< Ezara 10 >
1 Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
Ainsi donc Esdras priant, implorant, pleurant, et étendu devant le temple de Dieu, une très grande assemblée d’hommes, de femmes et d’enfants d’Israël se réunit auprès de lui, et le peuple pleura d’un grand pleur.
2 Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
Alors Séchénias, fils de Jéhiel, d’entre les enfants d’Elam, répondit à Esdras: Nous avons prévariqué contre notre Dieu, et nous avons pris des femmes étrangères des peuples de la terre; et maintenant, si on a du repentir de cela en Israël,
3 Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
Faisons alliance avec le Seigneur notre Dieu, en sorte que nous rejetions toutes les femmes, et ceux qui sont nés d’elles, suivant la volonté du Seigneur et de ceux qui craignent le précepte du Seigneur notre Dieu: qu’il soit fait selon la loi.
4 Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
Lève-toi, c’est à toi d’ordonner, et nous, nous serons avec toi; sois fort et agis.
5 Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
Esdras donc se leva, et adjura les princes des prêtres et des Lévites, et tout Israël, afin qu’ils fissent selon cette parole, et ils jurèrent.
6 Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
Et Esdras se leva devant la maison de Dieu, et s’en alla à la chambre de Johanan, fils d’Eliasib, et il y entra: il ne mangea point de pain et ne but point d’eau; car il pleurai t la transgression de ceux qui étaient venus de la captivité.
7 Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
Alors fut envoyée une voix en Juda et à Jérusalem, pour que tous les fils de la transmigration se rassemblassent à Jérusalem;
8 Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
Et pour que quiconque ne serait point venu dans trois jours, suivant le conseil des princes et des anciens, tout son bien lui fût ôté, et qu’il fût lui-même rejeté de l’assemblée de la transmigration.
9 Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
Tous les hommes de Juda et de Benjamin s’assemblèrent donc à Jérusalem dans les trois jours; c’était le neuvième mois, au vingtième jour du mois, et tout le peuple se tint sur la place de la maison de Dieu, tremblant à cause de leurs péchés et des pluies.
10 Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
Alors Esdras le prêtre se leva, et leur dit: Vous avez transgressé, et vous avez pris des femmes étrangères, pour ajouter au péché d’Israël.
11 Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
Or maintenant rendez gloire au Seigneur Dieu de vos pères, et faites ce qui lui plaît: séparez-vous des peuples de la terre et des femmes étrangères.
12 Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
Et toute la multitude répondit, et dit avec une voix forte: Qu’il soit fait selon la parole que vous nous avez dite.
13 Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
Cependant, parce que le peuple est nombreux, que c’est un temps de pluie, que nous ne pouvons rester dehors, et que l’ouvrage n’est pas d’un jour ni de deux (car nous avons grandement péché en cette chose),
14 Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
Que des princes soient établis dans toute la multitude, et que tous ceux qui dans nos villes ont pris des femmes étrangères, viennent en des temps marqués, et avec eux des anciens de chaque ville et les juges aussi, jusqu’à ce que soit détournée de nous la colère de notre Dieu provoquée à cause de ce péché.
15 Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
Ainsi Jonathan, fils d’Azahel, et Jaasia, fils de Thécué, furent présentés pour cela, et Mésollam et Sébéthaï, Lévites, les aidèrent.
16 Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
Et les fils de la transmigration firent ainsi. Et Esdras, le prêtre, et les hommes princes des familles, s’en allèrent dans les maisons de leurs pères, et tous selon leurs noms, et ils s’établirent au premier jour du dixième mois pour s’informer de la chose.
17 Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
Or ils n’achevèrent de dénombrer les hommes qui avaient pris des femmes étrangères, qu’au premier jour du premier mois.
18 Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
Et il se trouva d’entre les fils des prêtres qui avaient pris des femmes étrangères: d’entre les fils de Josué, les fils de Josédec, et ses frères, Maasia, Eliézer, Jarib et Godolia.
19 Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
Ils donnèrent leurs mains pour chasser leurs femmes, et pour offrir pour leur péché un bélier d’entre leurs brebis.
20 Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
Et d’entre les fils d’Emmer, Hanani et Zébédia;
21 Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
Et d’entre les fils de Harim, Maasia, Elia, Séméia, Jéhiel et Ozias;
22 Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
Et d’entre les fils de Pheshur, Elioénaï, Maasia, Ismaël, Nathanaël, Jozabed et Elasa;
23 Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
Et d’entre les fils des Lévites, Jozabed, et Séméi, Célaïa (c’est le même que Calita), Phataïa, Juda et Eliézer;
24 Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
Et d’entre les chantres, Eliasib; et d’entre les portiers, Sellum, Télem et Uri;
25 Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
Et d’Israël: d’entre les fils de Pharos, Réméia, Jézia, Melchia, Miamin, Eliézer, Melchia et Banéa;
26 A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
Et d’entre les fils d’Elam, Mathania, Zacharias, Jéhiel, Abdi, Jérimoth et Élia;
27 A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
Et d’entre les fils de Zéthua, Elioénaï, Eliasib, Mathania, Jérimuth, Zabad et Aziza;
28 A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
Et d’entre les fils de Bébaï, Johanan, Hanania, Zabbaï, Athalaï;
29 A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
Et d’entre les fils de Bani, Mosollam, Melluch, Adaïa, Jasub, Saal et Ramoth;
30 A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
Et d’entre les fils de Phahath-Moab, Edna, Chalal, Banaïas, Maasias, Mathanias, Béséléel, Bennuï, et Manassé;
31 A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
Et d’entre les fils de Hérem, Eliézer, Josué, Melchias, Séméias, Siméon,
32 Benjamini, Maluki ndi Semariya.
Benjamin, Maloch, Samarias;
33 A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
Et d’entre les fils d’Hasom, Mathanaï, Mathatha, Zabad, Eliphéleth, Jermaï, Manassé, Séméi;
34 A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
D’entre les fils de Bani, Maaddi, Amram, Vel,
35 Benaya, Bediya, Keluhi,
Banéas, Badaïas, Chéliaü,
36 Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
Vania, Marimuth, Eliasib,
37 Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
Mathanias, Mathanaï, Jasi,
38 A fuko la Binuyi anali Simei,
Et Bani, Bennuï, Séméi,
39 Selemiya, Natani, Adaya,
Et Salmias, Nathan, Adaïas,
40 Makinadebayi, Sasai, Sarai,
Et Mechnedebaï, Sisaï, Saraï,
41 Azaleli, Selemiya, Semariya,
Ezrel, Sélémiaü, Séméria,
42 Salumu, Amariya ndi Yosefe.
Sellum, Amaria, Joseph;
43 A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
D’entre les fils de Nébo, Jéhiel, Mathathias, Zabad, Zabina, Jeddu, Joël et Banaïa.
44 Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.
Tous ceux-ci avaient pris des femmes étrangères, et il y eut de ces femmes qui avaient enfanté des fils.