< Ezekieli 8 >

1 Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
Now in the sixth year, in the sixth month, on the fifth day of the month, when I was in my house and the responsible men of Judah were seated before me, the hand of the Lord came on me there.
2 Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
And looking, I saw a form like fire; from the middle of his body and down there was fire: and up from the middle of his body a sort of shining, like electrum.
3 Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
And he put out the form of a hand and took me by the hair of my head; and the wind, lifting me up between the earth and the heaven, took me in the visions of God to Jerusalem, to the way into the inner door facing to the north; where was the seat of the image of envy.
4 Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
And I saw the glory of the Lord there, as in the vision which I saw in the valley.
5 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
Then he said to me, Son of man, now let your eyes be lifted up in the direction of the north; and on looking in the direction of the north, to the north of the doorway of the altar, I saw this image of envy by the way in.
6 Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
And he said to me, Son of man, do you see what they are doing? even the very disgusting things which the children of Israel are doing here, causing me to go far away from my holy place? but you will see other most disgusting things.
7 Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
And he took me to the door of the open place; and looking, I saw a hole in the wall.
8 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
And he said to me, Son of man, make a hole in the wall: and after making a hole in the wall I saw a door.
9 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
And he said to me, Go in and see the evil and disgusting things which they are doing here.
10 Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
So I went in and saw; and there every sort of living thing which goes flat on the earth, and unclean beasts, and all the images of the children of Israel, were pictured round about on the wall.
11 Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
And before them seventy of the responsible men of the children of Israel had taken their places, every man with a vessel for burning perfumes in his hand, and in the middle of them was Jaazaniah, the son of Shaphan; and a cloud of smoke went up from the burning perfume.
12 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
And he said to me, Son of man, have you seen what the responsible men of the children of Israel do in the dark, every man in his room of pictured images? for they say, The Lord does not see us; the Lord has gone away from the land.
13 Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
Then he said to me, You will see even more disgusting things which they do.
14 Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
Then he took me to the door of the way into the Lord's house looking to the north; and there women were seated weeping for Tammuz.
15 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
Then he said to me, Have you seen this, O son of man? you will see even more disgusting things than these.
16 Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
And he took me into the inner square of the Lord's house, and at the door of the Temple of the Lord, between the covered way and the altar, there were about twenty-five men with their backs turned to the Temple of the Lord and their faces turned to the east; and they were worshipping the sun, turning to the east.
17 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
Then he said to me, Have you seen this, O son of man? is it a small thing to the children of Judah that they do the disgusting things which they are doing here? for they have made the land full of violent behaviour, making me angry again and again: and see, they put the branch to my nose.
18 Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”
For this reason I will let loose my wrath: my eye will not have mercy, and I will have no pity.

< Ezekieli 8 >