< Ezekieli 7 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Og Herrens Ord kom til mig, og han sagde:
2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
Og du Menneskesøn! saa siger den Herre, Herre om Israels Land: Der er Ende; Enden kommer over Landets fire Hjørner.
3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Nu forestaar Enden dig, og jeg vil sende min Vrede over dig og dømme dig efter dine Veje og lade dine Vederstyggeligheder falde tilbage paa dig.
4 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Og mit Øje skal ikke spare dig, og jeg vil ikke skaane; thi jeg vil lade dine Veje falde tilbage paa dig, og dine Vederstyggeligheder skulle blive i din Midte, og I skulle fornemme, at jeg er Herren.
5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
Saa siger den Herre, Herre: Ulykke, en eneste Ulykke, se, den kommer!
6 Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
Ende kommer! kommen er Enden, den er vaagnet op imod dig; se, den kommer.
7 Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
Morgenen kommer til dig, du Landets Indbygger! Tiden kommer; Forstyrrelsens Dag er nær, og der er intet Frydeskrig paa Bjergene.
8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
Nu snart vil jeg udøse min Harme over dig og fuldkomme min Vrede paa dig og dømme dig efter dine Veje og lade alle dine Vederstyggeligheder falde tilbage paa dig.
9 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
Og mit Øje skal ikke spare, og jeg vil ikke skaane; jeg vil lade dine Veje falde tilbage paa dig, og dine Vederstyggeligheder skulle blive i din Midte, og I skulle fornemme, at jeg er Herren, som slaar.
10 “Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
Se Dagen! se, den kommer! Morgenen bryder frem, Riset blomstrer, Hovmodigheden skyder op.
11 Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
Vold rejser sig til et Ris over Ugudelighed; der bliver intet tilovers af dem; og intet af deres Mangfoldighed, og intet af deres Mængde, og intet herligt iblandt dem!
12 Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
Tiden kommer, Dagen er kommen nær, den, som køber, glæde sig ej, og den, som sælger, sørge ej; thi Vreden naar hele dens Mangfoldighed.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
Thi den, som sælger, skal ikke komme til sit solgte Gods igen, om og hans Liv er iblandt de levende; thi Synet angaaende hele dens Mangfoldighed tages ej tilbage, og ingen skal styrke sit Liv ved sin Misgerning.
14 “Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
Man blæser i Trompeten og gør alt rede, men der drager dog ingen ud til Krigen; thi min Vrede naar hele dens Mangfoldighed.
15 Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
Sværdet udenfor og Pesten og Hungeren indenfor! den, som er paa Marken, skal dø for Sværdet, og den, som er i Staden, skulle Hunger og Pest fortære.
16 Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
Og undkomme nogle undkomne af dem, skulle de være paa Bjergene som Duer i Dalene, sukkende alle, hver for sin Misgernings Skyld.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
Alle Hænder skulle synke og alle Knæ ryste som Vand.
18 Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
Og de skulle iføre sig Sæk, og Rædsel skal betage dem, Skam skal komme over alle Ansigter og Skaldethed over alle deres Hoveder.
19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
De skulle kaste deres Sølv paa Gaderne, og deres Guld skal være dem til Modbydelighed; deres Sølv og deres Guld skal ikke kunne fri dem paa Herrens Vredes Dag, de skulle ikke kunne mætte deres Sjæl og ej fylde deres Indvolde dermed; thi det var dem Anstød til at synde.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
Som stadseligt Smykke brugte de det til Hoffærdighed og gjorde deraf deres Vederstyggeligheders Billeder, deres Grueligheder; derfor gjorde jeg dem til Modbydelighed.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
Og jeg vil give det i de fremmedes Haand som Rov og til de ugudelige paa Jorden som Bytte, at de kunne vanhellige det.
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
Og jeg vil vende mit Ansigt bort fra dem, og de skulle vanhellige min Skat; og Røvere skulle komme derind og vanhellige den.
23 “Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
Gør Lænken færdig! thi Landet er fuldt af Blodskyld og Staden fuld af Vold.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
Og jeg vil lade de værste iblandt Hedningerne komme, og de skulle indtage deres Huse til Ejendom; og jeg vil gøre Ende paa de stærkes Hovmodighed, og deres Helligdomme skulle vanhelliges.
25 Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
Ødelæggelse kommer; og de skulle søge Fred, og den skal ikke findes.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
Ulykke over Ulykke skal komme, og Rygte over Rygte skal opstaa; og de skulle søge efter et Syn hos en Profet; men Loven skal være borte for Præsten, og Raad for de gamle.
27 Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Kongen skal sørge, og Fyrsten skal iføre sig Forfærdelse, og Hænderne paa Folket i Landet skulle ryste; jeg vil handle med dem efter deres Veje og dømme dem efter deres Domme, og de skulle fornemme, at jeg er Herren.

< Ezekieli 7 >