< Ezara 3 >

1 Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
Když pak nastal měsíc sedmý, a byli synové Izraelští v městech, shromáždil se lid jednomyslně do Jeruzaléma.
2 Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
Tedy vstav Jesua syn Jozadakův s bratřími svými kněžími, a Zorobábel syn Salatielův s bratřími svými, vzdělali oltář Boha Izraelského, aby obětovali na něm oběti zápalné, jakož psáno jest v zákoně Mojžíše muže Božího.
3 Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
A když postavili oltář ten na základích jeho, ačkoli se obávali národů jiných zemí, však obětovali na něm oběti zápalné Hospodinu, oběti zápalné ráno i večer.
4 Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
Drželi také slavnost stánků, jakož psáno jest, obětujíce zápal na každý den, vedlé počtu a vedlé obyčeje každého dne,
5 Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
A potom obět zápalnou ustavičnou, i na novměsíce i na každou slavnost Hospodinu posvěcenou, i od každého dobrovolně obětujícího dobrovolnou obět Hospodinu.
6 Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
Od prvního dne toho měsíce sedmého počali obětovati zápalů Hospodinu, ačkoli chrám Hospodinův ještě nebyl založen.
7 Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
I dali peníze kameníkům a řemeslníkům, též potravy a nápoje i oleje Sidonským a Tyrským, aby vezli dříví cedrové z Libánu k moři Joppen, podlé povolení jim Cýra krále Perského.
8 Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
Léta pak druhého po jejich se navrácení k domu Božímu do Jeruzaléma, měsíce druhého, začali Zorobábel syn Salatielův, a Jesua syn Jozadakův, i jiní bratří jejich kněží a Levítové a všickni, kteříž byli přišli z toho zajetí do Jeruzaléma, a ustanovili Levíty od dvadcítiletých a výše, aby přihlédali k dílu domu Hospodinova.
9 Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
A tak postaven jest Jesua, synové jeho i bratří jeho, Kadmiel i synové jeho, synové Judovi spolu, aby přihlédali k dílu při domě Božím, potomci Chenadadovi, synové jejich i bratří jejich Levítové.
10 Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
A když zakládali grunty stavitelé chrámu Hospodinova, postavili kněží zobláčené s trubami, a Levíty, syny Azafovy s cymbály, aby chválili Hospodina vedlé nařízení Davida krále Izraelského.
11 Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
I prozpěvovali jedni po druhých, chválíce a oslavujíce Hospodina, nebo dobrý jest, a že na věky trvá milosrdenství jeho nad Izraelem. Všecken také lid prokřikoval hlasem velikým, chválíce Hospodina, proto že založen byl dům Hospodinův.
12 Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
Mnozí pak z kněží a z Levítů i z knížat čeledí otcovských, starci, kteříž byli viděli prvnější dům, když zakládali tento dům před očima jejich, plakali hlasem velikým. Mnozí nazpět prokřikovali s radostí hlasem velikým,
13 Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.
Tak že lid nemohl rozeznati hlasu prokřikování radostného od hlasu plačícího lidu; nebo lid ten prokřikoval hlasem velikým, a hlas ten slyšán byl daleko.

< Ezara 3 >