< Ezara 10 >

1 Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
Or, comme Esdras priait et faisait cette confession, pleurant et prosterné devant la maison de Dieu, une fort grande multitude d'Israélites, hommes, femmes et enfants, s'assembla vers lui; et ce peuple répandit des larmes en abondance.
2 Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
Alors Shécania, fils de Jéhiel, des enfants d'Élam, prit la parole, et dit à Esdras: Nous avons péché contre notre Dieu, en prenant des femmes étrangères d'entre les peuples de ce pays. Mais maintenant il est encore à cet égard quelque espérance pour Israël.
3 Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
Engageons-nous maintenant, par alliance avec notre Dieu, à renvoyer toutes ces femmes et tout ce qui est né d'elles, selon le conseil de mon seigneur et de ceux qui tremblent au commandement de notre Dieu; et que l'on fasse selon la loi.
4 Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
Lève-toi; car cette affaire te regarde, et nous serons avec toi. Prends donc courage, et agis.
5 Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
Alors Esdras se leva, et il fit jurer aux chefs des sacrificateurs, des Lévites et de tout Israël, qu'ils feraient selon cette parole; et ils le jurèrent.
6 Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
Puis Esdras se leva de devant la maison de Dieu, et s'en alla dans la chambre de Jochanan, fils d'Éliashib, et y entra; et il ne mangea point de pain et ne but point d'eau, parce qu'il était en deuil à cause du péché de ceux de la captivité.
7 Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
Alors on publia, en Juda et à Jérusalem, que tous les enfants de la captivité eussent à s'assembler à Jérusalem.
8 Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
Et que si quelqu'un ne s'y rendait pas dans trois jours, selon l'avis des principaux et des anciens, tout son bien serait mis en interdit, et qu'il serait séparé de l'assemblée de ceux de la captivité.
9 Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
Ainsi tous ceux de Juda et de Benjamin s'assemblèrent à Jérusalem dans les trois jours; ce fut au neuvième mois, le vingtième jour du mois; et tout le peuple se tint sur la place de la maison de Dieu, tremblant au sujet de cette affaire, et à cause des pluies.
10 Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
Puis Esdras, le sacrificateur, se leva et leur dit: Vous avez péché, en prenant chez vous des femmes étrangères, et vous avez ainsi rendu Israël plus coupable.
11 Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
Mais maintenant, faites la confession de votre faute à l'Éternel, le Dieu de vos pères, et faites sa volonté. Séparez-vous des peuples du pays et des femmes étrangères.
12 Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
Et toute l'assemblée répondit, et dit à haute voix: Oui, il faut que nous fassions comme tu dis.
13 Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
Mais le peuple est nombreux, et c'est le temps des pluies, et il n'y a pas moyen de se tenir dehors; et ce n'est pas une affaire d'un jour, ni de deux; car nous sommes un grand nombre qui avons péché dans cette affaire.
14 Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
Que nos chefs de toute l'assemblée demeurent donc; et que tous ceux qui dans nos villes ont introduit chez eux des femmes étrangères, viennent à des époques déterminées, avec les anciens et les juges de chaque ville, jusqu'à ce que l'ardeur de la colère de notre Dieu au sujet de cette affaire, se soit détournée de nous.
15 Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
Il n'y eut que Jonathan, fils d'Asaël, et Jachzia, fils de Thikva, qui s'opposèrent à cela; et Méshullam et Shabbéthaï, le Lévite, les appuyèrent.
16 Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
Mais les enfants de la captivité firent ainsi: On choisit Esdras, le sacrificateur, et les chefs des pères, selon les maisons de leurs pères, tous désignés par leurs noms. Ils siégèrent au premier jour du dixième mois, pour s'informer de cette affaire.
17 Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
Et le premier jour du premier mois, ils eurent fini avec tous ceux qui avaient pris chez eux des femmes étrangères.
18 Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
Parmi les fils des sacrificateurs, il s'en trouva qui avaient pris chez eux des femmes étrangères; d'entre les enfants de Jéshua, fils de Jotsadak, et d'entre ses frères: Maaséja, Éliézer, Jarib et Guédalia;
19 Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
Qui promirent de renvoyer leurs femmes, et d'offrir, comme coupables, un bélier pour leur péché.
20 Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
Des enfants d'Immer: Hanani et Zébadia.
21 Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
Des enfants de Harim: Maaséja, Élie, Shémaja, Jéhiel et Uzzia.
22 Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
Des enfants de Pashur: Eljoénaï, Maaséja, Ismaël, Nathanaël, Jozabad et Éléasa.
23 Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
Des Lévites: Jozabad, Shimeï, Kélaja (c'est Kélita), Péthachia, Juda et Éliézer.
24 Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
Des chantres: Éliashib; et des portiers: Shallum, Télem et Uri.
25 Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
De ceux d'Israël, des enfants de Parosh: Ramia, Jizzia, Malkija, Mijamin, Éléazar, Malkija et Bénaja.
26 A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
Des enfants d'Élam: Matthania, Zacharie, Jéhiel, Abdi, Jérémoth et Élie.
27 A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
Des enfants de Zatthu: Eljoénaï, Éliashib, Matthania, Jérémoth, Zabad et Aziza.
28 A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
Des enfants de Bébaï: Jochanan, Hanania, Zabbaï et Athlaï.
29 A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
Des enfants de Bani: Méshullam, Malluc, Adaja, Jashud, Shéal et Ramoth.
30 A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
Des enfants de Pachath-Moab: Adna, Kélal, Bénaja, Maaséja, Matthania, Bethsaléel, Binnuï et Manassé.
31 A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
Des enfants de Harim: Éliézer, Jishija, Malkija, Shémaja, Siméon,
32 Benjamini, Maluki ndi Semariya.
Benjamin, Malluc et Shémaria.
33 A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
Des enfants de Hashum: Mathnaï, Matthattha, Zabad, Éliphélet, Jérémaï, Manassé et Shimeï.
34 A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
Des enfants de Bani: Maadaï, Amram, Uël,
35 Benaya, Bediya, Keluhi,
Bénaja, Bédia, Kéluhu,
36 Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
Vania, Mérémoth, Éliashib,
37 Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
Matthania, Matthénaï, Jaasaï,
38 A fuko la Binuyi anali Simei,
Bani, Binnuï, Shimeï,
39 Selemiya, Natani, Adaya,
Shélémia, Nathan, Adaja,
40 Makinadebayi, Sasai, Sarai,
Macnadbaï, Shashaï, Sharaï,
41 Azaleli, Selemiya, Semariya,
Azaréel, Shélémia, Shémaria,
42 Salumu, Amariya ndi Yosefe.
Shallum, Amaria et Joseph.
43 A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
Des enfants de Nébo: Jéiel, Matthithia, Zabad, Zébina, Jaddaï, Joël et Bénaja.
44 Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.
Tous ceux-là avaient pris des femmes étrangères; et il y en avait d'entre eux qui avaient eu des enfants de ces femmes-là.

< Ezara 10 >