< Ezekieli 5 >

1 Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
And thou, son of man, take thee a sharp instrument, even a barber's razor, and cause it to pass upon thy head and thy beard; and take thee weighing-balances, and divide the hair.
2 Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
A third part shalt thou burn with fire in the midst of the city, when the days of the siege are fulfilled; and thou shalt take a third part and smite it round about with the sword; and a third part shalt thou scatter in the wind, and I will draw out a sword after them.
3 Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
Thou shalt also take thereof a small number, and bind them in thy skirts.
4 Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
And of these again take some and cast them into the fire, and burn them in the fire. From them shall a fire come forth upon the whole house of Israel.
5 Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
Thus saith the Lord Jehovah: This is Jerusalem; in the midst of the nations have I set her, and countries are round about her.
6 Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
But she hath wickedly resisted my ordinances more than the nations, and my statutes more than the countries, that are round about her. For they have refused my ordinances, and have not walked in my statutes.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
Therefore thus saith the Lord Jehovah: Because ye have been rebellious more than the nations that are round about you, and have not walked in my statutes, nor kept my ordinances, but have done according to the ordinances of the nations which are round about you,
8 “Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
therefore thus saith the Lord Jehovah: Behold I, even I, am against thee, and will execute judgments against thee in the sight of the nations.
9 Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
I will do to thee that which I have not yet done, and the like of which I shall not do again, because of all thine iniquities.
10 Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
Therefore the fathers shall eat the sons in the midst of thee, and the sons shall eat their fathers; and I will execute judgments in thee, and I will scatter the whole remnant of thee to all the winds.
11 Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
Therefore, as I live, saith the Lord Jehovah, because thou hast polluted my sanctuary with all thy detestable things, and with all thine abominations, therefore will I also withdraw mine eye from thee; neither will I spare, neither will I have any pity.
12 Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
A third part of thee shall die by the pestilence, or be consumed with hunger in the midst of thee; and a third part shall die by the sword round about thee; and a third part will I scatter to all the winds, and I will draw out a sword after them.
13 “Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
Thus shall mine anger be accomplished, and I will satiate my fury upon them, and receive satisfaction; and they shall know that I, Jehovah, have spoken it in my zeal, when I shall have accomplished my fury upon them.
14 “Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
Moreover, I will make thee a waste, and a reproach among the nations that are round about thee, in the sight of all that pass by.
15 Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
And thou shalt be a reproach, and a reviling, and a warning, and an astonishment to the nations that are round about thee, when I shall execute judgments upon thee in anger, and in fury, and in furious rebukes; —I, Jehovah, have spoken it; —
16 Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
when I shall send upon you the evil arrows of famine which bring destruction, which I send to destroy you, and increase the famine upon you, and break your staff of bread.
17 Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”
And I will send upon you famine, and evil beasts, which shall make thee childless; and pestilence and blood shall pass through thee; and the sword will I bring upon thee. I, Jehovah, have spoken it.

< Ezekieli 5 >