< Ezara 3 >

1 Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
Og der den syvende Maaned var kommen, og Israels Børn vare i deres Stæder, da samledes Folket som een Mand til Jerusalem.
2 Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
Og Jesua, Jozadaks Søn, og hans Brødre, Præsterne, gjorde sig rede tillige med Serubabel, Sealthiels Søn, og hans Brødre og byggede Israels Guds Alter til at ofre Brændoffer derpaa, som skrevet er i Moses, den Guds Mands Lov.
3 Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
Og de oprejste Alteret paa dets Grundvold; thi der var Forfærdelse over dem for Folkene i Landene, og de ofrede derpaa Brændofre til Herren, Brændofre om Morgenen og om Aftenen.
4 Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
Og de holdt Løvsalernes Højtid, som det var foreskrevet, og ofrede Brændofre hver Dag efter det fastsatte Tal, som Skik var, hver Dags Ting paa sin Dag;
5 Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
derefter ogsaa det bestandige Brændoffer og det for Nymaanederne og for alle Herrens helligede Højtider og for enhver, siom bragte et frivilligt Offer for Herren.
6 Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
Fra den første Dag i den syvende Maaned begyndte de at ofre Herren Brændofre, men Herrens Tempels Grundvold var ikke lagt.
7 Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
Og de gave Penge til Stenhuggerne og Tømmermændene og Mad og Drikke og Olie til dem fra Sidon og Tyrus, at de skulde føre Cedertræer fra Libanon til Havet imod Jafo efter den Tilladelse, de havde faaet af Kyrus, Kongen af Persien.
8 Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
Men i det andet Aar, efter at de vare komne til Guds Hus i Jerusalem, i den anden Maaned, da begyndte Serubabel, Sealthiels Søn, og Jesua, Jozadaks Søn, og de andre af deres Brødre, Præsterne og Leviterne og alle, som vare komne af Fangenskabet til Jerusalem, og de beskikkede Leviterne, fra tyve Aar gamle og derover, til at have Tilsyn med Arbejdet ved Herrens Hus.
9 Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
Da stode Jesua, hans Sønner og hans Brødre, Kadmiel med hans Sønner og Judas Børn som een Mand for at have Tilsyn med dem, som arbejdede ved Guds Hus, i lige Maade Henadads Børn, deres Børn og deres Brødre, Leviterne.
10 Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
Der Bygningsmændene lagde Grundvolden til Herrens Tempel, da lode de Præsterne staa iførte deres Præstedragt med Basuner og Leviterne, Asafs Børn, med Cymbler for at love Herren efter Davids, Israels Konges, Indretning.
11 Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
Og de sang, idet de lovede og takkede Herren, at han er god, at hans Miskundhed er evindelig over Israel; og alt Folket raabte med et stort Frydeskrig, idet de lovede Herren, fordi Grundvolden til Herrens Hus var lagt.
12 Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
Men mange af Præsterne og Leviterne og Øversterne for Fædrenehusene, de gamle, som havde set det første Hus, græd med høj Røst, da dette andet stod paa sin Grundvold for deres Øjne; men mange opløftede Røsten med Frydeskrig og med Glæde,
13 Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.
saa at Folket kunde ikke skelne Røsten af Glædens Frydeskrig fra Røsten af Folkets Graad, fordi Folket raabte med et stort Skrig, saa at man hørte Røsten langt borte.

< Ezara 3 >