< Ezekieli 6 >
1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Og Herrens ord kom til mig således:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
Menneskesøn, vend dit Ansigt mod Israels Bjerge, profeter imod dem
3 kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
og sig: Israels Bjerge, hør den Herre HERRENs Ord! Så siger den Herre HERREN til Bjergene og Højene, til Kløfterne og Dalene: Se, jeg sender Sværd over eder og tilintetgør eders Offerhøje.
4 Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
Eders Altre skal ødelægges, eders Solstøtter sønderbrydes, og eders dræbte lader jeg segne foran eders Afgudsbilleder;
5 Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
jeg kaster Israeliternes Lig hen for deres Afgudsbilleder og strør eders Ben rundt om eders Altre.
6 Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
Overalt hvor I bor, skal Byerne lægges øde og Offerhøjene gå til Grunde, for at eders Altre kan lægges øde og gå til Grunde, eders Afudsbilleder sønderbrydes og udryddes, eders Solstøtter hugges om og eders Værker tilintetgøres.
7 Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
Mandefald skal ske iblandt eder, og I skal kende, at jeg er HERREN.
8 “Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
Men en Rest lader jeg blive tilbage, idet nogle af eder undslipper fra Sværdet blandt Folkene, når I spredes i Landene,
9 Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
og de undslupne skal komme mig i Hu blandt Folkene, hvor de er Fanger; jeg sønderbryder deres bolerske Hjerter, som faldt fra mig, og deres bolerske Øjne, som hang ved deres Afgudsbilleder; og de skal væmmes ved sig selv over alt det onde, de har gjort, over alle deres Vederstyggeligheder.
10 Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
Og de skal kende, at jeg er HERREN; det var ikke tomme Ord, når jeg talede om at gøre den Ulykke på dem.
11 “Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
Så siger den Herre HERREN: Slå Hænderne sammen, stamp med Foden og råb Ve over alle Israels Huses grimme Vederstyggeligheder! De skal falde for Sværd, Hunger og Pest.
12 Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
Den, som er langt borte, skal dø af Pest; den, som er nær, skal falde for Sværd; og den, som levnes og reddes, skal dø af Hunger; således udtømmer jeg min Vrede over dem.
13 Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
De skal kende, at jeg er HERREN, når deres dræbte ligger midt iblandt deres Afgudsbilleder rundt om deres Altre på hver høj Bakke, på alle Bjergenes Tinder, under hvert grønt Træ og hver løvrig Eg, der, hvor de opsendte liflig Duft til deres Afgudsbilleder.
14 Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Jeg udrækker Hånden imod dem og gør Landet øde og tomt lige fra Ørkenen til Ribla, overalt hvor de bor; og de skal kende, at jeg er HERREN.