< Ezekieli 46 >
1 “Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
Така казва Господ Иеова: Портата на вътрешния двор, която гледа към изток, нека бъде затворена през шестте делнични дни; а в съботния ден да се отваря, и в деня на новолунието да се отваря.
2 Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
И князът нека влезе по пътя на предверието на външната порта, и нека застане при стълба на портата; а свещениците нека принасят всеизгарянето му и примирителните му приноси; и той да се поклони при прага на портата. Тогава да излезе; обаче да се не затваря портата до вечерта.
3 Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
А людете на Израилевата земя да се кланят във входа на същата порта пред Господа в съботите и в новолунията.
4 Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
А всеизгарянето, което князът ще принася Господу в съботен ден да бъде шест агнета без недостатък и един овен без недостатък.
5 Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
И хлебният принос за овена да бъде една ефа, а хлебният принос за агнетата колкото му дава ръка, и един ин дървено масло за една ефа.
6 Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
И в деня на новолунието приносът му да бъде юнец без недостатък, шест агнета, и един овен, които да бъдат без недостатък.
7 Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
И нека принася хлебен принос, една ефа за юнеца, и една ефа за овена, а за агнетата, колкото му стига ръка, и по един ин дървено масло за всяка ефа.
8 Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
И когато князът влиза, нека влиза по пътя на предверието на портата, и нека излиза по същия път.
9 “Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
Но когато людете на тая земя дохождат пред Господа във време на определените празници, тогава оня, който влиза по пътя на северната порта, за да се поклони, нека излиза по пътя на южната порта, а който влиза по пътя на южната порта, нека излиза по пътя на северната порта; да се не връща по пътя на портата, по който е влязъл, но да излиза като върви право напред.
10 Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
И князът да влиза всред тях, когато влизат; и когато излизат, да излизат заедно.
11 “Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
И на тържествата и на празниците хлебният принос да бъде една ефа за юнеца, и една ефа за овена; а за агнетата, колкото му дава ръка, и един ин дървено масло за всяка ефа.
12 Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
А когато князът принася доброволно всеизгаряне или доброволни примирителни приноси Господу, тогава да му отварят портата, която гледа към изток, и нека принася всеизгарянето си и примирителните си приноси както прави в съботен ден; тогава нека излиза; и подир излизането му нека затварят портата.
13 “Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
И да принасяш всеки ден във всеизгаряне Господу едногодишно агне без недостатък; всяка сутрин да го принасяш.
14 Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
И заедно с него да принасяш всяка сутрин за хлебен принос шестата част от една ефа, и третата част от един ин дървено масло, за да го смесиш с брашното; това да бъде хлебен принос Господу за винаги чрез вечна наредба.
15 Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
Така нека принасят агнето, хлебния принос, и дървеното масло всяка сутрин, за всегдашно всеизгаряне.
16 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
Така казва Господ Иеова: Ако князът даде подарък на някого от синовете си, това ще му бъде наследство, ще бъде притежание на неговите синове, ще им бъде притежание по наследство.
17 Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
Но ако даде подарък от наследството си на някого от слугите си, тогава ще бъде негов само до годината на освобождението, подир която да се възвръща на княза; а наследството му ще бъде за синовете му.
18 Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
При това, князът да не взема от наследството на людете като ги извежда с насилие от притежанието им; ако даде наследството на синовете си, то от своето притежание да им даде, за да се не разпръсват людете Ми всеки от притежанието си.
19 Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
После ме заведе през входа, който бе от страните на портата, в светите свещенически стаи, които гледат към север; и, ето, там имаше място отзад към запад.
20 Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
И рече ми: Това е мястото гдето свещениците ще варят приноса за престъпление и приноса за грях, и гдето ще пекат хлебния принос, за да не ги изнасят във външния двор и да осветят людете.
21 Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
Тогава като ме изведе във външния двор, преведе ме около четирите ъгъла на двора; и, ето, във всеки ъгъл на двора имаше двор.
22 Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
В четирите ъгъла на двора имаше заградени дворове, четиридесет лакти на длъж и тридесет на шир; тия четири двора в ъглите имаха еднаква мярка.
23 Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
И имаше ред здания наоколо в тях, около четирите двора; имаше готварници устроени наоколо под редовете.
24 Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”
Тогава ми каза: Тия са готварниците, дето служителите на дома ще варят жертвите на людете.