< Ezekieli 5 >
1 Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
Hlang capa nang samvo taengkah cunghang paihat aka haat te namah ham lo laeh. Te te namah ham lo lamtah na lu neh na hmuimul khaw vo laeh. Te phoeiah namah ham cooi khiing khueh lamtah boek.
2 Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
Vongup khohnin a thok neh pathum ah pakhat te khopuei laklung ah hmaipuei neh kolh. Pathum ah pakhat te lo lamtah a kaepvai ah cunghang neh tloek. Te phoeiah pathum ah pakhat khohli dongla haeh. Amih hnukah cunghang ka khoh bitni.
3 Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
Tedae te khui lamloh a sii ngai te bet lo lamtah na hnirhaep ah kaelh.
4 Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
Te lamkah te koep lo lamtah hmai khui la voei. Te te hmai neh hoeh lamtah te lamkah hmai te Israel imkhui pum la pak saeh.
5 Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
Ka Boeipa Yahovah loh he ni a. thui. Jerusalem he namtom lakli ah a kaepvai kah khohmuen neh ka khueh.
6 Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
Tedae ka laitloeknah he namtom lakah, ka khosing te khaw a kaepvai kah kho rhoek lakah halangnah neh a koek. Ka laitloeknah te a hnawt uh tih ka khosing dongah pongpa uh pawh.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
Te dongah ka Boeipa Yahovah loh he ni a. thui. Na kaepvai kah namtom lakah na hlangping dongah nim ka khosing dongah na pongpa uh pawt tih ka laitloeknah he na vai uh pawh. Na kaepvai namtom kah laitloeknah banglam pataeng na vai uh moenih.
8 “Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
Te dongah ka Boeipa Yahovah loh he ni a. thui. Kai kamah khaw nang kam pai thil coeng. Namtom mikhmuh kah laitloeknah neh na laklo ah ka saii ni.
9 Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
Nang kah tueilaehkoi cungkuem dongah ka saii vai pawt te nang taengah ka saii vetih te bang te koep ka saii mahpawh.
10 Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
Te dongah na khui kah napa rhoek loh a ca rhoek, ca rhoek loh napa rhoek a caak uh ni. Na soah tholhphu kan suk vetih na meet boeih te khohli cungkuem taengla ka haeh ni.
11 Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
Te dongah he tah ka Boeipa Yahovah kah olphong ni. Kai hingnah ni. Ka rhokso te namah kah sarhingkoi cungkuem neh, namah kah tueilaehkoi cungkuem neh na poeih het pawt nim? Te dongah ka hlaek vaengah ka mik loh rhen pawt vetih lungma ka ti van mahpawh.
12 Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
Nang taengkah te hlopthum ah hlopkhat, duektahaw ah duek uh vetih na khui ah khokha loh a khah ni. Na kaepvai kah Hlopthum ah hlopkhat te cunghang dongah cungku uh ni. Pathum ah khohli cungkuem taengla ka haeh vetih amih hnukah cunghang ka khoh ni.
13 “Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
Te daengah ni amih taengkah ka thintoek a daeh neh ka kosi ka hlam vetih dam ka ti eh. Te vaengah BOEIPA kamah loh ka kosi he amih soah ka sah phoeiah khaw ka thatlainah neh ka voek te a ming uh bitni.
14 “Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
Te phoeiah na kaepvai kah aka pongpa boeih mikhmuh neh namtom taengah nang te imrhong la, kokhahnah la kang khueh ni.
15 Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
Kai loh nang soah tholhphu te thintoek neh, kosi neh kan saii vaengah na kaepvai kah namtom taengah kokhahnah neh hnaelcoenah, thuituennah neh a rhaerhap la om bitni. Te dongah BOEIPA kamah loh kosi kah toelthamnah nen ni ka thui.
16 Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
Amih taengah yoethae khokha thaltang te ka kah ni. Nangmih aka phae ham te te ka kah te kutcaihnah lam ni a. om. Te dongah nang soah khokha kang koei vetih nangmih kah thahuelnah buh te ka bawt ni.
17 Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”
Nangmih taengah khokha neh boethae mulhing kan tueih vetih nangmih te cakol la n'khueh ni. Duektahaw neh thii loh nang te m'pah vetih na taengah cunghang kang khuen ni. BOEIPA kamah long ni ka thui.