< Ezara 3 >

1 Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
Kuin seitsemäs kuukausi oli tullut ja Israelin lapset olivat kaupungeissansa, tuli kansa kokoon niinkuin yksi mies Jerusalemiin.
2 Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
Niin nousi Jesua Jotsadakin poika, ja papit hänen veljensä, ja Serubbabel Sealtielin poika ja hänen veljensä ja rakensivat Israelin Jumalan alttarin uhrataksensa sen päällä polttouhria, niinkuin kirjoitettu on Moseksen, Jumalan miehen, laissa.
3 Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
Ja he laskivat alttarin perustuksensa päälle, vaikka he pelkäsivät sen maan kansoja; ja he uhrasivat sen päällä Herralle polttouhria aamulla ja ehtoolla.
4 Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
Ja he pitivät lehtimajan juhlaa niinkuin kirjoitettu on, ja tekivät polttouhria joka päivä, sen luvun jälkeen kuin tapa oli, kunkin päivänänsä,
5 Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
Senjälkeen alinomaisia polttouhreja, ja uuden kuun, ja kaikkein Jumalalle pyhitettyin juhlain, ja kaikkinaisia mieliuhreja, joita he hyvällä mielellä tekivät Herralle.
6 Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
Seitsemännen kuukauden ensimäisenä päivänä rupesivat he uhraamaan Herralle polttouhria; mutta ei Herran templin perustus ollut vielä laskettu.
7 Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
Ja he antoivat kivenhakkaajille ja taitavaille työväelle rahaa, ja ruokaa ja juomaa, ja öljyä Sidonilaisille ja Tyrolaisille, että he toisivat heille sedripuita Libanonista Japhoon merta myöten, Koreksen Persian kuninkaan suomasta,
8 Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
Mutta toisena vuonna sittekuin he tulivat Jerusalemiin Herran huoneen tykö, toisena kuukautena, rupesi Serubbabel Sealtielin poika, ja Jesua Jotsadakin poika, ja muut heidän jääneet veljensä, papit ja Leviläiset, ja kaikki, jotka vankeudesta tulivat Jerusalemiin, ja panivat kahdenkymmenen ajastaikaiset ja sitä vanhemmat Leviläiset Herran huoneen työn teettäjiksi.
9 Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
Ja Jesua seisoi poikinensa ja veljinensä, ja Kadmiel poikinensa, ja Juudan lapset, niinkuin yksi mies teettämässä työväkeä Herran huoneessa, Henadadin lapset poikinensa, ja Leviläiset veljinensä.
10 Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
Ja kuin rakentajat laskivat Herran templin perustuksen, asettivat he papit puetettuina, vaskitorvien kanssa, ja Leviläiset Asaphin pojat kanteleilla, kiittämään Herraa Davidin Israelin kuninkaan sanoilla.
11 Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
Ja he veisasivat vuorottain ylistäissänsä ja kiittäissänsä Herraa, että hän on hyvä ja hänen laupiutensa pysyy ijankaikkisesti Israelin ylitse. Ja kaikki kansa huusi korkialla äänellä ja kiitti Herraa, että Herran huoneen perustus oli laskettu.
12 Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
Mutta moni vanhoista papeista, ja Leviläisistä ja isäin päämiehistä, jotka olivat nähneet ensimäisen huoneen perustuksellansa, niin myös tämän huoneen silmäinsä edessä, itkivät suurella äänellä; ja moni huusi korkialla äänellä ilon tähden;
13 Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.
Että se huuto oli niin suuri, ettei kansa eroittanut ilon ääntä itkun äänestä; sillä kansa huusi korkialla äänellä, että se ääni kauvas kuului.

< Ezara 3 >