< Ezekieli 7 >
1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
Et toi, fils d’un homme, voici ce que dit le Seigneur Dieu à la terre d’Israël: La fin vient, elle vient la fin sur les quatre côtés de la terre.
3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Maintenant la fin est sur toi, et j’enverrai ma fureur contre toi; et je te jugerai selon tes voies, et je poserai contre toi toutes tes abominations.
4 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Et mon œil ne t’épargnera pas, et je n’aurai pas de pitié; mais tes voies, je les poserai sur toi, et tes abominations seront au milieu de toi; et vous saurez que je suis le Seigneur.
5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Une affliction unique, une affliction, voici qu’elle vient.
6 Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
La fin vient, elle vient la fin, elle s’est éveillée contre toi; voici qu’elle vient.
7 Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
La ruine vient sur toi, qui habites la terre; il vient, le temps; il est près, le jour de la tuerie, et non de la gloire des montagnes.
8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
C’est maintenant de près que je répandrai ma colère sur toi, et que j’assouvirai ma fureur sur toi; et que je te jugerai selon tes voies; et que je t’imposerai tous tes crimes;
9 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
Et mon œil n’épargnera pas, et je n’aurai pas de pitié; mais tes voies, je te les imposerai; et tes abominations seront au milieu de toi; et vous saurez que moi je suis le Seigneur qui frappe.
10 “Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
Voici le jour, voici qu’il vient: la ruine est sortie, la verge a fleuri, l’orgueil a germé;
11 Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
L’iniquité s’est élevée sur la verge de l’impiété; il ne restera rien d’eux, ni du peuple, ni de leur bruit; et il n’y aura pas de repos pour eux.
12 Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
Il est venu le temps, il s’est approché le jour; que celui qui achète ne se réjouisse point; et que celui qui vend ne s’afflige pas, parce que la colère est sur tout son peuple.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
Parce que celui qui vend ne reviendra pas à ce qu’il a vendu, lors même qu’ils seraient encore au nombre des vivants; parce que la vision qui regarde tout le peuple ne reviendra pas sans être accomplie; et l’homme par l’iniquité ne sera pas affermi.
14 “Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
Sonnez de la trompette; que tous se préparent, et il n’est personne qui aille au combat; car ma colère est sur tout son peuple.
15 Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
Le glaive au dehors; et la peste et la famine au dedans; celui qui est dans la campagne mourra par l’épée; et ceux qui sont dans la cité seront dévorés par la peste et par la famine.
16 Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
Et seront sauvés ceux qui d’entre eux auront fui: mais ils seront sur les montagnes comme les colombes des vallées, tout tremblants, chacun dans son iniquité.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
Toutes les mains seront affaiblies, et l’eau coulera de tous les genoux.
18 Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
Et ils se revêtiront de cilices, et la frayeur les couvrira; sur toute face sera la confusion, et sur toutes les têtes la calvitie.
19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
Leur argent sera jeté dehors, et leur or sera comme du fumier. Leur argent et leur or ne pourront les délivrer au jour de la fureur du Seigneur; ils ne rassasieront pas leur âme, et leurs ventres ne seront pas remplis, parce que c’est devenu une pierre d’achoppement dans leur iniquité.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
Ils ont fait servir l’ornement de leurs colliers à leur orgueil; et ils en ont fait les images de leurs abominations et de leurs simulacres; à eau se de cela, je l’ai rendu pour eux un objet immonde;
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
Et je le livrerai aux mains des étrangers pour être pillé, et aux impies de la terre pour être leur proie; et ils le souilleront,
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
Et je détournerai ma face d’eux; et ils violeront mon secret; et des émissaires y entreront et le souilleront.
23 “Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
Fais la conclusion, parce que la terre est pleine de jugements de sang et que la cité est remplie d’iniquité.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
Et j’amènerai les plus méchants d’entre les nations, et ils posséderont leurs maisons; et je ferai cesser l’orgueil des puissants, et ces méchants posséderont leurs sanctuaires.
25 Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
L’angoisse survenant, ils chercheront la paix, et il n’y en aura pas.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
Trouble sur trouble viendra, et bruit sur bruit; ils chercheront quelque vision auprès d’un prophète, et la loi manquera au prêtre, et le conseil aux anciens.
27 Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Le roi sera en deuil, le prince sera couvert de tristesse, et les mains du peuple de la terre trembleront. Selon leur voie je leur rendrai, et selon leurs jugements je les jugerai; et ils sauront que je suis le Seigneur.