< Ezara 10 >

1 Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
Ezra he a thangthui vaengah khaw a uem vaengah khaw a rhah neh Pathen im hmai ah bakop. A taengah Israel hlangping lamloh tongpa neh huta neh camoe neh uep tingtun uh khungdaeng. Pilnam khaw lungnat neh bungbung rhap uh.
2 Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
Te vaengah Elam kah Elam koca Jehiel capa Shekaniah loh a doo tih Ezra te, “Mamih tah mamih kah Pathen taengah boe n'koek uh dongah khohmuen pilnam lamkah kholong nu neh kho n'sak uh. Te cakhaw Israel ham ngaiuepnah om coeng.
3 Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
Te dongah ka boei rhoek neh mamih kah Pathen olpaek dongah aka thuen rhoek kah cilsuep bangla huta rhoek neh amih kah a cun boeih te tueih hamla mamih kah Pathen taengah paipi saii uh pawn sih lamtah olkhueng bangla vai uh saeh.
4 Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
Olka he namah hut coeng dongah thoo lamtah kaimih khaw nang taengah ka omuh. Thaahuel lamtah saii laeh,” a ti nah.
5 Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
Te dongah Ezra thoo tih a toemngam. Levi khosoih mangpa rhoek neh Israel boeih long khaw te ol bangla saii ham a toemngam uh.
6 Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
Te phoeiah tah Ezra te Pathen im hmai lamloh thoo tih Eliashib capa Jehohanan kah imkhan la cet. Buh te pahoi a paan dae ca pawt tih vangsawn boekoeknah ham a nguekcoi dongah tui khaw o pawh.
7 Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
Te dongah vangsawn koca boeih te Jerusalem la coi ham Judah neh Jerusalem ah ol a pat.
8 Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
Mangpa rhoek neh a hamca rhoek kah cilsuep bangla hnin thum khuiah aka pawk pawt boeih tah a khuehtawn boeih thup pah saeh lamtah anih te vangsawn hlangping lamloh hoep saeh,’ a ti.
9 Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
Te dongah Judah hlang neh Benjamin, Jerusalem pum tah hla ko hla kah hnin kul vaengah hnin thum khuiah tingtun uh. Te vaengah pilnam pum te Pathen im kah toltung ah ngol uh. Tekah ol neh khonal dong lamloh amih te thuen uh.
10 Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
Te vaengah khosoih Ezra pai tih amih te, “Boe na koek tih Israel kah dumlai te koei hamla kholong nu neh kho na sak uh.
11 Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
Te dongah na pa rhoek kah Pathen BOEIPA taengah tholh phongnah khueh uh laeh. A kolonah te saii uh lamtah khohmuen pilnam taeng lamkah neh kholong nu taeng lamloh hoep uh laeh,” a ti nah.
12 Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
Hlangping pum loh a doo uh tih ol a len la, “Namah ol van tangloeng ni, na ol bangla kaimih taengah saii pai.
13 Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
Tedae pilnam he ping tih khonal tue la om bal. Te dongah tollong ah pai ham thadueng a om moenih. He ol dongah boekoek la a ping dongah bitat he hnin at nen bueng pawt tih hnin nit ah coeng mahpawh.
14 Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
Hlangping boeih hamla mamih kah mangpa rhoek he pai mai saeh. Te phoeiah mah kho khuikah kholong nu neh kho aka sa boeih te a caeng tue bangla kun sak saeh. He olka dongah kaimih Pathen kah thintoek thinsa te kaimih lamloh a mael hil amih neh kho, kho kah a hamca rhoek loh laitloek saeh.
15 Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
Asahel capa Jonathan neh Tikvah capa Jahaziah loh he he a tlai thil tih amih rhoi te Levi Meshullam neh Shabbethai loh a bom.
16 Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
Te dongah vangsawn koca rhoek loh a saii uh. Te phoeiah khosoih Ezra loh hlang rhoek te a napa imkhui tarhing ah a napa boeilu neh a boel. A hla rha dongkah hnin lamhmacuek vaengah Amih boeih te a ming neh ol dawt hamla ngol uh.
17 Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
Lamhmacuek hla kah lamhmacuek khohnin ah kholong nu neh aka om hlang boeih te a khah uh.
18 Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
Te vaengah khosoih koca rhoek khuiah Jeshua koca lamkah Jozadak capa neh amah boeinaphung Maaseiah, Eliezer, Jarib neh Gedaliah tah kholong nu neh kho a sak te a hmuh.
19 Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
Te dongah a yuu rhoek te tueih hamla a kut te a yuh uh tih amamih kah dumlai dongah boiva la tutal a rhaem uh.
20 Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
Te phoeiah Immer koca rhoek lamloh Hanani neh Zebadiah.
21 Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
Harim koca lamloh Maaseiah, Elijah, Shemaiah, Jehiel neh Uzziah.
22 Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
Pashur koca lamloh Elioenai, Maaseiah, Ishmael, Nethanel, Jozabad neh Elasah.
23 Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
Levi lamloh Jozabad, Shimei, Kelaiah, Kelita, Pethahiah, Judah neh Eliezer.
24 Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
Laa sa rhoek lamloh Eliashib, thoh tawt lamloh Shallum, Telem neh Uri.
25 Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
Israel khuiah khaw Parosh koca lamloh Ramiah, Izziah, Malkhiah, Mijamin, Eleazar, Malkhiah neh Benaiah.
26 A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
Elam koca lamloh Mattaniah, Zekhariah, Jehiel, Abdi, Jerimoth neh Elijah.
27 A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
Zattu koca lamloh Elioenai, Eliashib, Mattaniah, Jerimoth, Zabad neh Aziza.
28 A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
Bebai koca lamloh Jehohanan, Hananiah, Zabbai neh Athlai.
29 A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
Bani koca lamloh Meshullam, Mallukh, Adaiah, Jashub, Sheal, Jerimoth neh Ramah.
30 A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
Pahathmoab koca lamloh Adna, Khelal, Benaiah, Maaseiah, Mattaniah, Bezalel, Binnui neh Manasseh.
31 A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
Harim koca ah Eliezer, Isshiah, Malkhiah, Shemaiah, Simeon.
32 Benjamini, Maluki ndi Semariya.
Benjamin, Mallukh neh Shemariah.
33 A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
Hashum koca lamloh Mattenai, Mattathah, Zabad, Eliphelet, Jeremai, Manasseh neh Shimei.
34 A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
Bani koca lamloh Maadai, Amram neh Uel.
35 Benaya, Bediya, Keluhi,
Benaiah, Bedeiah neh Keluhi kah Keluhi.
36 Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
Vaniah, Meremoth neh Eliashib.
37 Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
Mattaniah, Mattenai neh Jaasau.
38 A fuko la Binuyi anali Simei,
Bani, Binnui, Shimei.
39 Selemiya, Natani, Adaya,
Shelemiah, Nathan neh Adaiah.
40 Makinadebayi, Sasai, Sarai,
Macnadebai, Shashai neh Sharai.
41 Azaleli, Selemiya, Semariya,
Azarel, Shelemiah neh Shemariah.
42 Salumu, Amariya ndi Yosefe.
Shallum, Amariah neh Joseph.
43 A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
Nebo koca lamloh Jeiel, Mattithiah, Zabad, Zebina, Iddo, Joel neh Benaiah.
44 Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.
He rhoek boeih long he kholong nu a loh, a loh uh tih amih a yuu rhoek lamloh camoe a cun uh.

< Ezara 10 >