< Ezara 10 >
1 Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
While I was kneeling down in front of the temple and praying and crying, I was confessing [the sins that the Israeli people had committed]. Many people, men and women and children, gathered around me and also cried very much.
2 Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
Then Shecaniah, the son of Jehiel from the clan of Elam, said this to me: “We have disobeyed God. [Some of] us have married women who are not Israelis. But we can still confidently expect [Yahweh to be merciful to] us Israeli people.
3 Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
We will do what you, and the others who have an awesome respect for what our God has commanded, tell us to do. We will do what God told us in his laws. We will make an agreement with our God, saying that we will divorce our wives who are not Israelis, and we will send them away with their children.
4 Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
(It is your responsibility to/Because you are our leader, you must) [tell us what to do]. So get up, and be courageous, and do [what is necessary]. We will (support you/tell people to do what you say).”
5 Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
So I stood up and demanded that the leaders of the priests, the [other] descendants of Levi, and all [the other] Israeli people solemnly declare that they would do what Shecaniah said that they should do. So they all solemnly promised to do that.
6 Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
Then I went away from the front of the temple and went to the room where Jehohanan lived. I stayed there that night, but I did not eat or drink anything. I was still sad because some of the Israelis who had returned [from Babylonia] had not faithfully obeyed [God’s laws].
7 Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
Then we sent a message to all [the people in] Jerusalem and [in other towns in] Judah, saying that all those who had returned [from Babylonia] should come to Jerusalem immediately.
8 Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
We said that if any of them did not arrive within three days, the leaders of the people would order that all the property of those people would be taken from them, and that they would no longer be considered to belong to the Israeli people; [they would be considered to be foreigners].
9 Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
So within three days, on December 19, all the people of the tribes of Judah and Benjamin gathered in Jerusalem. They were there, sitting in the courtyard in front of the temple. They were trembling because it was raining hard and because they were worried [that they would be punished for what they had done].
10 Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
Then I stood up and said to them, “[Some of] you men have committed a very bad sin. You have married women who are not Israelis. By doing that, you have made us Israeli people more guilty [than we were before].
11 Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
So now you must confess to Yahweh, the God whom your ancestors [worshiped/belonged to], the sin which you have committed, and you must do what he wants. Separate yourselves from the people of other nations and from the women from those nations whom you have married.”
12 Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
The whole group answered, shouting loudly, “Yes, what you have said is right! We will do what you have said.”
13 Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
But then [one of] them said, “But we are a very large group, and it is raining hard. Also, there are many of us who have committed this bad sin. This is something that we cannot (take care of/handle) in one or two days, and we cannot stand here in this rain.
14 Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
So allow our leaders to decide for all of us what we should do. Tell everyone who has married a woman who is not Israeli to come at a time that you decide. They should come with the elders and judges from each city. If we do that, our God will stop being angry with us [because of what we have done].”
15 Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
Jonathan the son of Asahel, Jahzeiah the son of Tikvah, Meshullam, and Shabbethai, a descendant of Levi, were the only ones who objected to this.
16 Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
All the others who had returned from Babylonia said that they would do it. So I chose leaders of each of the clans, and I wrote down their names. On December 29, these men came and sat down to investigate the matter.
17 Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
By March 27 of the next year they finished determining which men had married women who were not Israelis.
18 Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
This is a list of the names of the priests who had married non-Israeli women, and the clans to which they belonged. From the clan of Jeshua and his brothers, who were sons of Jehozadak, there were Maaseiah, Eliezer, Jarib, and Gedaliah.
19 Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
They solemnly promised to divorce their wives, and they each sacrificed a ram to be an offering [to atone] for their sins.
20 Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
From the clan of Immer there were Hanani and Zebadiah.
21 Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
From the clan of Harim there were Maaseiah, Elijah, Shemaiah, Jehiel, and Uzziah.
22 Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
From the clan of Pashhur there were Elioenai, Maaseiah, Ishmael, Nethanel, Jozabad, and Elasah.
23 Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
The [other] descendants of Levi [who had married non-Israeli women] were Jozabad, Shimei, Kelaiah (whose other name was Kelita), Pethahiah, Judah, and Eliezer.
24 Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
There was Eliashib the musician. From the temple guards there were Shallum, Telem, and Uri.
25 Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
This is a list of the names of the other Israelis who had married foreign wives: From the clan of Parosh there were Ramiah, Izziah, Malchijah, Mijamin, Eleazar, Hashabiah, and Benaiah.
26 A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
From the clan of Elam there were Mattaniah, Zechariah, Jehiel, Abdi, Jeremoth, and Elijah.
27 A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
From the clan of Zattu there were Elioenai, Eliashib, Mattaniah, Jeremoth, Zabad, and Aziza.
28 A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
From the clan of Bebai there were Jehohanan, Hananiah, Zabbai, and Athlai.
29 A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
From the clan of Bani there were Meshullam, Malluch, Adaiah, Jashub, Sheal, and Jeremoth.
30 A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
From the clan of Pahath-Moab there were Adna, Kelal, Benaiah, Maaseiah, Mattaniah, Bezalel, Binnui, and Manasseh.
31 A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
From the clan of Harim there were Eliezer, Ishijah, Malkijah, Shemaiah, Shimeon,
32 Benjamini, Maluki ndi Semariya.
Benjamin, Malluch, and Shemariah.
33 A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
From the clan of Hashum there were Mattenai, Mattattah, Zabad, Eliphelet, Jeremai, Manasseh, and Shimei.
34 A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
From the clan of Bigvai there were Maadai, Amram, Uel,
35 Benaya, Bediya, Keluhi,
Benaiah, Bedeiah, Keluhi,
36 Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
Vaniah, Meremoth, Eliashib,
37 Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
Mattaniah, Mattenai, and Jaasu.
38 A fuko la Binuyi anali Simei,
From the clan of Binnui there were Shimei,
39 Selemiya, Natani, Adaya,
Shelemiah, Nathan, Adaiah,
40 Makinadebayi, Sasai, Sarai,
Macnadebai, Shashai, Sharai,
41 Azaleli, Selemiya, Semariya,
Azarel, Shelemiah, Shemariah,
42 Salumu, Amariya ndi Yosefe.
Shallum, Amariah, and Joseph.
43 A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
From the clan of Nebo there were Jeiel, Mattithiah, Zabad, Zebina, Jaddai, Joel, and Benaiah.
44 Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.
Each of those men had married a woman who was not an Israeli. [But immediately] they divorced those women and sent them and their children away.