< Ezekieli 8 >
1 Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
C’Était dans la sixième année, le cinquième jour du sixième mois, j’étais assis dans ma maison et les anciens de Juda étaient assis en face de moi, quand s’abaissa là sur moi la main du Seigneur.
2 Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
Et je vis soudain une forme qui avait comme l’apparence d’un feu; depuis ce qui semblait ses reins jusqu’en bas. C’Était du feu, et depuis ses reins jusqu’en haut, cela apparaissait comme une splendeur, comme une sorte de hachmal.
3 Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
Et elle étendit une forme de main et me saisit par les tresses de ma tête et un souffle m’emporta entre terre et ciel et m’amena à Jérusalem dans des visions divines, à l’entrée de la porte intérieure qui regarde vers le Nord, où est placée l’idole de la jalousie irritante.
4 Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
Et il y avait là la gloire du Dieu d’Israël pareille à l’apparition que j’avais vue dans la Plaine.
5 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
Et il me dit: "Fils de l’homme, lève donc les yeux dans la direction du Nord;" je levai les yeux dans la direction du Nord, et voici que du côté du Nord, à la porte de l’autel, il y avait cette statue de la jalousie à l’entrée.
6 Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
Et il me dit: "Fils de l’homme, vois-tu ce qu’ils font, les grandes abominations que la maison d’Israël commet ici pour que je m’éloigne de mon sanctuaire? Et tu verras encore d’autres grandes abominations."
7 Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
Il me mena à l’entrée de la cour et je vis qu’il y avait un trou dans le mur.
8 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
Et il me dit: "Fils de l’homme, creuse donc dans le mur," et je creusai dans le mur, et voici qu’il y avait une entrée.
9 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
Et il me dit: "Entre et vois les exécrables abominations qu’ils commettent ici."
10 Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
J’Entrai et je vis qu’il y avait toutes les formes de reptiles et d’animaux immondes, et toutes les idoles de la maison d’Israël gravées sur le mur, tout alentour.
11 Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
Et soixante-dix hommes des anciens de la maison d’Israël, avec Yaazania, fils de Schafan, debout parmi eux, se tenaient devant elles, chacun son encensoir à la main, et un épais nuage d’encens s’élevait.
12 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
Et il me dit: "As-tu vu, fils de l’homme, ce que les anciens d’Israël font dans les ténèbres, chacun dans ses chambres d’images? Car, disent-ils, l’Eternel ne nous voit pas, l’Eternel a abandonné le pays!"
13 Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
Et il me dit: "Tu verras encore d’autres grandes abominations qu’ils commettent."
14 Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
Il me mena à l’entrée de la maison de l’Eternel qui regarde au nord, et voici que des femmes y étaient assises, pleurant le Tammouz.
15 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
Et il me dit: "As-tu vu, fils de l’homme? Tu verras encore des abominations plus grandes que celles-là."
16 Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
Il me fit entrer dans la cour intérieure de la maison de l’Eternel, et voici qu’à l’entrée du sanctuaire de l’Eternel, entre le parvis et l’autel, il y avait quelque vingt-cinq hommes qui avaient le dos tourné au sanctuaire de l’Eternel et la face vers l’Orient, et ils se prosternaient vers l’Orient devant le soleil.
17 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
Et il me dit: "As-tu vu, fils de l’homme? Est-ce trop peu de chose pour la maison de Juda de faire les abominations qu’ils ont faites ici, pour qu’ils remplissent le pays de violence et recommencent à m’irriter? Et voilà qu’ils portent les rameaux à leur nez.
18 Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”
Et moi aussi j’agirai avec colère, mon oeil ne sera pas indulgent et je n’aurai pas pitié; ils crieront à mes oreilles à grand bruit mais je ne les écouterai point."