< Ezekieli 8 >
1 Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
А шесте године, шестог месеца, дана петог, кад сеђах у својој кући и старешине Јудине сеђаху преда мном, паде онде на ме рука Господа Господа.
2 Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
И видех, а то облик на очи као огањ, од бедара Му доле беше огањ, а од бедара горе беше као светлост, као јака светлост.
3 Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
И пружи као руку, и ухвати ме за косу на глави, и подиже ме дух међу небо и земљу, и однесе ме у Јерусалим у утвари Божјој на врата унутрашња која гледају на север, где стајаше идол од ревности, који дражи на ревност.
4 Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
И гле, онде беше слава Бога Израиљевог на очи као она што је видех у пољу.
5 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
И рече ми: Сине човечји, подигни очи своје к северу. И подигох очи своје к северу, и гле, са севера на вратима олтарским беше онај идол од ревности на уласку.
6 Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
Потом ми рече: Сине човечји, видиш ли шта ти раде? Велике гадове које ту чини дом Израиљев да отидем далеко од светиње своје? Али ћеш још видети већих гадова.
7 Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
И одведе ме на врата од трема, и погледах, а то једна рупа у зиду.
8 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
А Он ми рече: Сине човечји, прокопај овај зид. И прокопах зид, а то једна врата.
9 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
Тада ми рече: Уђи и види опаке гадове које чине ту.
10 Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
И ушавши видех, и гле, свакојаке животиње што гамижу и свакојаки гадни скотови, и сви гадни богови дома Израиљевог беху написани по зиду свуда унаоколо.
11 Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
И пред њима стајаше седамдесет људи између старешина дома Израиљевог с Јазанијом, сином Сафановим, који стајаше међу њима, сваки с кадионицом својом у руци, и подизаше се густ облак од када.
12 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
Тада ми рече: Видиш ли, сине човечји, шта чине старешине дома Израиљевог у мраку свак у својој писаној клети? Јер говоре: Не види нас Господ, оставио је Господ ову земљу.
13 Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
Потом ми рече: Још ћеш видети већих гадова које они чине.
14 Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
И одведе ме на врата дома Господњег која су са севера; и гле, жене сеђаху и плакаху за Тамузом.
15 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
И рече ми: Јеси ли видео, сине човечји? Још ћеш видети већих гадова од тих.
16 Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
И одведе ме у трем унутрашњи дома Господњег; и гле, на уласку у цркву Господњу између трема и олтара беше око двадесет и пет људи окренутих леђима к цркви Господњој, лицем к истоку, и клањаху се сунцу према истоку.
17 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
Тада ми рече: Јеси ли видео, сине човечји? Мало ли је дому Јудином што чине те гадове које чине овде? Него још напунише земљу насиља и окренуше се да ме драже; и ето држе грану пред носом својим.
18 Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”
Зато ћу и ја учинити у гневу, неће жалити око моје, нити ћу се смиловати, и кад стану викати гласно у моје уши, нећу их услишити.