< Ezekieli 46 >
1 “Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
Esto es lo que el Señor ha dicho: la puerta del atrio interior que mira hacia el este debe cerrarse los seis días hábiles; pero el sábado debe estar abierto, y en el momento de la luna nueva, debe estar abierto.
2 Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
Y el gobernante debe entrar por el pórtico de la puerta exterior, y tomar su lugar junto al umbral de la puerta, y los sacerdotes harán su ofrenda quemada y sus ofrendas de paz, y él rendirá culto en el umbral de la puerta; luego saldrá y la puerta no se cerrará hasta la tarde.
3 Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
Y la gente de la tierra debe adorar en la puerta de esa puerta delante del Señor en los sábados y en las lunas nuevas.
4 Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
Y la ofrenda quemada ofrecida al Señor por el gobernante en el día de reposo debe ser de seis corderos sin defecto en ellos y un carnero sin defecto;
5 Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
Y la ofrenda de cereales debe ser un efa para las ovejas, y para los corderos lo que sea capaz de dar, y un hin de aceite por un efa.
6 Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
Y en el momento de la luna nueva, será un becerro de la manada sin defecto en él, y seis corderos y un carnero, todos sin defecto:
7 Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
Y él debe dar una ofrenda de comida, un efa por el becerro y un efa por las ovejas, y para los corderos todo lo que pueda dar, y un hin de aceite por un efa.
8 Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
Y cuando el gobernante entra, debe entrar por el pórtico de la puerta, y debe salir por el mismo camino.
9 “Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
Pero cuando la gente de la tierra se presenta ante el Señor en las fiestas fijas, el que entra por la puerta norte para adorar debe salir por la puerta sur; y el que entra por la puerta sur debe salir por la puerta norte; no debe volver por la puerta por la que entró, sino que debe ir directamente delante de él.
10 Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
Y el gobernante, cuando entran, debe entrar con ellos, y debe salir con ellos cuando salen.
11 “Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
En las fiestas y las reuniones fijas, las ofrendas de cereales deben ser un efa por un becerro, y un efa para un carnero, y para los corderos lo que sea capaz de dar, y un hin de aceite para un efa.
12 Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
Y cuando el gobernante hace una ofrenda gratuita, una ofrenda quemada o una ofrenda de paz dada gratuitamente al Señor, la puerta que mira al este debe abrirse para él, y él debe hacer su ofrenda quemada y sus ofrendas de paz como lo hace en el día de reposo, luego saldrá; y la puerta se cerrará después de que salga.
13 “Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
Y debes dar un cordero de un año de edad sin defecto para una ofrenda quemada al Señor todos los días; de mañana a mañana, debes darlo.
14 Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
Y cada mañana, debes dar una ofrenda de cereal con ella, una sexta parte de un efa y una tercera parte de un hin de aceite para humedecer la flor de harina; Una ofrenda de cereal ofrecida al Señor en todo momento por un orden eterno.
15 Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
Y deben dar el cordero y la ofrenda de cereal y el aceite, siempre por la mañana, por una ofrenda quemada continuamente.
16 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
Esto es lo que el Señor Dios ha dicho: si el gobernante le da una propiedad a cualquiera de sus hijos, es su herencia y será propiedad de sus hijos; Es de ellos por su herencia.
17 Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
Y si él da una parte de su herencia a uno de sus siervos, será suyo hasta el año de la liberación, y luego regresará al gobernante; porque es herencia de sus hijos, y será de ellos.
18 Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
Y el gobernante no debe tomar la herencia de ninguna de las personas, expulsándolas de sus propiedades; él debe dar una herencia a sus hijos de la propiedad que es suya, para que mi pueblo no pueda ser expulsado de su propiedad.
19 Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
Y me llevó por el camino al lado de la puerta hacia las habitaciones consagradas a los sacerdotes, mirando hacia el norte; y vi un lugar al lado de ellas hacia el oeste.
20 Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
Y él me dijo: Este es el lugar donde los sacerdotes deben cocinar la ofrenda por la culpa y la ofrenda por el pecado, y donde la ofrenda de cereales debe cocinarse en el horno para que no puedan ser sacados a la plaza exterior para santificar a la gente.
21 Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
Y me sacó a la patio exterior y me hizo pasar por los cuatro ángulos del patio; y vi que en cada ángulo del patio había un patio cerrado.
22 Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
En los cuatro ángulos había espacios amurallados, de cuarenta codos de largo y treinta de ancho; Los cuatro eran del mismo tamaño.
23 Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
Y había una línea de muro alrededor de ellos, alrededor de los cuatro, y se hicieron chimeneas debajo de las paredes todo alrededor.
24 Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”
Y me dijo: Estos son los cuartos de ebullición, donde los ministros hervirán la ofrenda del pueblo.