< Ezekieli 5 >

1 Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
Wena-ke, ndodana yomuntu, zithathele ingqamu ebukhali, zithathele impuco yabageli, uyihambise phezu kwekhanda lakho laphezu kwesilevu sakho; ubusuzithathela isikali sokulinganisa, wehlukanise inwele.
2 Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
Ingxenye yesithathu uzayitshisa ngomlilo phakathi komuzi sezigcwalisekile insuku zokuvimbezela; uthathe ingxenye yesithathu utshaye inhlangothi zonke zayo ngenkemba; lengxenye yesithathu uyihlakaze emoyeni; njalo ngizahwatsha inkemba emva kwabo.
3 Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
Njalo uzathatha ezinlutshwana ngenani kuzo, uzigoqele emaphethelweni ezembatho zakho.
4 Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
Ubusuthatha kuzo futhi, uziphosele phakathi komlilo, uzitshise emlilweni; kuzaphuma kuwo umlilo uye kuyo yonke indlu kaIsrayeli.
5 Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
Itsho njalo iNkosi uJehova: Le yiJerusalema; ngiyimisile phakathi kwezizwe lamazwe inhlangothi zonke zayo.
6 Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
Kodwa iphendule izahlulelo zami zaba yibubi okwedlula izizwe, lezimiso zami okwedlula amazwe ayihanqileyo; ngoba bazalile izahlulelo zami, lezimiso zami kabahambanga kuzo.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Ngoba leyisile okwedlula izizwe ezilihanqileyo, lingahambanga ezimisweni zami, lingazenzanga izahlulelo zami, lingenzanga njengokwezahlulelo zezizwe ezilihanqileyo;
8 “Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, ngimelene lawe, ngitsho mina, njalo ngizakwenza izahlulelo phakathi kwakho, emehlweni ezizwe.
9 Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
Ngenze phakathi kwakho engingazange ngikwenze, lengingasayikukwenza okunjengakho, ngenxa yamanyala akho wonke.
10 Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
Ngakho oyise bazakudla amadodana phakathi kwakho, lamadodana azakudla oyise. Njalo ngizakwenza izahlulelo phakathi kwakho, lensali yakho yonke ngizayihlakaza kuwo wonke umoya.
11 Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
Ngakho, kuphila kwami, itsho iNkosi uJehova, isibili, ngoba ungcolisile indawo yami engcwele ngazo zonke izinengiso zakho langamanyala akho wonke, ngakho lami ngizakunciphisa, futhi ilihlo lami kaliyikuhawukela, futhi lami kangiyikuyekela.
12 Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
Ingxenye yesithathu yakho izakufa ngomatshayabhuqe wesifo, langendlala bazaqedwa phakathi kwakho; lengxenye yesithathu izakuwa ngenkemba enhlangothini zonke zakho; lengxenye yesithathu ngizayihlakaza kuwo wonke umoya, ngihwatshe inkemba emva kwabo.
13 “Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
Ngokunjalo ukuthukuthela kwami kuzapheleliswa, ngenze ukufutheka kwami kuphumule phezu kwabo, ngiduduzeke; njalo bazakwazi ukuthi mina iNkosi ngikhulumile ekutshisekeni kwami, lapho sengiphelelise ukufutheka kwami kubo.
14 “Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
Futhi ngizakwenza ube lunxiwa ube lihlazo phakathi kwezizwe ezikuhanqileyo, emehlweni akhe wonke owedlulayo.
15 Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
Ngakho kuzakuba lihlazo, lenhlekisa, imfundiso, lesesabiso ezizweni ezikuhanqileyo nxa ngisenza izahlulelo phakathi kwakho ngolaka langokufutheka langokukhuza kokufutheka; mina Nkosi ngikhulumile.
16 Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
Lapho ngithumela phezu kwabo imitshoko emibi yendlala, ezakuba ngeyokubhubhisa, engizayithumela ukulibhubhisa, ngizakwandisa indlala phezu kwenu, ngephule udondolo lwesinkwa kini.
17 Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”
Ngokunjalo ngizathuma phezu kwenu indlala lezilo ezimbi, ezizakwemuka abantwana; lomatshayabhuqe wesifo legazi kudabule phakathi kwakho; ngilethe inkemba phezu kwakho. Mina Nkosi ngikhulumile.

< Ezekieli 5 >