< Ezekieli 1 >

1 Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.
Or il arriva en la trentième année, au quatrième mois, au cinquième jour du mois, que lorsque j’étais au milieu des captifs, près du fleuve de Chobar, les deux furent ouverts, et je vis les visions de Dieu.
2 Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende,
Le cinquième du mois, c’est la cinquième année de la transmigration du roi Joachim,
3 Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.
La parole du Seigneur fut adressée à Ezéchiel, le prêtre, fils de Buzi, dans la terre des Chaldéens, près du fleuve de Chobar, et là fut sur lui la main du Seigneur.
4 Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira.
Et je vis, et voilà qu’un vent de tourbillon venait de l’aquilon; et une grande nuée, et un feu tournoyant, et une lumière éclatante tout autour, et du milieu, c’est-à-dire du milieu du feu, brillait comme une espèce de succin;
5 Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu
Et au milieu du feu la ressemblance ressemblance de quatre animaux; et voici leur aspect: la ressemblance d’un homme.
6 koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi.
Chacun d’eux avait quatre faces, et chacun d’eux quatre ailes.
7 Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira.
Leurs pieds étaient droits, et la plante de leurs pieds comme la plante du pied d’un veau, et il sortait d’eux des étincelles ayant l’apparence de l’airain le plus brillant.
8 Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko,
Et des mains d’hommes étaient sous leurs ailes aux quatre côtés; et ils avaient des faces et des ailes aux quatre côtés.
9 ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.
Et les ailes de l’un étaient jointes à celles de l’autre; ils ne se retournaient pas lorsqu’ils marchaient; mais chacun d’eux allait devant sa face.
10 Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga.
Quant à la ressemblance de leur visage, c’était une face d’homme et une face de lion, à la droite des quatre; mais une face de bœuf à la gauche des quatre, et une face d’aigle au-dessus des quatre.
11 Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake.
Leurs faces et leurs ailes s’étendaient en haut: ils se tenaient l’un l’autre par deux de leurs ailes, et ils couvraient leur corps par les deux autres;
12 Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita.
Et chacun d’eux marchait devant sa face; là où était l’impétuosité de l’esprit, là ils allaient; et ils ne se retournaient pas lorsqu’ils marchaient.
13 Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo.
Et la ressemblance des animaux et leur aspect étaient comme un feu de charbons ardents et comme un aspect de lampes. Voici ce qu’on voyait courir au milieu des animaux: l’éclat d’un feu, et la foudre sortant du feu.
14 Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.
Et les animaux allaient et revenaient, comme la foudre étincelante.
15 Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi.
Et comme je regardais les animaux, apparut sur la terre, près des animaux, une roue ayant quatre faces;
16 Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana.
Et l’aspect des roues et leur structure étaient comme la vue de la mer, et toutes quatre se ressemblaient: et leur aspect et leur structure étaient comme ceux d’une roue qui est au milieu d’une autre roue.
17 Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka.
Elles allaient constamment par leurs quatre côtés, et elles ne se retournaient pas lorsqu’elles marchaient.
18 Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.
Les roues avaient aussi une étendue, une hauteur et un aspect horrible; et tout le corps des quatre roues était plein d’yeux tout autour.
19 Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso.
Et lorsque les animaux marchaient, marchaient pareillement aussi les roues près d’eux; et lorsque les animaux s’élevaient de terre, s’élevaient en même temps aussi les roues.
20 Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija.
Partout où allait l’esprit, là allant l’esprit, les roues aussi pareillement s’élevaient en le suivant. Car l’esprit de vie était dans les roues.
21 Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.
Lorsque les animaux allaient, les roues allaient; lorsqu’ils s’arrêtaient, elles s’arrêtaient; lorsqu’ils s’élevaient de terre, pareillement s’élevaient aussi les roues, en les suivant; parce que l’esprit de vie était en elles.
22 Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake.
Et une ressemblance du firmament était au-dessus de la tête des animaux, comme l’aspect d’un cristal horrible et étendu en haut sur leurs têtes.
23 Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake.
Mais sous le firmament, leurs ailes étaient droites l’une vis-à-vis de l’autre; l’un avec deux de ses ailes voilait son corps, et l’autre semblablement se voilait.
24 Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.
Et j’entendais le bruit de leurs ailes comme le bruit des grandes eaux, comme la voix du Dieu très haut: quand ils marchaient, c’était comme le bruit d’une grande multitude, comme le bruit d’un camp; et quand ils s’arrêtaient, leurs ailes s’abaissaient.
25 Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake.
Car lorsque la voix se faisait entendre au-dessus du firmament qui était sur leurs têtes, ils s’arrêtaient et baissaient leurs ailes.
26 Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu.
Et sur ce firmament qui était suspendu au-dessus de leurs têtes, c’était comme l’aspect d’un saphir ressemblant à un trône; et sur cette ressemblance d’un trône, une ressemblance comme l’aspect d’un homme dessus.
27 Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo.
Et je vis comme une espèce de succin, comme l’apparence d’un feu, au dedans de lui tout autour; depuis ses reins et au-dessus, et depuis ses reins jusqu’en bas, je vis comme une espèce de feu, resplendissant tout autour.
28 Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula. Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.
Je vis comme l’aspect de l’arc, lorsqu’il est dans une nuée au jour de la pluie; tel était l’aspect de la splendeur tout autour.

< Ezekieli 1 >