< Ezekieli 45 >

1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
Och när I genom lottkastning fördelen landet till arvedel, då skolen I åt HERREN giva en offergärd, en helig del av landet, i längd tjugufem tusen alnar och i bredd tio tusen; detta stycke skall vara heligt till hela sitt omfång runt omkring.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
Härav skall tagas till helgedomen en liksidig fyrkant, fem hundra alnar i längd och fem hundra i bredd, runt omkring, och till utmark där runt omkring femtio alnar.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
Av det tillmätta stycket skall du alltså avmäta ett område, tjugufem tusen alnar i längd och tio tusen i bredd; där skall helgedomen, det högheliga, ligga.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
Detta skall vara en helig del av landet, och det skall tillhöra prästerna, som göra tjänst i helgedomen, dem som få träda fram till att göra tjänst inför HERREN; detta skall vara en plats åt dem för deras hus, så ock en helig plats för helgedomen.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
Och ett stycke, tjugufem tusen alnar i längd och tio tusen i bredd, skall tillhöra leviterna, som göra tjänst i huset, såsom deras besittning, med tjugu tempelkamrar.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
Och åt staden skolen I giva till besittning ett område, fem tusen alnar i bredd och tjugufem tusen i längd, motsvarande det heliga offergärdsområdet; det skall höra hela Israels hus till.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
Och fursten skall på båda sidor om det heliga offergärdsområdet och stadens besittning få ett område, beläget invid det heliga offergärdsområdet och stadens besittning, dels på västra sidan, västerut, dels ock på östra sidan, österut, och I längd motsvarande en stamlotts utsträckning från västra gränsen till östra.
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
Detta skall han hava till sitt land, till besittning i Israel. Och mina furstar skola då icke mer förtrycka mitt folk, utan skola låta Israels hus få behålla sitt land efter sina stammar.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Så säger Herren, HERREN: Nu må det vara nog, I Israels furstar. Skaffen bort våld och förtryck, och öven rätt och rättfärdighet; hören upp att driva mitt folk ifrån hus och hem, säger Herren, HERREN.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
Riktig våg, riktig efa, riktigt bat-mått skolen I hava.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
Efan och bat-måttet skola hålla samma mått, så att bat-måttet rymmer tiondedelen av en homer, och likaledes efan tiondedelen av en homer; ty efter homern skall man bestämma måtten.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
Sikeln skall innehålla tjugu gera; tjugu siklar, tjugufem siklar, femton siklar skall minan innehålla hos eder.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
Detta är den offergärd I skolen giva: en sjättedels efa av var homer vete och en sjättedels efa av var homer korn;
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
vidare den stadgade gärden av olja, räknat efter bat av olja: en tiondedels bat av var kor (som är ett mått på tio bat och lika med en homer, ty tio bat utgöra en homer);
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
vidare av småboskapen från Israels betesmarker ett djur på vart tvåhundratal, till spisoffer, brännoffer och tackoffer, för att bringa försoning för folket, säger Herren, HERREN.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
Allt folket i landet skall vara förpliktat till denna offergärd åt fursten i Israel.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
Men fursten skall det åligga att frambära brännoffer, spisoffer och drickoffer på festerna, nymånaderna och sabbaterna, vid alla Israels hus' högtider. Han skall anskaffa syndoffer, spisoffer, brännoffer och tackoffer till att bringa försoning för Israels hus.
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
Så säger Herren, HERREN: På första dagen i första månaden skall du taga en felfri ungtjur och rena helgedomen.
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
Och prästen skall taga något av syndoffrets blod och stryka på husets dörrpost och på altaravsatsens fyra hörn och på dörrposten till den inre förgårdens port.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
Så skall du ock göra på sjunde dagen i månaden, om så är, att någon har syndat ouppsåtligen och av fåkunnighet; på detta sätt skolen I bringa försoning för huset.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
På fjortonde dagen i första månaden skolen I fira påskhögtid; i sju dagar skolen I hålla högtid, och man skall då äta osyrat bröd.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
På den dagen skall fursten för sig själv och för allt folket i landet offra en tjur till syndoffer.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
Men sedan, under högtidens sju dagar, skall han dagligen under de sju dagarna offra såsom brännoffer åt HERREN sju tjurar och sju vädurar, alla felfria, och såsom syndoffer en bock dagligen.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
Och såsom spisoffer skall han offra en efa till var tjur och en efa till var vädur, jämte en hin olja till var efa.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
På femtonde dagen i sjunde månaden skall han vid högtiden frambära likadana offer under de sju dagarna, likadana syndoffer, brännoffer och spisoffer och lika mycket olja.

< Ezekieli 45 >