< Ezekieli 6 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Опет ми дође реч Господња говорећи:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
Сине човечји, окрени лице своје према горама Израиљевим, и пророкуј против њих,
3 kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
И реци: Горе Израиљеве, чујте реч Господа Господа, овако вели Господ Господ горама и хумовима, потоцима и долинама: Ево ме, ја ћу пустити на вас мач и оборићу висине ваше.
4 Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
И ваши ће се олтари раскопати, и сунчани ликови ваши изломиће се, и поваљаћу побијене ваше пред гадним боговима вашим.
5 Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
И побацаћу мртва телеса синова Израиљевих пред гадне богове њихове, и разметнућу кости ваше око олтара ваших.
6 Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
Свуда где наставате градови ће се опустошити и висине ће опустети, и олтари ће се ваши раскопати и опустети, и гадни богови ваши изломиће се и неће их више бити, и сунчани ликови ваши исећи ће се, и дела ће се ваша уништити.
7 Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
И побијени ће падати усред вас, и познаћете да сам ја Господ.
8 “Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
Али ћу вас оставити неколико који би утекли од мача међу народима кад се расијете по земљама.
9 Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
И који од вас побегну, опоменуће се мене међу народима, где буду у ропству, како ми дотужаше срцем својим курварским које одступи од мене, и очима својим курварским, којима идоше за гадним боговима својим, и сами ће себи бити мрски за зла која чинише у свим градовима својим.
10 Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
И познаће да сам ја Господ и да нисам говорио узалуд да ћу им учинити то зло.
11 “Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
Овако вели Господ Господ: Пљесни рукама и лупи ногом, и реци: Јаох! Ради свих гадних зала дома Израиљевог, јер ће пасти од мача, од глади и од помора.
12 Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
Ко буде далеко, умреће од помора; а ко буде близу, пашће од мача; а ко остане и буде опкољен, умреће од глади; тако ћу навршити гнев свој на њима.
13 Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
И познаћете да сам ја Господ кад буду побијени њихови међу гадним боговима њиховим, око олтара њихових, на сваком високом хуму и на свим врховима горским и под сваким зеленим дрветом и под сваким гранатим храстом, свуда где су кадили угодним мирисима свим гадним боговима својим.
14 Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Јер ћу замахнути руком својом на њих, и обратићу земљу њихову у пустош гору од пустиње Дивлате по свим становима њиховим; и познаће да сам ја Господ.

< Ezekieli 6 >