabheli indodana kaSalatiyeli labafowabo, bakha ilathi likaNkulunkulu kaIsrayeli ukuze banikele iminikelo yokutshiswa phezu kwalo, njengokubhaliweyo emlayweni kaMozisi umuntu kaNkulunkulu.
3 Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
Basebemisa ilathi ezisekelweni zalo, ngoba ukwesaba kwakuphezu kwabo ngenxa yabantu belizwe, basebenikela eNkosini iminikelo yokutshiswa phezu kwalo, iminikelo yokutshiswa ekuseni lantambama.
4 Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
Basebesenza umkhosi wamadumba njengokubhaliweyo, banikela iminikelo yokutshiswa insuku ngensuku ngenani, njengomkhuba, udaba losuku ngosuku lwalo.
5 Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
Langemva kwalokho umnikelo wokutshiswa njalonjalo, lowekuthwaseni kwezinyanga, lowemikhosi yonke emisiweyo yeNkosi eyayingcwelisiwe, lowakhe wonke owanikela ngesihle umnikelo wesihle eNkosini.
6 Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
Ngosuku lokuqala lwenyanga yesikhombisa baqalisa ukunikela iminikelo yokutshiswa eNkosini, kodwa isisekelo sethempeli leNkosi sasingakabekwa.
7 Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
Basebenika imali kubabazi bamatshe lakubabazi bezigodo, lokudla lokunathwayo lamafutha kumaSidoni lakumaTire ukuze balethe izigodo zemisedari zivela eLebhanoni bezisa elwandle eJopha, ngokwemvumo kaKoresi inkosi yePerisiya kubo.
8 Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
Langomnyaka wesibili wokufika kwabo endlini kaNkulunkulu eJerusalema, ngenyanga yesibili, baqalisa oZerubhabheli indodana kaSalatiyeli loJeshuwa indodana kaJozadaki, lensali yabafowabo, abapristi lamaLevi, labo bonke ababebuyile eJerusalema bevela ekuthunjweni; basebemisa amaLevi kusukela koleminyaka engamatshumi amabili kusiya phezulu ukongamela umsebenzi wendlu yeNkosi.
9 Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
Kwasekusukuma oJeshuwa, amadodana akhe, labafowabo, uKadimiyeli lamadodana akhe, abantwana bakoJuda, njengomuntu munye ukongamela abenzi bomsebenzi endlini kaNkulunkulu, amadodana kaHenadadi, amadodana abo labafowabo amaLevi.
10 Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
Abakhi sebebekile isisekelo sethempeli leNkosi, bamisa abapristi begqokile belezimpondo, lamaLevi, amadodana kaAsafi, elensimbi ezincencethayo, ukudumisa iNkosi, njengokwezandla zikaDavida inkosi yakoIsrayeli.
11 Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
Baphendulana ngokuhlabela bedumisa bebonga iNkosi, ngoba ilungile, ngoba umusa wayo umi kuze kube nininini kuIsrayeli. Bonke abantu basebememeza ngokumemeza okukhulu ekuyidumiseni iNkosi, ngoba isisekelo sendlu yeNkosi sasesibekiwe.
12 Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
Kodwa abanengi babapristi lamaLevi lenhloko zaboyise, abadala ababeyibonile indlu yokuqala, isisekelo salindlu sesibekiwe emehlweni abo, bakhala inyembezi ngelizwi elikhulu; kodwa abanengi baphakamisa ilizwi ngokumemeza ngentokozo.
13 Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.
Ngokunjalo abantu kabehlukanisanga umsindo wokumemeza kwentokozo lomsindo wokukhala kwabantu, ngoba abantu baklabalala ngokuklabalala okukhulu, umsindo waze wezwakala khatshana.

< Ezara 3 >