< Ezekieli 9 >

1 Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
And he criede in myn eeris with greet vois, and seide, The visityngis of the citee han neiyed, and ech man hath in his hond an instrument of sleyng.
2 Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
And lo! sixe men camen fro the weie of the hiyere yate, that biholdith to the north, and the instrument of deth of ech man was in his hond; also o man in the myddis of hem was clothid with lynnun clothis, and a pennere of a writere at hise reynes; and thei entriden, and stoden bisidis the brasun auter.
3 Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
And the glorie of the Lord of Israel was takun vp fro cherub, which glorie was on it, to the threisfold of the hous; and the Lord clepide the man that was clothid with lynun clothis, and hadde a pennere of a writere in hise leendis.
4 ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
And the Lord seide to hym, Passe thou bi the myddis of the citee, in the myddis of Jerusalem, and marke thou Thau on the forhedis of men weilynge and sorewynge on alle abhomynaciouns that ben doon in the myddis therof.
5 Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
And he seide to hem in myn heryng, Go ye thorouy the citee, and sue ye hym, and smytte ye; youre iye spare not, nether do ye merci.
6 Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Sle ye til to deth, an eld man, a yong man, and a virgyn, a litil child, and wymmen; but sle ye not ony man, on whom ye seen Thau; and bigynne ye at my seyntuarie. Therfore thei bigunnen at the eldere men, that weren bifore the face of the hous.
7 Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
And he seide to hem, Defoule ye the hous, and fille ye the hallis with slayn men; go ye out. And thei yeden out, and killiden hem that weren in the citee.
8 Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
And lo! whanne the sleyng was fillid, Y was left. And Y felle doun on my face, and Y criede, and seide, Alas! alas! alas! Lord God, therfor whether thou schalt leese alle remenauntis of Israel, and schalt schede out thi stronge veniaunce on Jerusalem?
9 Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
And he seide to me, The wickidnesse of the hous of Israel and of Juda is ful greet, and the lond is fillid of bloodis, and the citee is fillid with turnyng awei; for thei seiden, The Lord hath forsake the lond, and the Lord seeth not.
10 Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
Therfor and myn iye schal not spare, nether Y schal do merci; Y schal yelde the weie of hem on the heed of hem.
11 Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”
And lo! the man that was clothid in lynun clothis, that hadde a pennere in his bak, answeride a word, and seide, Y haue do, as thou comaundidist to me.

< Ezekieli 9 >