< Ezekieli 7 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
При това, Господното слово дойде към мене и казваше:
2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
А ти, сине човешки, слушай. Така казва Господ Иеова към Израилевата земя: Край! краят дойде На четирите краища на страната.
3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Сега е дошъл краят върху тебе; Защото ще изпратя гнева Си върху тебе, Ще те съдя според постъпките ти, И ще възвърна върху тебе всичките ти мерзости.
4 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Окото ми не ще те пощади, Нито ще ти покажа милост; Но ще възвърна върху тебе постъпките ти, И въздаянията ти за твоите мерзости ще бъдат всред тебе; И ще познаете, че Аз съм Господ.
5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
Така казва Господ Бог Иеова: Зло, едно небивало зло, ето, иде;
6 Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
Краят дойде, краят дойде, Бди против тебе; ето, настъпи.
7 Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
Присъдата ти дойде върху тебе, който живееш в тая земя; Времето дойде, денят наближи, Ден на смущение по планините, а не на възклицание.
8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
Сега скоро ще излея върху тебе яростта Си, И ще изчерпя гнева Си върху тебе; Ще те съдя според постъпките ти, И ще възвърна върху тебе всичките ти мерзости,
9 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
Окото Ми няма да пощади, Нито ще покажа милост; Ще ти въздам според постъпките ти, И въздаянията за твоите мерзости ще бъдат всред тебе; И вие ще познаете, че Аз, Който ви поразявам, съм Господ.
10 “Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
Ето, денят, ето, иде! Твоята присъда се яви! Жезълът се разцъфтя, гордостта поникна!
11 Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
Насилието порасна в тояга за беззаконието им; Нищо не ще остане от тях, Нито от това множество, Нито от имота им; И няма да остане великолепие между тях.
12 Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
Времето дойде, денят наближи; Който купува, да се не радва; И който продава, да не жали; Защото има гняв върху цялото това множество.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
Защото продавачът няма да притежава наново продаденото от него, Ако и да е останал жив; Понеже видението относно цялото това множество няма да се отмени, Нито ще утвърди някой себе си Чрез беззаконния си живот.
14 “Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
Затръбиха и приготвиха всичко, Но никой не отива на боя; Защото Моят гняв е върху цялото това множество.
15 Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
Ножът е вън, а морът и гладът вътре; Който е на нивата ще умре от нож; А който е в града, глад и мор ще го погълнат.
16 Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
А ония от тях, които избягнат, като се избавят Ще бъдат по планините като гълъбите по долините, Всичките плачещи, всеки за беззаконието си.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
Всички ръце ще ослабват, И всички колена ще станат като вода.
18 Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
Ще се препашат с вретище, И ужас ще ги покрие; Срам ще има по лицата на всичките, И плешивост по главите на всички тях.
19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
Среброто си ще хвърлят по улиците, И златото им ще им бъде като нечисто нещо; Среброто и златото им не ще могат да ги избавят В деня на гнева Господен; Те няма да наситят душите си, нито да напълнят червата си; Защото о тях се спънаха и паднаха в беззаконието си.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
Господ постави славното Си украшение, за да се гордеят с него; Но те направиха в него образите на своите мерзости, На омразните си идоли; Затова, Аз го обръщам в нещо нечисто за тях.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
Ще го предам в ръцете на чужденци за плячка, И на нечестивите на земята за корист; И те ще го омърсят;
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
И като отвърна лицето Си от тях, Те ще омърсят светилището Ми, И грабители ще влязат в него и ще го омърсят.
23 “Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
Направи верига; Защото земята е пълна с кървави престъпления, И градът е пълен с насилие.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
Затова, ще докарам най-злите от народите, И те ще се завладеят къщите им; Ще направя да престане и гордостта на силните; И светите им места ще се омърсят.
25 Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
Погибел иде; Ще потърсят мир, но не ще има.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
Бедствие след бедствие ще дохожда, И слух след слух ще пристига; Тогава ще поискат видение от пророк; Но поуката ще се изгуби от свещеника, И съветът от старейшините.
27 Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Царят ще жалее, Първенецът ще се облече в смайване, И ръцете на людете на страната ще ослабват. Според постъпките им ще им направя, И според заслужването им ще ги съдя; И ще познаят, че Аз съм Господ.

< Ezekieli 7 >