< Ezekieli 6 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
و کلام خداوند بر من نازل شده، گفت:۱
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
«ای پسر انسان نظر خود را بر کوههای اسرائیل بدوز و درباره آنها نبوت کن.۲
3 kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
و بگو: ای کوههای اسرائیل کلام خداوند یهوه را بشنوید! خداوند یهوه به کوهها و تلها و وادیها و دره هاچنین می‌فرماید: اینک من شمشیری بر شمامی آورم و مکان های بلند شما را خراب خواهم کرد.۳
4 Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
و مذبح های شما منهدم و تمثالهای شمسی شما شکسته خواهد شد و کشتگان شمارا پیش بتهای شما خواهم‌انداخت. و لاشهای بنی‌اسرائیل را پیش بتهای ایشان خواهم گذاشت و استخوانهای شما را گرداگرد مذبح های شما خواهم پاشید.۴
5 Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
۵
6 Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
و در جمیع مساکن شما شهرهاخراب و مکان های بلند ویران خواهد شد تا آنکه مذبح های شما خراب و ویران شود و بتهای شماشکسته و نابود گردد و تمثالهای شمسی شمامنهدم و اعمال شمامحو شود.۶
7 Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
و چون کشتگان شما در میان شما بیفتند، آنگاه خواهی دانست که من یهوه هستم.۷
8 “Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
اما بقیتی نگاه خواهم داشت. وچون در میان کشورها پراکنده شوید، بقیه السیف شما در میان امت‌ها ساکن خواهند شد.۸
9 Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
ونجات‌یافتگان شما در میان امت‌ها در جایی که ایشان را به اسیری برده‌اند مرا یاد خواهند داشت. چونکه دل زناکار ایشان را که از من دور شده است خواهم شکست و چشمان ایشان را که در عقب بتهای ایشان زنا کرده است - پس خویشتن را به‌سبب اعمال زشتی که در همه رجاسات خودنموده‌اند مکروه خواهند داشت.۹
10 Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
و خواهنددانست که من یهوه هستم و عبث نگفتم که این بلارا بر ایشان وارد خواهم آورد.»۱۰
11 “Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
خداوند یهوه چنین می‌گوید: «به‌دست خود بزن و پای خود را بر زمین بکوب و بگو: وای بر تمامی رجاسات و شریر خاندان اسرائیل زیراکه به شمشیر و قحط و وباخواهد افتاد.۱۱
12 Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
آنکه دور باشد به وبا خواهد مرد و آنکه نزدیک است به شمشیر خواهد افتادو آنکه باقی‌مانده و درمحاصره باشد از گرسنگی خواهد مرد و من حدت خشم خود را بر ایشان به اتمام خواهم رسانید.۱۲
13 Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
و خواهید دانست که من یهوه هستم، هنگامی که کشتگان ایشان در میان بتهای ایشان به اطراف مذبح های ایشان، بر هر تل بلند و برقله های تمام کوهها و زیر هر درخت سبز و زیر هر بلوط کشن، در جایی که هدایای خوشبو برای همه بتهای خود می‌گذرانیدند یافت خواهند شد.۱۳
14 Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
و دست خود را بر ایشان دراز کرده، زمین را درتمام مسکن های ایشان خرابتر و ویرانتر از بیابان دبله خواهم ساخت. پس خواهند دانست که من یهوه هستم.»۱۴

< Ezekieli 6 >