< Ezekieli 6 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Un Tā Kunga vārds notika uz mani sacīdams:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
Cilvēka bērns! Griez savu vaigu pret Israēla kalniem un sludini pret tiem
3 kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
Un saki: Israēla kalni, klausāties Tā Kunga Dieva vārdu! Tā saka Tas Kungs Dievs uz kalniem un pakalniem, uz upēm un ielejām: redzi! Es vedu pār jums zobenu un izdeldu jūsu elku altārus.
4 Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
Un jūsu altāri taps nopostīti un jūsu saules stabi nolauzti, un es gāzīšu jūsu nokautos jūsu elku priekšā.
5 Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
Un Es nodošu Israēla bērnu trūdus viņu elku priekšā un kaisīšu jūsu kaulus ap jūsu altāriem.
6 Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
Visur, kur jūs mājojat, pilsētas būs postītas un elku kalni atstāti, jo jūsu altāri būs sagāzti un nopostīti un jūsu elki būs salauzti un izdeldēti, un jūsu saules stabi tiks nocirsti un jūsu darījumi iznīcināti.
7 Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
Un jūsu vidū gulēs nokauti, un jūs samanīsiet, ka Es esmu Tas Kungs.
8 “Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
Bet Es (kādus) atlicināšu, ka jums paliek, kas zobenam izmūk starp pagāniem, kad jūs tapsiet izkaisīti pa zemēm.
9 Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
Tad jūsu izglābtie mani pieminēs starp pagāniem, kur tie būs cietumā, kad Es būšu salauzis viņu mauku sirdis, kas no Manis atkāpušās, un viņu acis, kas mauko pakaļ viņu elkiem, un tiem riebsies tas ļaunums, ko tie darījuši visās savās negantībās.
10 Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
Un tiem būs samanīt, ka Es esmu Tas Kungs; Es nebūt neesmu velti runājis, ka viņiem darīšu šo ļaunumu.
11 “Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
Tā saka Tas Kungs Dievs: sasit savas rokas un sit ar kāju pie zemes un sauc: ak vai! Pār visām niknām Israēla nama negantībām, jo tie kritīs caur zobenu, caur badu un caur mēri.
12 Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
Kas tālu, tas kritīs caur mēri, un kas tuvu, tas kritīs caur zobenu, bet kas atliksies un izglābsies, nomirs badā. Tā Es pret tiem izdarīšu savu bardzību.
13 Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
Tad jūs samanīsiet, ka Es esmu Tas Kungs, kad viņu nokautie gulēs viņu elku priekšā ap viņu altāriem pa visiem augstiem pakalniem, pa visiem kalnu galiem un apakš visiem zaļiem kokiem un apakš visiem kupliem ozoliem, tais vietās, kur tie saldu smaržu upurēja visiem saviem elkiem.
14 Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Un Es izstiepšu savu roku pār viņiem, un darīšu zemi par postažu un tuksnesi vairāk nekā Diblas tuksnesi, visur, kur viņi mājo; un tie samanīs, ka Es esmu Tas Kungs.

< Ezekieli 6 >