< Ezekieli 7 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Потом дође ми реч Господња говорећи:
2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
Сине човечји, овако каже Господ Господ за земљу Израиљеву: Крај, дође крај на четири стране земљи.
3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Дође ти крај, и пустићу гнев свој на те, и судићу ти по путевима твојим и обратићу на те све гадове твоје.
4 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
И око моје неће те пожалити, нити ћу се смиловати, него ћу путеве твоје обратити на те, и гадови ће твоји бити усред тебе, и познаћете да сам ја Господ.
5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
Овако вели Господ Господ: Зло, једно зло, ево иде.
6 Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
Крај дође, крај дође, уста на те, ево дође.
7 Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
Дође јутро теби, становниче земаљски, дође време, приближи се дан, кад ће бити полом, а не јека горска.
8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
Сада ћу одмах излити јарост своју на те, и навршићу гнев свој на теби, и судићу ти по твојим путевима, и обратићу на те све гадове твоје.
9 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
Неће жалити око моје, нити ћу се смиловати, даћу ти по путевима твојим, и гадови ће твоји бити усред тебе, и познаћете да сам ја Господ, који бије.
10 “Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
Ево дана, ево дође, јутро наста, процвате прут, поноситост напупи.
11 Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
Насиље нарасте прут безакоња, нико неће остати од њих ни од мноштва њиховог ни од буке њихове, нити ће бити нарицања за њима.
12 Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
Дође време, приспе дан; ко купује нека се не радује, и ко продаје нека не жали, јер ће доћи гнев на све људство њихово.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
Јер ко продаје, неће опет доћи до оног што прода, ако и остане жив; јер утвара за све мноштво њихово неће се вратити натраг, и нико се неће окрепити безакоњем својим да сачува живот свој.
14 “Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
Затрубише у трубе, и спремише све; али нема никога да изађе у бој, јер се гнев мој распалио на све људство њихово.
15 Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
Напољу мач, а унутра помор и глад; ко буде у пољу, погинуће од мача; а ко буде у граду, њега ће глад и помор прождрети.
16 Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
А који их утеку, избавиће се и биће по горама као голубови из долина, сви ће уздисати, сваки за своје безакоње.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
Све ће руке клонути и сва ће колена постати као вода.
18 Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
И припасаће око себе кострет, и дрхат ће их попасти, и на сваком ће лицу бити стид, и све ће им главе бити ћелаве.
19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
Сребро ће своје побацати по улицама, и злато ће њихово бити као нечистота; сребро њихово и злато њихово неће их моћи избавити у дан гнева Господњег; неће наситити душе своје нити ће напунити трбуха свог, јер им је безакоње њихово спотицање.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
Јер славни накит свој обратише на охолост, и начинише од њега ликове гадова својих, гнусобе своје; зато учиних да им је нечистота.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
И даћу га у руке иностранцима да га разграбе, и безбожницима на земљи да је плен, и оскврниће га.
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
И одвратићу лице своје од њих, и оскврниће светињу моју, и ући ће у њу лупежи и оскврниће је.
23 “Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
Начини вериге, јер је земља пуна крвног суда, и град је пун насиља.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
Зато ћу довести најгоре између народа да наследе куће њихове, и укинућу охолост силних, и света места њихова оскврниће се.
25 Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
Иде погибао; они ће тражити мира, али га неће бити.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
Невоља за невољом долазиће, и глас за гласом стизаће; и они ће тражити утвару од пророка; закона ће нестати у свештеника и савета у стараца.
27 Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Цар ће тужити, и кнезови ће се обући у жалост, и руке народу земаљском дрхтаће; учинићу им по путевима њиховим и судићу им према судовима њиховим; и познаће да сам ја Господ.

< Ezekieli 7 >